< Hiob 13 >

1 “Mʼani ahu eyinom nyinaa, mʼaso ate, na ate ase.
“Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
2 Nea wunim no, me nso minim; wonyɛ abomfiaa mma me.
Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
3 Nanso mepɛ sɛ mekasa kyerɛ Otumfo no na mekyerɛkyerɛ mʼasɛm mu kyerɛ Onyankopɔn.
Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
4 Mode atoro mmom na asra me ho; mo nyinaa moyɛ ayaresafo a munsi hwee!
Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
5 Sɛ mobɛyɛ komm koraa a ɛno na ɛbɛyɛ nyansa ama mo!
Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
6 Afei muntie mʼano asɛm; muntie mʼanoyi.
Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
7 Mobɛka amumɔyɛsɛm ama Onyankopɔn ana? Mobɛka nnaadaasɛm ama no ana?
Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
8 Mobɛkyea mo aso ama no? Mobɛka Onyankopɔn asɛm ama no ana?
Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
9 Sɛ ɔhwehwɛ mo mu a, ebesi mo yiye ana? Mubetumi adaadaa no sɛnea modaadaa nnipa no ana?
Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
10 Sɛ mokyeaa mo aso wɔ kokoa mu a, sɛnea ɛte biara, ɔbɛka mo anim
Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
11 Nʼanuonyam mmɔ mo hu ana? Ne ho suro ntɔ mo so ana?
Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
12 Mo kasatɔmmɛ yɛ mmɛbu a ɛte sɛ nsõ; mo anoyi yɛ dɔte twann anoyi.
Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
13 “Monyɛ komm mma menkasa; na nea ɛbɛyɛ me biara mmra me so.
“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
14 Adɛn nti na mede me ho to amane mu na mede me nkwa to me nsam?
Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
15 Ɛwɔ mu sɛ okum me de, nanso ne so na mʼani bɛda; ampa ara medi mʼakwan ho adanse wɔ nʼanim.
Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
16 Nokware, eyi na ɛbɛyɛ me nkwagye, efisɛ nea onsuro Onyankopɔn no rentumi nkɔ nʼanim!
Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
17 Muntie me nsɛm yi yiye; monyɛ aso mma nea meka.
Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
18 Afei a masiesie me nkurobɔ yi, minim sɛ medi bem.
Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
19 Obi betumi abɔ me kwaadu ana? Sɛ ɛte saa de a, anka mɛyɛ komm na mawu.
Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
20 “Onyankopɔn, yɛ saa nneɛma abien yi pɛ ma me, na afei meremfa me ho nhintaw wo:
“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
21 Yi wo nsa fi me so kɔ akyirikyiri, na gyae wo ho hu a wode hunahuna me no.
Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
22 Ɛno de, samena me na mɛba, anaa ma menkasa na bua me.
Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
23 Mfomso ne bɔne dodow ahe na mayɛ? Kyerɛ me me mfomso ne me bɔne.
Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
24 Adɛn nti na wode wʼanim asie me na wudwen sɛ meyɛ wo tamfo?
Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
25 Wobɛyɛ ahaban a mframa rebɔ no ayayade ana? Wobɛtaa ntɛtɛ a awo ana?
Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
26 Wokyerɛw sobo a ɛyɛ yaw tia me, na woka me mmabunmmere mu bɔne nyinaa gu me so.
Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
27 Wode nkyehama gu mʼanan; wohwɛ mʼanammɔnkwan nyinaa so yiye na wode agyiraehyɛde ayeyɛ mʼanammɔn mu.
Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
28 “Enti onipa nkwa sa te sɛ ade a aporɔw, te sɛ atade a nwewee adi.
“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

< Hiob 13 >