< Zaburi 82 >
1 Zaburi ya Asafu. Mungu anaongoza kusanyiko kuu, anatoa hukumu miongoni mwa “miungu”:
Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
2 “Hata lini utaendelea kuwatetea wasio haki na kuonyesha upendeleo kwa waovu?
“Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
3 Teteeni wanyonge na yatima, tunzeni haki za maskini na walioonewa.
Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4 Mwokoeni mnyonge na mhitaji, wakomboeni kutoka mkononi mwa mwovu.
Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
5 “Hawajui lolote, hawaelewi lolote. Wanatembea gizani; misingi yote ya dunia imetikisika.
“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6 “Nilisema, ‘Ninyi ni “miungu”; ninyi nyote ni wana wa Aliye Juu Sana.’
“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7 Lakini mtakufa kama wanadamu wa kawaida; mtaanguka kama mtawala mwingine yeyote.”
Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
8 Ee Mungu, inuka uihukumu nchi, kwa kuwa mataifa yote ni urithi wako.
Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.