< Ayubu 25 >

1 Ndipo Bildadi Mshuhi akajibu:
Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 “Mamlaka na kuheshimiwa ni vyake Mungu; yeye huthibitisha amani katika mbingu juu.
“Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
3 Je, majeshi yake yaweza kuhesabika? Ni nani asiyeangaziwa na nuru yake?
Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
4 Mtu awezaje kuwa mwadilifu mbele za Mungu? Awezaje mtu aliyezaliwa na mwanamke kuwa safi?
Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
5 Ikiwa hata mwezi sio mwangavu nazo nyota si safi machoni pake,
Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
6 sembuse mtu ambaye ni funza: mwanadamu ambaye ni buu tu!”
nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”

< Ayubu 25 >