< Proverbios 26 >

1 Honrar a un tonto es tan inoportuno como la nieve en el verano, o la lluvia durante la cosecha.
Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 La maldición no caerá sobre la persona que no la merece. Será como el ave o la golondrina que revolotean.
Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 Los caballos necesitan un látigo, los asnos necesitan un freno. ¡Del mismo modo, los tontos necesitan vara en sus lomos!
Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 No respondas al tonto según su estupidez, o terminarás igual que ellos.
Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 No respondas al tonto según su estupidez, o pensaran que son sabios.
Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 Confiar la entrega de un mensaje en manos de un tonto, es como cortar tus pies o beber veneno.
Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 Un proverbio dicho por un tonto es tan inútil como las piernas de un inválido.
Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 Honrar a un tonto es tan inútil como tratar de atar una piedra a una honda.
Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 Un proverbio dicho por un tonto es tan ridículo como ver a un borracho entre espinos.
Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 Todo el que contrata a un tonto o a un desconocido errante, es como un arquero que hiere a la gente lanzando flechas al azar.
Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 Los tontos repiten su estupidez, así como un perro vuelve a comer su vomito.
Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 ¡Has visto a un hombre sabio en su propia opinión? ¡Hay más esperanza para un tonto que para él!
Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 Los perezosos son los que dicen: “¡Hay un león en el camino, un león por las calles!”
Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 El perezoso se voltea en la cama, como la puerta se recuesta en sus bisagras.
Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 Los perezosos extienden su mano hasta el plato, pero están demasiado cansados como para llevarse la comida a la boca.
Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 Los perezosos son más sabios en su propia opinión que muchos consejeros prudentes.
Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 Tomar parte en la disputa de otra persona es como agarrar a un perro callejero por las orejas.
Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
18 Serás como un loco lanzando flechas con fuego y matando gente
Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 si mientes a tu amigo, para luego decirle que era una broma.
ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 Sin madera, el fuego se apaga, y sin chismosos, se acaba la discordia.
Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 Una persona conflictiva aumenta la discordia, como poner carbón en brasas, o madera en el fuego.
Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 Escuchar chismes es como tragar bocados de tu comida preferida. Llegan hasta lo más profundo.
Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 La persuación con intenciones malvadas es como un esmalte brillante de plomo en una olla de barro.
Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 La gente te adulará aunque te odien. En el fondo te mienten.
Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 Cuando las personas sean buenas contigo, no les creas. Su mente está llena de odio hacia ti.
Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 Aunque su odio esté oculto detrás de su astucia, su maldad quedará expuesta delante de todos.
Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 Aquellos que cavan fosos para hacer caer a otros, terminarán cayendo ellos mismos. Y los que hacen rodar piedras, quedarán aplastados por ellas.
Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 Si mientes, muestras odio por las víctimas de tus mentiras. Si halagas a las personas, causarás desastre.
Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.

< Proverbios 26 >