< Приче Соломонове 1 >
1 Приче Соломуна сина Давидовог, цара Израиљевог,
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 Да се познаје мудрост и настава, да се разумеју речи разумне,
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 Да се прима настава у разуму, у правди, у суду и у свему што је право,
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 Да се даје лудима разборитост, младићима знање и помњивост.
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 Мудар ће слушати и више ће знати, и разуман ће стећи мудрост,
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 Да разуме приче и значење, речи мудрих људи и загонетке њихове.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 Почетак је мудрости страх Господњи; луди презиру мудрост и наставу.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Слушај, сине, наставу оца свог, и не остављај науке матере своје.
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 Јер ће бити венац од милина око главе твоје, и гривна на грлу твом.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Сине мој, ако би те мамили грешници, не пристај;
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 Ако би рекли: Ходи с нама да вребамо крв, да заседамо правоме низашта;
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 Прождрећемо их као гроб живе, и свеколике као оне који силазе у јаму; (Sheol )
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
13 Свакојаког блага добићемо, напунићемо куће своје плена;
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Бацаћеш жреб свој с нама; један ће нам тоболац бити свима;
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 Сине мој, не иди на пут с њима, чувај ногу своју од стазе њихове.
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 Јер ногама својим трче на зло и хите да проливају крв.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Јер се узалуд разапиње мрежа на очи свакој птици;
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 А они вребају своју крв и заседају својој души.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Такви су путеви свих лакомих на добитак, који узима душу својим господарима.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 Премудрост виче на пољу, на улицама пушта глас свој;
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 У највећој вреви виче, на вратима, у граду говори своје беседе;
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 Луди, докле ћете љубити лудост? И подсмевачима докле ће бити мио подсмех? И безумни, докле ће мрзети на знање?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Обратите се на карање моје; ево, изасућу вам дух свој, казаћу вам речи своје.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Што звах, али не хтесте, пружах руку своју, али нико не мари,
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 Него одбацисте сваки савет мој, и карање моје не хтесте примити;
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 Зато ћу се и ја смејати вашој невољи, ругаћу се кад дође чега се бојите;
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 Кад као пустош дође чега се бојите, и погибао ваша као олуја кад дође, кад навали на вас невоља и мука.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Тада ће ме звати, али се нећу одазвати; рано ће тражити, али ме неће наћи.
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Јер мрзише на знање, и страх Господњи не изабраше;
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 Не присташе на мој савет, и презираше сва карања моја.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Зато ће јести плод од путева својих, и наситиће се савета својих.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Јер ће луде убити мир њихов, и безумне ће погубити срећа њихова.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Али ко ме слуша боравиће безбрижно, и биће на миру не бојећи се зла.
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”