< 4 Мојсијева 29 >

1 А седмог месеца први дан да имате свети сабор; посао ропски ниједан не радите; то да вам је трубни дан.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 И принесите жртву паљеницу за мирис угодни Господу, једно теле, једног овна, седам јагањаца од године здравих;
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 А дар уз њих белог брашна смешаног с уљем три десетине уз теле и две десетине уз овна,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 И по једну десетину уз свако јагње од седам јагањаца;
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 И једног јарца за грех, ради очишћења вашег;
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 Осим жртве паљенице у почетку месеца и дара њеног, и осим свагдашње жртве паљенице и дара њеног и налива њихових по уредби њиховој, за мирис угодни, за жртву огњену Господу.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 И десети дан тог месеца седмог да имате свети сабор; и мучите душе своје; не радите никакав посао;
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 Него принесите Господу за мирис угодни жртву паљеницу, једно теле, једног овна, седам јагањаца од године, а нека вам је здраво;
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 И дар уз њих белог брашна помешаног с уљем три десетине уз теле, две десетине уз овна,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 По једну десетину уза свако јагње од оних седам јагањаца;
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 Јарца једног за грех, осим жртве за грех ради очишћења, и осим свагдашње жртве паљенице и дара њеног и налива њихових.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 И петнаести дан тог месеца седмог да имате свети сабор; ниједан посао ропски не радите; него празнујте празник Господу седам дана.
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 И принесите жртву паљеницу, огњену жртву за угодни мирис Господу, тринаест телаца, два овна, четрнаест јагањаца од године, а нека су здрави;
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 И дар уз њих брашна белог смешана с уљем по три десетине уза свако теле од тринаест телаца, по две десетине уза сваког овна од она два овна,
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 И по једну десетину уза свако јагње од оних четрнаест јагањаца;
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 И једног јарца за грех, осим свагдашње жртве паљенице и дара њеног и налива њеног.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 А други део дванаест телаца, два овна, четрнаест јагањаца од године здравих,
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 И дар њихов и налив њихов, уз теоце, уз овнове и уз јагањце, по броју њиховом, како је уређено;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 И јарца једног за грех, осим свагдашње жртве паљенице и дара њеног и налива њеног.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 А трећи дан једанаест телаца, два овна и четрнаест јагањаца од године здравих;
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 И дарове њихове и наливе њихове, уз теоце, уз овнове и уз јагањце, по броју њиховом, како је уређено;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 И једног јарца за грех, осим свагдашње жртве паљенице и дара њеног и налива њеног.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 А четврти дан десет телаца, два овна, четрнаест јагањаца од године здравих;
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 И дар њихов и наливе њихове, уз теоце, уз овнове и уз јагањце, по броју њиховом, како је уређено;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 И једног јарца за грех, осим свагдашње жртве паљенице и дара њеног и налива њеног.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 А пети дан девет телаца, два овна, четрнаест јагањаца од године здравих;
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 И дар њихов и наливе њихове, уз теоце, уз овнове и уз јагањце, по броју њиховом, како је уређено;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 И једног јарца за грех, осим свагдашње жртве паљенице и дара њеног и налива њеног.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 А шести дан осам телаца, два овна, четрнаест јагањаца од године здравих,
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 И дар њихов и наливе њихове, уз теоце, уз овнове и уз јагањце, по броју њиховом, како је уређено;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 И једног јарца за грех, осим свагдашње жртве паљенице и дара њеног и налива њеног.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 А седми дан седам телаца, два овна, четрнаест јагањаца од године здравих,
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 И дар њихов и наливе њихове, уз теоце, уз овнове и уз јагањце, по броју њиховом, како је уређено;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 И јарца за грех, осим свагдашње жртве паљенице и дара њеног и налива њеног.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 А осми дан да вам је празник; ниједан посао ропски не радите.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 Него принесите жртву паљеницу, жртву огњену за угодни мирис Господу, једно теле, једног овна, седам јагањаца од године здравих.
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 И дар њихов и наливе њихове, уз теле, уз овна и уз јагањце, по броју њиховом, како је уређено;
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 И једног јарца за грех, осим свагдашње жртве паљенице и дара њеног и налива њеног.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 То приносите Господу на празнике своје, осим оног што бисте по завету или од своје воље принели за жртве паљенице или дарове или наливе или жртве захвалне.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 И каза Мојсије синовима Израиљевим све што заповеди Господ.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< 4 Мојсијева 29 >