< Књига пророка Михеја 6 >
1 Слушајте шта говори Господ: Устани, суди се с горама, и нека чују хумови глас твој.
Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
2 Слушајте, горе и тврди темељи земаљски, парбу Господњу, јер Господ има парбу с народом својим, и с Израиљем се суди.
Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
3 Народе мој, шта сам ти учинио? И чим сам ти досадио? Одговори ми.
“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
4 Јер те изведох из земље мисирске и искупих из куће ропске и послах пред тобом Мојсија, Арона и Марију.
Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
5 Народе мој, опомени се шта науми Валак цар моавски и шта му одговори Валам, син Веоров, од Ситима до Галгала шта би, да познаш правду Господњу.
Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
6 Са чим ћу доћи пред Господа да се поклоним Богу Вишњем? Хоћу ли доћи преда Њ са жртвама паљеницама? С теоцима од године?
Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
7 Хоће ли Господу бити миле хиљаде овнова? Десетине хиљада потока уља? Хоћу ли дати првенца свог за преступ свој? Плод утробе своје за грех душе своје?
Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
8 Показао ти је, човече, шта је добро; и шта Господ иште од тебе осим да чиниш што је право и да љубиш милост и да ходиш смерно с Богом својим?
Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
9 Глас Господњи виче граду, и ко је мудар види име твоје; слушајте прут и Оног који га је одредио.
Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
10 Није ли јоште у кући безбожниковој благо неправо? И ефа крња, гадна?
Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
11 Хоће ли ми бити чист у кога су мерила лажна и у тобоцу преварно камење?
Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
12 Јер су богатуни његови пуни неправде, и становници говоре лаж, и у устима им је језик преваран.
Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
13 Зато ћу те и ја бити да оболиш, пустошићу те за грехе твоје.
Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
14 Ти ћеш јести, али се нећеш наситити, и падање твоје биће усред тебе; и склањаћеш, али нећеш избавити, и што избавиш предаћу мачу.
Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
15 Ти ћеш сејати, али нећеш жети; ти ћеш цедити маслине, али се нећеш намазати уљем, и маст, али нећеш пити вино.
Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
16 Јер се држе уредбе Амријеве и сва дела дома Ахавовог, и ходите по саветима њиховим, да те предам у погибао, и становнике његове у подсмех, и носићете срамоту народа мог.
Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”