< Књига пророка Јеремије 35 >
1 Реч која дође Јеремији од Господа у време Јоакима, сина Јосијиног цара Јудиног, говорећи:
Yehova anayankhula ndi Yeremiya nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, kuti:
2 Иди к дому синова Рихавових и говори с њима, те их доведи у дом Господњи, у коју клет, и подај им вино, нека пију.
“Pita ku banja la Arekabu ndipo ukawayitane kuti abwere mʼchipinda chimodzi cha Nyumba ya Yehova ndipo akafika uwapatse vinyo kuti amwe.”
3 Тада узех Јазанију, сина Јеремије, сина Ховасијиног и браћу његову и све синове и сав дом синова Рихавових.
Choncho ndinakatenga Yaazaniya (mwana wa Yeremiya winanso amene anali mwana wa Habaziniya), abale ake, ana ake onse aamuna ndi banja lonse la Arekabu.
4 И доведох их у дом Господњи, у клет синова Анана сина Игдалијиног човека Божијег, која је до клети кнезовске, над клећу Масије сина Салумовог, вратара.
Ndinabwera nawo ku Nyumba ya Yehova, ku chipinda cha ophunzira a mneneri Hanani mwana wa Igidaliya, munthu wa Mulungu. Chipinda chimenechi chinali pafupi ndi chipinda cha akuluakulu, chimene chinali pamwamba pa chipinda cha Maaseya mwana wa Salumu, mlonda wa pa khomo.
5 И метнух пред синове дома Рихавовог крчаге пуне вина, и чаше, па им рекох: Пијте вино.
Kenaka ndinayika mabotolo odzaza ndi vinyo ndi zikho zake pamaso pa Arekabu ndipo ndinawawuza kuti, “Imwani vinyoyu.”
6 А они рекоше: Нећемо пити вино, јер Јонадав, син Рихавов, отац наш забранио нам је рекавши: Не пијте вино, ни ви ни синови ваши до века;
Koma iwo anayankha kuti, “Ife sitimwa vinyo, chifukwa kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula kuti, ‘Inuyo ngakhale zidzukulu zanu, musadzamwe vinyo mpaka kalekale.
7 И куће не градите, ни семена сејте, ни винограда садите нити га држите, него у шаторима живите свега века свог, да бисте дуго живели на земљи, где сте дошљаци.
Musadzamange nyumba kapena kufesa mbewu, kapena kulima minda ya mpesa; musadzakhale ndi zinthu zimenezi. Mʼmalo mwake muzidzakhale mʼmatenti. Mukadzatero mudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukukhalamo.’
8 И послушасмо глас Јонадава, сина Рихавовог оца свог, у свему што нам заповеди да не пијемо вино свега века свог, ни ми ни наше жене, ни синови наши ни кћери наше,
Ife takhala tikumvera zonse zimene kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula. Ife ngakhale akazi athu kapena ana athu aamuna ndi aakazi sitinamwepo vinyo
9 Ни да градимо кућа да у њима живимо, ни да имамо винограда ни њиве ни усева.
kapena kumanga nyumba kuti tizikhalamo kapenanso kukhala ndi minda ya mpesa, minda ina iliyonse kapena mbewu.
10 Него живимо у шаторима, и слушамо и чинимо све како нам је заповедио Јонадав, отац наш.
Koma takhala mʼmatenti ndipo tamvera kwathunthu chilichonse chimene kholo lathu Yehonadabu anatilamula.
11 А кад дође Навуходоносор, цар вавилонски, у ову земљу, рекосмо: Хајде да отидемо у Јерусалим испред војске халдејске и војске сирске; и тако остасмо у Јерусалиму.
Koma pamene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anathira nkhondo dziko lino, ife tinati, ‘Tiyeni tichoke, tipite ku Yerusalemu kuti tithawe magulu ankhondo a Akasidi ndi Aaramu.’ Kotero ife takhala tikukhala mu Yerusalemu.”
12 Тада дође реч Господња Јеремији говорећи:
Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya kuti,
13 Овако вели Господ над војскама Бог Израиљев: Иди реци Јудејцима и Јерусалимљанима: Зар нећете да примите науке да слушате речи моје? Говори Господ.
“Iyeyu, Yehova Mulungu wa Israeli anawuza Yeremiya kuti: Pita ukawawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Kodi simungatengeko phunziro ndi kumvera mawu anga?’ akutero Yehova.
14 Извршују се речи Јонадава, сина Рихавовог, који забрани синовима својим да не пију вино, и не пију вино до данас, него слушају заповест оца свог; а ја вам говорих зарана једнако, а ви ме не послушасте.
‘Yehonadabu mwana wa Rekabu analamula ana ake kuti asamwe vinyo ndipo lamulo limeneli alisunga. Mpaka lero lino iwo samwa vinyo, chifukwa akumvera lamulo la kholo lawo. Koma Ine ndakhala ndikuyankhula nanu kawirikawiri kukuchenjezani, koma inu simunandimvere Ine.
15 И слах к вама све слуге своје пророке зарана једнако говорећи: Вратите се сваки са свог пута злог, и поправите дела своја и не идите за другим боговима служећи им, пак ћете остати у земљи коју сам дао вама и оцима вашим, али не пригнусте уха свог нити ме послушасте.
Kawirikawiri ndakhala ndikutumiza atumiki anga, aneneri, kwa inu. Iwo akhala akukuwuzani kuti, ‘Aliyense wa inu asiye ntchito zake zoyipa ndi kukonza makhalidwe ake; musatsatire milungu ina ndi kumayitumikira. Pamenepo mudzakhala mʼdziko limene ndinakupatsani ndi makolo anu.’ Komabe inu simunasamale zimenezi kapena kundimvera Ine.
16 Да, синови Јонадава сина Рихавовог извршују заповест оца свог што им је заповедио, а тај народ не слуша мене.
Zidzukulu za Yehonadabu mwana wa Rekabu zakhala zikumvera lamulo limene kholo lawo anazilamula, koma inuyo simunandimvere Ine.
17 Зато овако вели Господ Бог над војскама, Бог Израиљев: Ево, ја ћу пустити на Јуду и на све становнике јерусалимске све зло што изрекох за њих; јер им говорах, а они не послушаше, и звах их а они се не одазваше.
“Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndidzagwetsera pa Yuda ndi pa onse okhala mu Yerusalemu masautso onse amene ndinakonza chifukwa sanandimvere. Ndinawayitana koma iwo sanayankhe.’”
18 А породици Рихавовој рече Јеремија: Овако вели Господ над војскама Бог Израиљев: Што слушате заповест Јонадава оца свог и држите све заповести његове и чините све како вам је заповедио,
Yeremiya anawuza banja la Arekabu mawu onse a Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, kuti, “Munamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu ndipo mwatsatira malangizo ake onse ndi kuchita chilichonse chimene anakulamulani.”
19 Зато овако вели Господ над војскама Бог Израиљев: Неће нестати Јонадаву, сину Рихавовом човека који би стајао преда мном до века.
Tsono Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Yehonadabu mwana wa Rekabu sadzasowa munthu wonditumikira Ine nthawi zonse.”