< Књига пророка Јеремије 1 >

1 Речи Јеремије, сина Хелкијиног, између свештеника који беху у Анатоту у земљи Венијаминовој,
Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
2 Коме дође реч Господња у време Јосије сина Амоновог, цара Јудиног, тринаесте године царовања његовог,
Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
3 И у време Јоакима сина Јосијиног, цара Јудиног, до свршетка једанаесте године царовања Седекије сина Јосијиног над Јудом, док не би пресељен Јерусалим, петог месеца.
Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
4 И дође ми реч Господња говорећи:
Yehova anayankhula nane kuti,
5 Пре него те саздах у утроби, знах те; и пре него изиђе из утробе, посветих те; за пророка народима поставих те.
“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
6 А ја рекох: Ох, Господе, Господе! Ево, не знам говорити, јер сам дете.
Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
7 А Господ ми рече: Не говори: Дете сам; него иди куда те год пошаљем, и говори шта ти год кажем.
Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
8 Не бој их се, јер сам ја с тобом да те избављам, говори Господ.
Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
9 И пруживши Господ руку своју дотаче се уста мојих, и рече ми Господ: Ето, метнух речи своје у твоја уста.
Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
10 Види, постављам те данас над народима и царствима да истребљујеш и обараш, и да затиреш и раскопаваш, и да градиш и да садиш.
Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
11 После ми дође реч Господња говорећи: Шта видиш, Јеремија? И рекох: Видим прут бадемов.
Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
12 Тада ми рече Господ: Добро си видео, јер ћу настати око речи своје да је извршим.
Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
13 Опет ми дође реч Господња другом говорећи: Шта видиш? И рекох: Видим лонац где ври, и предња му је страна према северу.
Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
14 Тада ми рече Господ: Са севера ће навалити зло на све становнике ове земље.
Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
15 Јер, гле, ја ћу сазвати све породице из северних царстава, вели Господ, те ће доћи, и сваки ће метнути свој престо на вратима јерусалимским и око свих зидова његових и око свих градова Јудиних.
Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
16 И изрећи ћу им суд свој за сву злоћу њихову што ме оставише, и кадише другим боговима, и клањаше се делу руку својих.
Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
17 Ти дакле опаши се и устани и говори им све што ћу ти заповедити; не бој их се, да те не бих сатро пред њима.
“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
18 Јер ево ја те постављам данас као тврд град и као ступ гвозден и као зидове бронзане свој овој земљи, царевима Јудиним и кнезовима његовим и свештеницима његовим и народу земаљском.
Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
19 Они ће ударити на те, али те неће надвладати, јер сам ја с тобом, вели Господ, да те избављам.
Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

< Књига пророка Јеремије 1 >