< Књига пророка Исаије 54 >
1 Весели се, нероткињо која не рађаш, запевај и покликни ти, која не трпиш муке од порођаја, јер пуста има више деце него ли она која има мужа, вели Господ.
“Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
2 Рашири место шатора свог, и завесе стана твог нека се разастру, не брани, продужи ужа своја, коље своје утврди.
Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
3 Јер ћеш се надесно и налево распространити, и семе ће твоје наследити народе, и пусте ће градове населити.
Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
4 Не бој се, јер се нећеш осрамотити, и немој се стидети, јер нећеш бити прекорна, него ћеш заборавити срамоту младости своје, и прекора удовиштва свог нећеш се више сећати.
“Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
5 Јер ти је муж Творац твој, име Му је Господ над војскама, и Избавитељ ти је Светац Израиљев, Бог свој земљи зваће се.
Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
6 Јер као жену остављену и у духу ожалошћену дозва те Господ, и као младу жену пуштену, говори Господ.
Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
7 Замало оставих те, али с великом милошћу прибраћу те.
“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
8 У малом гневу сакрих за час лице своје од тебе, али ћу те вечном милошћу помиловати, вели Избавитељ твој Господ.
Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
9 Јер ми је то као потоп Нојев: јер као што се заклех да потоп Нојев неће више доћи на земљу, тако се заклех да се нећу разгневити на те нити ћу те карати.
“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
10 Ако ће се и горе помакнути и хумови се поколебати, опет милост моја неће се одмакнути од тебе, и завет мира мог неће се поколебати, вели Господ, који ти је милостив.
Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
11 Невољнице, коју ветар размеће, која си без утехе, ево ја ћу наместити камење твоје на мрамору порфирном, и основаћу те на сафирима.
“Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
12 И начинићу ти прозоре од кристала, и врата од камена рубина, и све међе твоје од драгог камења.
Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
13 А синови ће твоји сви бити научени од Господа, и обилан мир имаће синови твоји.
Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
14 Правдом ћеш се утврдити, далеко ћеш бити од насиља, те се нећеш бојати, и од страхоте, јер ти се неће приближити.
Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
15 Гле, биће их који ће се сабирати на те, али неће бити од мене; који се год саберу на те, пашће.
Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
16 Гле, ја сам створио ковача који распаљује угљевље и вади оруђе за свој посао, ја сам створио и крвника да убија.
“Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
17 Никакво оружје начињено против тебе неће бити срећно, и сваки језик који се подигне на те на суду сапрећеш. То је наследство слуга Господњих и правда њихова од мене, вели Господ.
palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.