< Књига пророка Исаије 40 >
1 Тешите, тешите народ мој, говори Бог ваш.
Atonthozeni, atonthozeni anthu anga, akutero Mulungu wanu.
2 Говорите Јерусалиму љубазно, и јављајте му да се навршио рок његов, да му се безакоње опростило, јер је примио из руке Господње двојином за све грехе своје.
Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu ndipo muwawuzitse kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha, tchimo lawo lakhululukidwa. Ndawalanga mokwanira chifukwa cha machimo awo onse.
3 Глас је некога који виче: Приправите у пустињи пут Господњи, поравните у пустоши стазу Богу нашем.
Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti, “Konzani njira ya Yehova mʼchipululu; wongolani njira zake; msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
4 Све долине нека се повисе, и све горе и брегови нека се слегну, и што је криво нека буде право, и неравна места нека буду равна.
Chigwa chilichonse achidzaze. Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse; Dziko lokumbikakumbika alisalaze, malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
5 И јавиће се слава Господња, и свако ће тело видети; јер уста Господња говорише.
Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera, ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona, pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
6 Глас говори: Вичи. И рече: Шта да вичем? Да је свако тело трава и све добро његово као цвет пољски.
Wina ananena kuti, “Lengeza.” Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani? “Pakuti anthu onse ali ngati udzu ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
7 Суши се трава, цвет опада кад дух Господњи дуне на њ; доиста је народ трава.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.” Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
8 Суши се трава, цвет опада; али реч Бога нашег остаје довека.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota, koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
9 Изађи на високу гору, Сионе, који јављаш добре гласове; подигни силно глас свој, Јерусалиме, који јављаш добре гласове; подигни, не бој се. Кажи градовима Јудиним: Ево Бога вашег.
Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni, kwera pa phiri lalitali. Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu, fuwula kwambiri, kweza mawu, usachite mantha; uza mizinda ya ku Yuda kuti, “Mulungu wanu akubwera!”
10 Ево, Господ Бог иде на јаког, и мишица ће Његова овладати њим; ево плата је његова код Њега и дело његово пред Њим.
Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu, ndipo dzanja lake likulamulira, taonani akubwera ndi mphotho yake watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
11 Као пастир пашће стадо своје; у наручје своје сабраће јагањце, и у недрима ће их носити, а дојилице ће водити полако.
Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa: Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
12 Ко је измерио воду грстима својим и небеса премерио пеђу? Ко је мером измерио прах земаљски, и горе измерио на мерила и брегове на потег?
Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu, kapena kuyeza kulemera kwa mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
13 Ко је управљао Духом Господњим? Или Му био саветник и научио Га?
Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
14 С ким се договарао и ко Га је уразумио и научио путу суда, и научио Га знању и показао Му пут разума?
Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya, kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru? Iye anapempha nzeru kwa yani ndi njira ya kumvetsa zinthu?
15 Гле, народи су као кап из ведра, и као прашка на мерилима броје се; гле, премешта острва као прашак.
Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko. Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo; mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
16 Ни Ливан не би био доста за огањ, и животиње његове не би биле доста за жртву паљеницу.
Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe, ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
17 Сви су народи као ништа пред Њим, мање неголи ништа и таштина вреде Му.
Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake; Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu ndi cha chabechabe.
18 С ким ћете дакле изједначити Бога? И какву ћете Му прилику наћи?
Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
19 Уметник лије лик, и златар га позлаћује, и верижице сребрне лије.
Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide naliveka mkanda wasiliva.
20 А ко је сиромах, те нема шта принети, бира дрво које не труне, и тражи вештог уметника да начини резан лик, који се не помиче.
Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere amasankha mtengo umene sudzawola, nafunafuna mʼmisiri waluso woti amupangire fano limene silingasunthike.
21 Не знате ли? Не чујете ли? Не казује ли вам се од искона? Не разумете ли од темеља земаљских?
Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe? Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
22 Он седи над кругом земаљским, и њени су Му становници као скакавци; Он је разастро небеса као платно и разапео их као шатор за стан.
Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi, Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala. Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga, nayikunga ngati tenti yokhalamo.
23 Он обраћа кнезове у ништа, судије земаљске чини да су као таштина.
Amatsitsa pansi mafumu amphamvu nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
24 Као да нису посађени ни посејани, и као да им се стабло није укоренило у земљи, чим дуне на њих, посахну, и вихор као плеву разнесе их.
Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene kapena kufesedwa chapompano, ndi kungoyamba kuzika mizu kumene ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
25 С ким ћете ме дакле изједначити да бих био као он? вели Свети.
Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani? Kapena kodi alipo wofanana nane?”
26 Подигните горе очи своје и видите; ко је то створио? Ко изводи војску свега тога на број и зове свако по имену, и велике ради силе Његове и јаке моћи не изостаје ниједно?
Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani. Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi? Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo, nayitana iliyonse ndi dzina lake. Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri, palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
27 Зашто говориш, Јакове, и кажеш, Израиљу: Сакривен је пут мој од Господа, и ствар моја не излази пред Бога мог?
Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti, “Yehova sakudziwa mavuto anga, Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
28 Не знаш ли? Ниси ли чуо да Бог вечни Господ, који је створио крајеве земаљске, не сустаје нити се утруђује? Разуму Његовом нема мере.
Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Yehova ndiye Mulungu wamuyaya, ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi. Iye sadzatopa kapena kufowoka ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
29 Он даје снагу уморном, и нејаком умножава крепост.
Iye amalimbitsa ofowoka ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
30 Деца се море и сустају, и младићи падају;
Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka, ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
31 Али који се надају Господу, добијају нову снагу, подижу се на крилима као орлови, трче и не сустају, ходе и не море се.
koma iwo amene amakhulupirira Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.