< 1 Мојсијева 34 >
1 А Дина кћи Лијина, коју роди Јакову, изађе да гледа девојке у оном крају.
Tsopano Dina, mwana amene Leya anaberekera Yakobo, anapita kukacheza ndi akazi ena a mʼdzikolo.
2 А угледа је Сихем, син Емора Ефејина, кнеза од оне земље, и узе је и леже с њом и осрамоти је.
Pamene Sekemu mwana wa Hamori Mhivi, mfumu ya deralo, anamuona, anamugwirira.
3 И приону срце његово за Дину кћер Јаковљеву, и девојка му омиле, и он јој се умиљаваше.
Koma Sekemu anamukondadi namwali uja, Dina, mwana wa Yakobo motero kuti anamuyankhula mawu womutonthoza.
4 И рече Сихем Емору оцу свом говорећи: Ожени ме овом девојком.
Choncho Sekemu anati kwa abambo ake Hamori, “Mundipezere mtsikana uyu kuti akhale mkazi wanga.”
5 А Јаков чу да је осрамотио Дину кћер његову; а синови његови беху у пољу са стоком његовом, и Јаков оћуте докле они не дођу.
Yakobo anamva kuti mwana wake Dina wagwiriridwa, koma sanachitepo kanthu msanga kudikira mpaka ana ake amuna omwe anali ku busa atabwerako.
6 А Емор отац Сихемов изиђе к Јакову да се разговори с њим.
Kenaka Hamori, abambo a Sekemu, anapita kukakambirana ndi Yakobo.
7 А кад дођоше синови Јаковљеви из поља и чуше шта је било, жао би људима врло и разгневише се веома, што учини срамоту Израиљу облежав кћер Јаковљеву, како не би ваљало чинити.
Pa nthawi iyi nʼkuti ana a Yakobo atabwererako ku busa kuja. Iwo atangomva zimene zinachitika, anawawidwa mtima. Iwo anapsa mtima kwambiri kuti Sekemu nʼkuchita chonyansa choterechi mu dziko la Israeli, kumugwirira Dina, mwana wa Yakobo.
8 Тада им рече Емор говорећи: Син мој Сихем срцем приону за вашу кћер; подајте му је за жену.
Koma Hamori anawawuza kuti, “Mwana wanga Sekemu wamukonda kwambiri mwana wanu. Chonde muloleni kuti akhale mkazi wake.
9 И опријатељите се с нама; кћери своје удајите за нас и кћерима нашим жените се.
Tiyeni tichite mgwirizano wa ukwati kuti ife tidzikwatira ana anu ndi inu mudzikwatira ana athu.
10 Па живите с нама, и земља ће вам бити отворена; настаните се и тргујте и држите баштине у њој.
Khazikikani pakati pathu. Mukhoza kupeza malo wokhala kulikonse kumene mufuna. Mukhozanso kuchita malonda momasuka ndi kupeza chuma.”
11 И рече Сихем оцу девојчином и браћи јој: Да нађем милост пред вама, и даћу шта ми год кажете.
Pamenepo Sekemu anati kwa abambo ndi alongo ake a Dina, “Inu mundikomere mtima, ndipo ndidzakupatsani chilichonse munganene.
12 Иштите ми колико год хоћете уздарја и дара, ја ћу дати шта год кажете; само ми дајте девојку за жену.
Tchulani mtengo wamalowolo umene ndiyenera kupereka, ndipo ndipereka. Ndidzakupatsani chilichonse chimene mukufuna malingana inu mukandipatsa namwaliyu kuti ndimukwatire.”
13 А синови Јаковљеви одговорише Сихему и Емору оцу његовом преварно, јер осрамоти Дину сестру њихову.
Ana a Yakobo anayankha Sekemu ndi abambo ake, Hamori mwachinyengo chifukwa mlongo wawo, Dina anali atayipitsidwa.
14 И рекоше им: Не можемо то учинити ни дати сестре своје за човека необрезаног, јер је то срамота нама.
Iwo anati, “Sitingachite zimenezo, kupereka mlongo wathu kwa munthu wosachita mdulidwe. Chimenecho ndi chinthu cha manyazi kwa ife.
15 Него ћемо вам учинити по вољи, ако ћете се изједначити с нама и обрезати све мушкиње између себе.
Tikuvomerani pokhapokha mutakhala ngati ife, mutachita mdulidwe ana anu onse aamuna.
16 Онда ћемо удавати своје кћери за вас и женићемо се вашим кћерима, и постаћемо један народ.
Kenaka tidzakulolani kuti mukwatire ana athu, ifenso tizikwatira ana anu. Choncho tidzakhala pakati panu ndipo tidzakhala anthu amodzi.
17 Ако ли не пристанете да се обрежете, ми ћемо узети своју девојку и отићи ћемо.
Koma ngati simuvomereza kuchita mdulidwe titenga mlongo wathu ndi kupita.”
18 И по вољи бише речи њихове Емору и Сихему сину Еморовом.
Mawu amenewa anakondweretsa Hamori ndi mwana wake Sekemu.
19 И момак не оклеваше учинити то; јер му кћи Јаковљева омиле веома; и он беше највише поштован између свих у кући оца свог.
Mnyamata uja amene anali wolemekezeka kwambiri pa banja lake lonse, sanachedwe kuchita mdulidwe popeza anamukonda kwambiri mwana wa Yakobo.
20 И отиде Емор и син му Сихем на врата града свог, и рекоше грађанима говорећи:
Choncho Hamori ndi mwana wake Sekemu anapita ku chipata cha mzinda wawo kukayankhula ndi anthu a mu mzindawo.
21 Ови људи хоће мирно да живе с нама, да се настане у овој земљи и да тргују по њој; а ево земља је широка и за њих; па ћемо се кћерима њиховим женити и своје ћемо кћери удавати за њих.
Iwo anati, “Anthu awa ndi a mtendere. Aloleni kuti akhale mʼdziko mwathu muno nachitamo malonda. Dzikoli lili ndi malo ambiri woti iwo nʼkukhalamo. Tingathe kukwatira ana awo aakazi ndipo angathe kukwatira ana athu aakazi.
22 Али ће тако пристати да живе с нама и да постанемо један народ, ако се све мушкиње међу нама обрежу, као што су они обрезани.
Komatu anthuwa adzavomereza kukhala amodzi a ife pokhapokha ngati amuna onse pakati pathu atachita mdulidwe monga alili iwo.
23 Њихова стока и њихово благо и сва говеда њихова неће ли бити наша? Сложимо се само с њима, па ће остати код нас.
Tikatero, ndiye kuti ziweto zawo zonsezi, katundu wawo yenseyu ndi ziweto zawo zina zonsezi zidzakhala zathu. Choncho tiyeni tiwavomereze ndipo adzakhazikika pakati pathu.”
24 И који излажаху на врата града његовог, сви послушаше Емора и Сихема сина његовог; и обреза се све мушкиње, сви који излажаху на врата града његовог.
Amuna onse amene anatuluka ku chipata cha mzinda anavomerezana ndi Hamori ndi mwana wake Sekemu, ndipo aliyense wamwamuna mu mzindamo anachita mdulidwe.
25 А трећи дан кад они беху у боловима, узеше два сина Јаковљева Симеун и Левије, браћа Динина, сваки свој мач и уђоше слободно у град и побише све мушкиње.
Patapita masiku atatu, amuna onse akumvabe ululu wa kuchita mdulidwe uja, ana awiri a Yakobo, Simeoni ndi Levi, alongo ake a Dina, anatenga malupanga ndi kulowa mu mzindawo mwakachetechete napha amuna onse.
26 Убише и Емора и сина му Сихема оштрим мачем, и узевши Дину из куће Сихемове отидоше.
Anapha Hamori ndi Sekemu. Anakatenga Dina ku nyumba kwa Sekemu nanyamuka.
27 Тада дођоше синови Јаковљеви на побијене, и опленише град, јер у њему би осрамоћена сестра њихова.
Ana a Yakobo anafika kwa anthu ophedwawo ndi kututa katundu mu mzindawo chifukwa anagwiririra mlongo wawo.
28 И узеше овце њихове и говеда њихова и магарце њихове, шта год беше у граду и шта бод беше у пољу.
Analanda nkhosa zawo, ngʼombe zawo, abulu awo ndi china chilichonse chawo mu mzindamo pamodzi ndi za ku minda.
29 И све благо њихово, и сву децу и жене њихове похваташе и одведоше, и шта год беше у којој кући.
Anawatengera chuma chawo chonse, akazi ndi ana awo, pamodzi ndi zonse zimene zinapezeka mʼnyumba zawo. Zonsezi zinayesedwa ngati zolandidwa ku nkhondo.
30 А Јаков рече Симеуну и Левију; сметосте ме, и омразисте ме народу ове земље, Хананејима и Ферезејима; у мене има мало људи, па ако се скупе на ме, хоће ме убити те ћу се истребити ја и дом мој.
Pamenepo Yakobo anati kwa Simeoni ndi Levi, “Mwandiputira mavuto, ndi kundiyipitsira dzina pakati pa anthu a mʼdziko lino, Akanaani ndi Aperezi. Ife ndife owerengeka, ndipo atati aphatikizane kudzandithira nkhondo, ndiye kuti ine ndi banja langa tidzawonongeka.”
31 А они рекоше: Зар са сестром нашом да раде као с курвом?
Koma iwo anayankha kuti, “Pepani, nanga achite kumusandutsa mlongo wathu ngati mkazi wachiwerewere?”