< 2 Књига Самуилова 24 >

1 А Господ се опет разгневи на Израиља, и надражи Давида на њих говорећи: Хајде изброј Израиља и Јуду.
Nthawi inanso Yehova anawakwiyira Aisraeli ndipo anawutsa mtima wa Davide kuti awavutitse ndipo anati, “Pita kawerenge Aisraeli ndi Ayuda.”
2 И рече цар Јоаву, војводи свом: Прођи по свим племенима Израиљевим од Дана до Вирсавеје, и избројте народ, да знам колико има народа.
Choncho mfumu inati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali nawo. “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba kuti mukawerenge anthu omenya nkhondo ndi cholinga choti ndidziwe chiwerengero chawo.”
3 А Јоав рече цару: Нека дода Господ Бог твој к народу колико га је сад још сто пута толико, и да цар господар мој види својим очима; али зашто цар господар мој хоће то?
Koma Yowabu anayankha mfumu kuti, “Yehova Mulungu wanu achulukitse ankhondo anu kukhala miyandamiyanda, ndipo alole inu mbuye wanga mfumu mudzazione zimenezi. Koma nʼchifukwa chiyani inu mbuye wanga mfumu mukufuna kuchita zimenezi?”
4 Али реч царева би јача од Јоава и војвода; и отиде Јоав и војводе од цара да преброје народ Израиљев.
Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu ndi atsogoleri a ankhondo. Choncho anachoka pamaso pa mfumu kupita kukawerenga anthu omenya nkhondo mu Israeli.
5 И прешавши преко Јордана стадоше у логор у Ароиру, с десне стране града, који је на средини потока Гадовог, и код Јазира.
Atawoloka Yorodani, iwo anamanga misasa yawo pafupi ndi Aroeri kummwera kwa mzinda wa ku chigwa ndipo kenaka iwo anapita ku dziko la Gadi mpaka ku Yazeri.
6 Потом дођоше у Галад, и у доњу земљу Одсију, а одатле отидоше у Дан-Јан и у околину сидонску.
Iwo anapita ku Giliyadi ndi ku chigwa cha Tahitimu Hodisi ndipo anapitirira mpaka ku Dani Yaani ndi madera ozungulira Sidoni.
7 Потом дођоше до града Тира и у све градове јевејске и хананејске; и отидоше на јужну страну Јудину у Вирсавеју.
Kenaka iwo anapita molunjika linga la ku Turo ndi ku mizinda yonse ya Ahivi ndi Akanaani. Pomaliza anapita ku Beeriseba ku Negevi wa ku Yuda.
8 И обишавши сву земљу вратише се у Јерусалим после девет месеци и двадесет дана.
Atayendayenda mʼdziko lonse anabwerera ku Yerusalemu patapita miyezi isanu ndi inayi ndi masiku makumi awiri.
9 И Јоав даде цару број преписаног народа; и беше од Израиља осам стотина хиљада људи за војску који махаху мачем, а људи од Јуде пет стотина хиљада.
Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa mfumu: Mu Israeli munali anthu 800,000 amphamvu amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga ndipo mu Yuda munali anthu 500,000.
10 Тада Давида такну у срце, пошто преброја народ, и рече Давид Господу: Сагреших веома што то урадих. Али, Господе, узми безакоње слуге свог, јер веома лудо радих.
Davide anatsutsika mu mtima mwake atatha kuwerenga anthuwo ndipo anapemphera kwa Yehova kuti, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono Yehova, ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
11 А кад Давид уста ујутру, дође реч Господња Гаду, пророку који беше Давиду виделац, и рече:
Davide asanadzuke mmawa mwake mawu a Yehova anafika kwa mneneri Gadi, mlosi wa Davide kuti,
12 Иди и кажи Давиду: Овако вели Господ: Троје ти дајем, изабери једно да ти учиним.
“Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
13 И дође Гад к Давиду, и каза му говорећи: Хоћеш ли ти да буде седам гладних година у земљи твојој, или да бежиш три месеца од непријатеља својих и они да те гоне, или да буде три дана помор у твојој земљи? Сад промисли и гледај шта ћу одговорити Ономе који ме је послао.
Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa iye, “Kodi mungakonde kuti mʼdziko mwanu mukhale njala kwa zaka zitatu? Kapena kuti mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu? Kapena kuti mʼdziko muno mukhale mliri kwa masiku atatu? Tsopano, ganizirani bwino ndipo musankhe chomwe mudzamuyankhe amene wandituma.”
14 А Давид рече Гаду: У тескоби сам љутој; али нека западнемо Господу у руке, јер је милост Његова велика; а људима да не западнем у руке.
Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ife atilange ndi Yehova pakuti chifundo chake ndi chachikulu, koma ndisalangidwe ndi anthu.”
15 И тако пусти Господ помор на Израиља од јутра до одређеног времена, и помре народа од Дана до Вирсавеје седамдесет хиљада људи.
Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene anafuna mwini wake, ndipo unapha anthu 70,000 kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba.
16 А кад анђео пружи руку своју на Јерусалим да га убија, сажали се Господу са зла, и рече анђелу који убијаше народ: Доста, спусти руку. А анђео Господњи беше код гумна Орне Јевусејина.
Pamene mngelo anatambasula dzanja lake kuti awononge Yerusalemu, Yehova anamva chisoni chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
17 А Давид кад виде анђела где бије народ, проговори и рече Господу: Ево, ја сам згрешио, ја сам зло учинио, а те овце шта су учиниле? Нека се рука Твоја обрати на мене и на дом оца мог.
Davide ataona mngelo amene ankakantha anthu uja, anati kwa Yehova, “Ine ndi amene ndachimwa. Ine mʼbusa ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Langani ineyo pamodzi ndi banja langa.”
18 Потом опет дође Гад к Давиду исти дан, и рече му: Иди, начини Господу олтар на гумну Орне Јевусејина.
Tsiku limenelo Gadi anapita kwa Davide ndi kukanena kuti, “Pitani kamangeni guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.”
19 И отиде Давид по речи Гадовој, како Господ заповеди.
Ndipo Davide anapita monga momwe Yehova anamulamulira kudzera mwa Gadi.
20 Тада Орна обазревши се угледа цара и слуге његове где иду к њему; и отиде Орна и поклони се цару лицем до земље,
Arauna atayangʼana ndi kuona mfumu ndi anthu ake akubwera kumene kunali iye, iyeyo anatuluka ndi kuwerama pamaso pa mfumu mpaka nkhope yake kugunda pansi.
21 И рече: Што је дошао цар господар мој слузи свом? А Давид рече: Да купим од тебе то гумно, да начиним на њему олтар Господу да би престао помор у народу.
Arauna anati, “Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mfumu mwabwera kwa mtumiki wanu?” Davide anayankha kuti, “Kudzagula malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe kuti mliri uli pa anthuwa usiye.”
22 А Орна рече Давиду: Нека узме цар господар мој и принесе на жртву шта му је воља; ево волова за жртву паљеницу, и кола и јармова волујских за дрва.
Arauna anati kwa Davide, “Mbuye wanga mfumu mutenge chilichonse chimene chikukondweretseni ndi kuchipereka nsembe. Nazi ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, nazi zopunthira tirigu ndi magoli angʼombe kuti zikhale nkhuni.
23 Све то даваше цару Орна као цар, и рече Орна цару: Господ Бог твој нека те милостиво прими.
Inu mfumu, Arauna akupereka zonsezi kwa inu mfumu.” Arauna anatinso kwa iye, “Yehova Mulungu wanu akuvomerezeni.”
24 А цар рече Орни: Не; него ћу купити од тебе по цени, нити ћу принети Господу Богу свом жртву паљеницу поклоњену. И тако купи Давид гумно и волове за педесет сикала сребра.
Koma mfumu inayankha Arauna kuti, “Ayi, Ine ndikunenetsa kuti ndikulipira. Sindidzapereka kwa Yehova Mulungu wanga nsembe yopsereza imene sindinavutikire.” Kotero Davide anagula malo wopunthira tiriguwo ndi ngʼombe ndipo anapereka kwa Araunayo masekeli asiliva makumi asanu.
25 И онде начини Давид олтар Господу, и принесе жртве паљенице и жртве захвалне. И Господ се умилостиви земљи, и преста помор у Израиљу.
Davide anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Ndipo Yehova anayankha pempherolo mʼmalo mwa dziko lonse, ndipo mliri unatha pa Aisraeli.

< 2 Књига Самуилова 24 >