< Jeremija 52 >

1 Dvadeset i jedna godina bijaše Sedekiji kad poèe carovati, i carova jedanaest godina u Jerusalimu. Materi mu bješe ime Amutala kæi Jeremijina, iz Livne.
Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
2 On èinjaše što je zlo pred Gospodom sasvijem kako je èinio Joakim.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
3 Jer od gnjeva Gospodnjega zbi se Jerusalimu i Judi, te ih odbaci ispred sebe. A Sedekija se odmetnu od cara Vavilonskoga.
Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
4 I tako devete godine njegova carovanja, desetoga dana doðe Navuhodonosor car Vavilonski sa svom vojskom svojom na Jerusalim; i stadoše u oko pod njim, i naèiniše opkope oko njega.
Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
5 I grad bi opkoljen do jedanaeste godine carovanja Sedekijina.
Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
6 I devetoga dana èetvrtoga mjeseca nasta velika glad u gradu, te narod zemaljski nemaše hljeba.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
7 Tada grad bi provaljen, i vojnici svi pobjegoše i izidoše iz grada noæu na vrata izmeðu dva zida uz vrt carev, a Haldejci bijahu svuda oko grada; i otidoše putem k pustinji.
Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
8 Ali vojska Haldejska potjera cara, i stigoše Sedekiju u polju Jerihonskom, a sva vojska što bijaše s njim razbježe se od njega.
koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
9 I uhvatiše cara i odvedoše ga k caru Vavilonskom u Rivlu u zemlji Ematskoj; i ondje mu sudi.
Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
10 I pokla car Vavilonski sinove Sedekijine na njegove oèi, i sve knezove Judine pokla u Rivli.
Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
11 I Sedekiji iskopa oèi, i svezav ga u dvoje verige mjedene odvede ga car Vavilonski u Vavilon i metnu ga u tamnicu, gdje osta do smrti svoje.
Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
12 A desetoga dana petoga mjeseca godine devetnaeste carovanja Navuhodonosora cara Vavilonskoga doðe u Jerusalim Nevuzardan zapovjednik stražarski, koji služaše caru Vavilonskom.
Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
13 I popali dom Gospodnji i dom carski i sve domove u Jerusalimu; sve velike kuæe popali ognjem.
Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
14 I sve zidove Jerusalimske unaokolo razvali sva vojska Haldejska što bijaše sa zapovjednikom stražarskim.
Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
15 A narod siromašni i ostatak naroda što osta u gradu, i prebjege što prebjegoše k caru Vavilonskom, i ostali prosti narod, odvede Nevuzardan zapovjednik stražarski.
Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
16 Samo od siromašnoga naroda u zemlji ostavi Nevuzardan zapovjednik stražarski koji æe biti vinogradari i ratari.
Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
17 I stupove mjedene što bijahu u domu Gospodnjem, i podnožja i more mjedeno koje bijaše u domu Gospodnjem, izlomiše Haldejci, i mjed od njih odnesoše u Vavilon.
Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
18 I lonce i lopate i viljuške i kotliæe i kadionice i sve sudove mjedene kojima služahu, uzeše,
Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
19 I umivaonice i kliješta s kotliæima i loncima i svijetnjacima i kadionicama i èašama, što god bijaše zlatno i što god bijaše srebrno, uze zapovjednik stražarski.
Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
20 Dva stupa, jedno more, i dvanaest volova mjedenijeh što bijahu pod podnožjima, što naèini car Solomun za dom Gospodnji, ne bješe mjere mjedi od svijeh tijeh sudova.
Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
21 A stupovi bijahu svaki od osamnaest lakata u visinu, a unaokolo od dvanaest lakata, a èetiri prsta bješe svaki debeo i šupalj;
Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
22 I ozgo na njemu bijaše oglavlje mjedeno, i oglavlje bješe visoko pet lakata, i pletenica i šipci oko oglavlja, sve od mjedi; taki bijaše i drugi stup sa šipcima.
Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
23 I bijaše devedeset i šest šipaka sa svake strane; svega šipaka na pletenici unaokolo bijaše sto.
Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
24 Uze zapovjednik stražarski i Seraju prvoga sveštenika i Sofoniju drugoga sveštenika, i tri vratara.
Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
25 A iz grada uze jednoga dvoranina, koji bijaše nad vojnicima, i sedam ljudi koji stajahu pred carem, koji se naðoše u gradu, i prvoga pisara vojnièkoga, koji popisivaše narod po zemlji u vojsku, i šezdeset ljudi iz naroda zemaljskoga, koji se naðoše u gradu.
Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
26 Uze ih Nevuzardan zapovjednik stražarski i odvede k caru Vavilonskom u Rivlu.
Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
27 A car ih Vavilonski pobi i pogubi u Rivli u zemlji Ematskoj. Tako bi preseljen Juda iz zemlje svoje.
Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
28 Ovo je narod što ga preseli Navuhodonosor: sedme godine tri tisuæe i dvadeset i tri Judejca;
Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
29 Godine osamnaeste Navuhodonosorove preseli iz Jerusalima osam stotina i trideset i dvije duše;
mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
30 Godine dvadeset treæe Navuhodonosorove preseli Nevuzardan zapovjednik stražarski Judejaca sedam stotina i èetrdeset i pet duša; svega èetiri tisuæe i šest stotina duša.
mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
31 A trideset sedme godine otkako se zarobi Joahin car Judin, dvanaestoga mjeseca, dvadeset petoga dana, Evil-Merodah car Vavilonski iste godine zacariv se izvadi iz tamnice Joahina cara Judina.
Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
32 I lijepo govori s njim, i namjesti mu prijesto više prijestola drugih careva koji bijahu kod njega u Vavilonu.
Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
33 I promijeni mu haljine tamnièke, i on jeðaše svagda s njim svega vijeka svojega.
Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
34 I hrana mu se jednako davaše od cara Vavilonskoga svaki dan svega vijeka njegova do smrti njegove.
Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.

< Jeremija 52 >