< Isaías 9 >
1 Mas não haverá mais tristeza para ela que estava em angústia. No primeiro tempo, ele desprezou a terra de Zebulom e a terra de Naftali; mas no segundo tempo ele a tornou gloriosa, pelo caminho do mar, além do Jordão, a Galiléia das nações.
Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.
2 As pessoas que caminharam na escuridão viram uma grande luz. A luz brilhou sobre aqueles que viviam na terra da sombra da morte.
Anthu oyenda mu mdima awona kuwala kwakukulu; kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani kuwunika kwawafikira.
3 Você multiplicou a nação. Você aumentou a alegria deles. Eles se alegram diante de você de acordo com a alegria da colheita, assim como os homens se alegram quando dividem o saque.
Inu mwauchulukitsa mtundu wanu ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo. Iwo akukondwa pamaso panu, ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola, ngatinso mmene anthu amakondwera pamene akugawana zolanda ku nkhondo.
4 Pelo jugo de seu fardo, e pelo bastão de seu ombro, a vara de seu opressor, vocês se quebraram como no dia de Midian.
Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani, inu mwathyola goli limene limawalemera, ndodo zimene amamenyera mapewa awo, ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.
5 Pois toda a armadura do homem armado na batalha ruidosa, e as vestes enroladas em sangue, será para queimar, combustível para o fogo.
Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo, ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi zidzatenthedwa pa moto ngati nkhuni.
6 Pois uma criança nasce para nós. Um filho nos é dado; e o governo estará em seus ombros. Seu nome será chamado Conselheiro Maravilhoso, Deus Poderoso, Pai Eterno, Príncipe da Paz.
Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife, ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake. Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
7 Do aumento de seu governo e da paz não haverá fim, no trono de Davi, e em seu reino, para estabelecê-lo e sustentá-lo com justiça e com retidão a partir daquele momento, mesmo para sempre. O zelo de Javé dos Exércitos fará isso.
Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pa mpando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi.
8 O Senhor enviou uma palavra para Jacob, e cai sobre Israel.
Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo; ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
9 All o povo saberá, incluindo Efraim e os habitantes de Samaria, que dizem com orgulho e arrogância de coração,
Anthu onse okhala mu Efereimu ndi okhala mu Samariya, adzadziwa zimenezi. Iwo amayankhula modzikuza kuti,
10 “Os tijolos caíram, mas vamos construir com pedra cortada. As figueiras de sicômoro foram cortadas, mas vamos colocar cedros em seu lugar”.
“Ngakhale njerwa zagumuka, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema. Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa, koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
11 Therefore Yahweh colocará no alto contra ele os adversários de Rezin, e agitará seus inimigos,
Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
12 Os sírios na frente, e os filisteus por trás; e eles devorarão Israel de boca aberta. Por tudo isso, sua raiva não é desviada, mas sua mão ainda está estendida.
Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo ayasama pakamwa kuti adye a Israeli. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
13 No entanto, as pessoas não se voltaram para aquele que as atingiu, nem procuraram o Yahweh dos exércitos.
Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja, ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
14 Therefore Yahweh cortará a cabeça e a cauda de Israel, ramo de palma e palheta, em um dia.
Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe, nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
15 O ancião e o homem honrado é o chefe, e o profeta que ensina mentiras é a cauda.
mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka, mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
16 Para aqueles que conduzem este povo, os desviam; e aqueles que são liderados por eles são destruídos.
Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa, ndipo otsogoleredwa amatayika.
17 Portanto, o Senhor não se regozijará com seus jovens, nem terá compaixão de seus órfãos e viúvas; para todos é profano e um malfeitor, e cada boca fala loucuras. Por tudo isso, sua raiva não é desviada, mas sua mão ainda está estendida.
Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata, ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye, pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo aliyense amayankhula zopusa. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
18 Pois a maldade queima como uma fogueira. Ela devora os sarças e os espinhos; sim, ele se acende na mata da floresta, e eles rolam para cima em uma coluna de fumaça.
Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto; moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga, umayatsa nkhalango yowirira, ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
19 Através da ira de Yahweh dos exércitos, a terra é queimada; e as pessoas são o combustível para o fogo. Ninguém poupa seu irmão.
Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse, dziko lidzatenthedwa ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto; palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
20 Uma pessoa devorará na mão direita, e terá fome; e ele comerá na mão esquerda, e eles não ficarão satisfeitos. Cada um comerá a carne de seu próprio braço:
Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya, koma adzakhalabe ndi njala; kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya, koma sadzakhuta. Aliyense azidzadya ana ake omwe.
21 Manasseh comendo Efraim e Efraim comendo Manasseh, e juntos estarão contra Judá. Por tudo isso, sua raiva não é desviada, mas sua mão ainda está estendida.
Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase; onsewa pamodzi adzadya Yuda. Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.