< Zachariasza 4 >

1 Potem Anioł, który rozmawiał ze mną, powrócił i obudził mnie, jak budzi się kogoś ze snu.
Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo.
2 I zapytał mnie: Co widzisz? Odpowiedziałem: Spojrzałem, a oto świecznik cały ze złota, a na jego szczycie jest czasza, na nim siedem lamp, a [także] siedem rurek do tych siedmiu lamp, które [są] na jego szczycie;
Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira.
3 Dwa drzewa oliwne obok niego, jedno po prawej stronie czaszy, a drugie po jej lewej stronie.
Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”
4 Wtedy odezwałem się do Anioła, który rozmawiał ze mną, i zapytałem: Co to jest, mój Panie?
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”
5 Anioł, który rozmawiał ze mną, odpowiedział mi: Czy nie wiesz, co to jest? Odpowiedziałem: Nie [wiem], mój Panie.
Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”
6 Wtedy odpowiedział mi: Oto słowo PANA do Zorobabela: Nie wojskiem ani siłą, ale moim Duchem, mówi PAN zastępów.
Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
7 Czymże ty jesteś, góro wielka? Wobec Zorobabela staniesz się równiną. On bowiem wyniesie główny kamień z głośnym okrzykiem: Łaska, łaska nad nim.
“Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’”
8 I doszło słowo PANA do mnie mówiące:
Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti,
9 Ręce Zorobabela położyły fundamenty tego domu, jego ręce go dokończą; a poznasz, że PAN zastępów posłał mnie do was.
“Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.
10 Któż bowiem wzgardził dniem małych [początków]? Oni bowiem będą się radować, patrząc na pion w ręku Zorobabela i na tych siedmioro oczu PANA, które przebiegają całą ziemię.
“Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli. (“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)
11 Wtedy odezwałem się i zapytałem go: Co [oznaczają te] dwa drzewa oliwne po prawej i lewej stronie tego świecznika?
Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”
12 I ponownie odezwałem się, i zapytałem go: Co [oznaczają te] dwie gałęzie oliwne, które dwiema złotymi rurkami wypuszczają z siebie złocistą oliwę?
Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”
13 On zapytał: Nie wiesz, [co to jest]? Odpowiedziałem: Nie [wiem], mój Panie.
Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”
14 Wtedy powiedział: To są dwaj pomazańcy, którzy stoją przed Panem całej ziemi.
Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”

< Zachariasza 4 >