< مزامیر 33 >
ای صالحان در خداوند شادی نمایید، زیرا که تسبیح خواندن راستان رامی شاید. | ۱ 1 |
Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
خداوند را بربط حمد بگویید. با عودده تار او را سرود بخوانید. | ۲ 2 |
Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
سرودی تازه برای اوبسرایید. نیکو بنوازید با آهنگ بلند. | ۳ 3 |
Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
زیرا کلام خداوند مستقیم است و جمیع کارهای او با امانت است. | ۴ 4 |
Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
عدالت و انصاف را دوست میدارد. جهان از رحمت خداوند پر است. | ۵ 5 |
Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
به کلام خداوند آسمانها ساخته شد و کل جنود آنها به نفخه دهان او. | ۶ 6 |
Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
آبهای دریا را مثل توده جمع میکند و لجهها را در خزانهها ذخیره مینماید. | ۷ 7 |
Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
تمامی اهل زمین از خداوند بترسند. جمیع سکنه ربع مسکون از او بترسند. | ۸ 8 |
Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
زیرا که او گفت و شد. او امر فرمود و قایم گردید. | ۹ 9 |
Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
خداوندمشورت امتها را باطل میکند. تدبیرهای قبائل را نیست میگرداند. | ۱۰ 10 |
Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
مشورت خداوند قائم است تا ابدالاباد. تدابیر قلب او تا دهرالدهور. | ۱۱ 11 |
Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
خوشابحال امتی که یهوه خدای ایشان است وقومی که ایشان را برای میراث خود برگزیده است. | ۱۲ 12 |
Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
از آسمان خداوند نظر افکند و جمیع بنی آدم را نگریست. | ۱۳ 13 |
Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
از مکان سکونت خویش نظر میافکند، برجمیع ساکنان جهان. | ۱۴ 14 |
kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
او که دلهای ایشان را جمیع سرشته است و اعمال ایشان را درک نموده است. | ۱۵ 15 |
Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
پادشاه به زیادتی لشکر خلاص نخواهد شد و جبار به بسیاری قوت رهایی نخواهد یافت. | ۱۶ 16 |
Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
اسب به جهت استخلاص باطل است و به شدت قوت خودکسی را رهایی نخواهد داد. | ۱۷ 17 |
Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
اینک چشم خداوند بر آنانی است که از او میترسند، برآنانی که انتظار رحمت او را میکشند. | ۱۸ 18 |
Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
تاجان ایشان را از موت رهایی بخشد و ایشان رادر قحط زنده نگاه دارد. | ۱۹ 19 |
kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
جان ما منتظرخداوند میباشد. او اعانت و سپر ما است. | ۲۰ 20 |
Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
زیرا که دل ما در او شادی میکند و در نام قدوس او توکل میداریم. | ۲۱ 21 |
Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
ای خداوندرحمت تو بر ما باد. چنانکه امیدوار توبودهایم. | ۲۲ 22 |
Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.