< Amahubo 88 >
1 Nkosi Nkulunkulu wosindiso lwami, emini, ebusuku ngakhala phambi kwakho.
Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
2 Umkhuleko wami kawuze phambi kwakho; beka indlebe yakho ekukhaleni kwami.
Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
3 Ngoba umphefumulo wami ugcwele ukuhlupheka, lempilo yami ifinyelela engcwabeni. (Sheol )
Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol )
4 Ngibalwa lalabo abehlela emgodini; nginjengomuntu ongelamandla.
Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
5 Ngikhululwe phakathi kwabafileyo, nginjengababuleweyo abalele engcwabeni, ongasabakhumbuliyo; ngoba bequnyiwe basuswa esandleni sakho.
Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
6 Ungifakile emgodini ongaphansi kakhulu, emnyameni, ekujuleni.
Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
7 Intukuthelo yakho iyangeleka, langawo wonke amagagasi akho ungihluphile. (Sela)
Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
8 Ususele khatshana lami abejwayelene lami; wangenza ngibe yisinengiso kubo; ngivalelwe, ngingephume.
Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
9 Ilihlo lami liyaphela ngenxa yosizi. Ngikubizile lonke usuku, Nkosi, ngelulele izandla zami kuwe.
maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
10 Abafileyo uyabenzela izimangaliso yini? Imimoya efileyo izavuka yini ikudumise? (Sela)
Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
11 Uthando lwakho luzalandiswa yini engcwabeni? Ukuthembeka kwakho encithakalweni yini?
Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
12 Izimangaliso zakho zizakwaziwa yini emnyameni? Lokulunga kwakho elizweni lokukhohlwa yini?
Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
13 Kodwa mina, Nkosi, ngikhalile kuwe, lekuseni umkhuleko wami uzakuza phambi kwakho.
Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
14 Nkosi, ulahlelani umphefumulo wami? Ubufihlelani ubuso bakho kimi?
Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
15 Ngihluphekile ngingofayo kusukela ebutsheni, ngithwele ukwesabeka kwakho, ngikhathazekile.
Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
16 Ulaka lwakho olutshisayo ludlulile phezu kwami, okwesabekayo kwakho kungiqedile.
Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
17 Kungizingelezile njengamanzi usuku lonke, kungihanqile kanyekanye.
Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
18 Ususele khatshana lami othandayo lomngane, abejwayelene lami basemnyameni.
Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.