< Amahubo 45 >
1 Inhliziyo yami iphuphuma ngendaba enhle; ngikhuluma ngezinto engizenzele inkosi; ulimi lwami lulusiba lombhali ophangisayo.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
2 Umuhle kulabantwana babantu; umusa uthululwe endebeni zakho; ngenxa yalokho uNkulunkulu ukubusisile kuze kube phakade.
Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
3 Bhinca inkemba yakho emlenzeni, qhawe, udumo lwakho lobukhosi bakho.
Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
4 Lebukhosini bakho gada uphumulele, ngenxa yeqiniso lobumnene bokulunga; lesandla sakho sokunene sikufundise izinto ezesabekayo.
Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
5 Imitshoko yakho ibukhali enhliziyweni yezitha zenkosi; izizwe zizakuwa ngaphansi kwakho.
Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
6 Isihlalo sakho sobukhosi, Nkulunkulu, ngesaphakade laphakade; intonga yakho yobukhosi iyintonga yobuqotho.
Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
7 Uthanda ukulunga, njalo uzonda ububi; ngenxa yalokho uNkulunkulu, uNkulunkulu wakho, ukugcobile ngamafutha entokozo ngaphezu kwabanakwenu.
Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
8 Izembatho zakho zonke ziqholiwe ngemure lenhlaba lekhasiya; ezigodlweni zempondo zendlovu abakwenze wathokoza ngazo.
Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
9 Amadodakazi amakhosi aphakathi kwabesifazana bakho abadumileyo; indlovukazi imi esandleni sokunene sakho yembethe igolide leOfiri.
Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
10 Zwana, ndodakazi, unakane, ubeke indlebe yakho; ukhohlwe abantu bakini lendlu kayihlo;
Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
11 khona inkosi izalangatha ubuhle bakho; ngoba iyinkosi yakho, njalo khothama kuyo.
Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
12 Lendodakazi yeTire ilesipho, labanothileyo ebantwini, bazancenga ubuso bakho.
Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
13 Indodakazi yenkosi iyakhazimula yonke ngaphakathi, isembatho sayo singesegolide elelukiweyo.
Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
14 Izalethwa enkosini yembethe isembatho esifekethisiweyo; izintombi eziyilandelayo, abangane bayo, zizalethwa kuwe.
Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
15 Zizalethwa ngokuthaba lenjabulo, zizangena esigodlweni senkosi.
Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
16 Esikhundleni saboyihlo kuzakuba ngamadodana akho, uzawabeka abe yiziphathamandla emhlabeni wonke.
Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
17 Ibizo lakho ngizalenza likhunjulwe ezizukulwaneni zonke; ngenxa yalokho izizwe zizakudumisa kuze kube nini lanini.
Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.