< Amahubo 110 >
1 INkosi yathi eNkosini yami: Hlala ngakwesokunene sami, ngize ngenze izitha zakho zibe yisenabelo senyawo zakho.
Salimo la Davide. Yehova akuwuza Mbuye wanga kuti, “Khala ku dzanja langa lamanja mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.”
2 INkosi izathuma intonga yamandla akho ivela eZiyoni. Busa phakathi kwezitha zakho.
Yehova adzakuza ndodo yamphamvu ya ufumu wako kuchokera mʼZiyoni; udzalamulira pakati pa adani ako.
3 Abantu bakho bazavuma ngosuku lwamandla akho, ebuhleni bobungcwele, kusukela esizalweni semadabukakusa kuza kuwe amazolo obutsha bakho.
Ankhondo ako adzakhala odzipereka pa tsiku lako la nkhondo. Atavala chiyero chaulemerero, kuchokera mʼmimba ya mʼbandakucha, udzalandira mame a unyamata wako.
4 INkosi ifungile, kayiyikuphenduka: Wena ungumpristi kuze kube nininini ngokwendlela kaMelkizedeki.
Yehova walumbira ndipo sadzasintha maganizo ake: “Ndiwe wansembe mpaka muyaya monga mwa unsembe wa Melikizedeki.”
5 INkosi ngakwesokunene sakho izachoboza amakhosi osukwini lokuthukuthela kwayo.
Ambuye ali kudzanja lako lamanja; Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake.
6 Izakwehlulela phakathi kwezizwe, kugcwale izidumbu; izachoboza inhloko phezu kwelizwe elikhulu.
Adzaweruza anthu a mitundu ina, adzadzaza dziko lapansi ndi mitembo ndipo adzaphwanya olamulira a pa dziko lonse lapansi.
7 Izanatha esifuleni endleleni; ngakho-ke izaphakamisa ikhanda.
Iye adzamwa mu mtsinje wa mʼmbali mwa njira; choncho adzaweramutsa mutu wake.