< Amahubo 109 >

1 Nkulunkulu wendumiso yami, ungathuli.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
2 Ngoba umlomo wokhohlakeleyo lomlomo wenkohliso uvulekile umelene lami; bakhulume lami ngolimi lwamanga.
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
3 Bangihanqa ngamazwi enzondo, balwa bemelene lami kungelasizatho.
Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
4 Esikhundleni sothando lwami bayizitha zami, kodwa mina ngisemkhulekweni.
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
5 Basebengibuyisela okubi esikhundleni sokuhle, lenzondo esikhundleni sothando lwami.
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
6 Umise omubi phezu kwakhe, loSathane kame ngakwesokunene sakhe.
Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
7 Ekwahlulelweni kwakhe kaphume elecala; lomkhuleko wakhe ube yisono.
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
8 Insuku zakhe kazibe nlutshwana; omunye athathe isikhundla sakhe.
Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
9 Abantwana bakhe kabangabi loyise, lomkakhe abe ngumfelokazi.
Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 Abantwana bakhe kabazulazule bephanza isinkwa sabo, bacele bevela emanxiweni abo.
Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 Umebolekisi kabambe konke alakho, labezizweni baphange izithelo zomsebenzi wakhe.
Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 Kungabi khona omelulela umusa, futhi kungabi khona ozwela intandane zakhe.
Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 Inzalo yakhe kayiqunywe, lebizo labo lesulwe esizukulwaneni esilandelayo.
Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 Ububi baboyise bukhunjulwe eNkosini, lesono sikanina singesulwa.
Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 Kabube phambi kweNkosi njalonjalo, ukuze aqume ukukhunjulwa kwabo kusuke emhlabeni.
Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
16 Ngenxa yokuthi wayengakhumbuli ukwenza umusa, kodwa wazingela umuntu ohluphekayo longumyanga, lodabukileyo enhliziyweni ukumbulala.
Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
17 Njengoba wathanda ukuqalekisa, ngakho kakwehlele kuye; njengoba wayengathandi ukubusisa, ngakho kakube khatshana laye.
Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
18 Njengoba wagqoka isiqalekiso njengesigqoko sakhe, ngakho kakungene emibilini yakhe njengamanzi, lanjengamafutha emathanjeni akhe.
Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 Kakube kuye njengesembatho azembesa ngaso, kube libhanti azibopha ngalo njalonjalo.
Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 Lokhu kube ngumvuzo wezitha zami ovela eNkosini, lowalabo abakhuluma okubi ngomphefumulo wami.
Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
21 Kodwa wena, Jehova, Nkosi, ngenzela ngenxa yebizo lakho; ngoba umusa wakho ulungile, ngikhulule.
Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 Ngoba mina ngiyisihlupheki lomyanga, lenhliziyo yami ilimele phakathi kwami.
Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 Ngedlula njengesithunzi sisiba side; ngizanyazanyiswe njengesikhonyane.
Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 Amadolo ami ayaxega ngokuzila ukudla, lenyama yami isicakile iswela ukukhuluphala.
Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 Mina sengibe lihlazo kubo, bengibona banikina ikhanda labo.
Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
26 Ngisize, Nkosi, Nkulunkulu wami, ungisindise ngokomusa wakho.
Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 Ukuze bazi ukuthi lesi yisandla sakho; wena, Nkosi, ukwenzile.
Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 Kabathuke bona, kodwa wena ubusise; nxa bevuka kabayangeke, kodwa inceku yakho kayithabe.
Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 Izitha zami kazigqokiswe ngehlazo, kazizigoqele ngenhloni zazo njengesembatho.
Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
30 Ngizayibonga kakhulu iNkosi ngomlomo wami; njalo ngizayidumisa phakathi kwabanengi.
Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 Ngoba izakuma ngakwesokunene komyanga, ukumsindisa kulabo abalahla umphefumulo wakhe.
Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.

< Amahubo 109 >