< UMakho 10 >
1 Wasesukuma lapho weza emingceleni yeJudiya edabula ngaphetsheya kweJordani; amaxuku asebuya abuthana kuye; wasephinda ukubafundisa, njengokwejwayela kwakhe.
Ndipo Yesu anachoka pamalowo ndi kupita kudera la Yudeya ndi kutsidya la mtsinje wa Yorodani. Magulu a anthu anabweranso kwa Iye, ndipo monga mwachizolowezi chake anawaphunzitsa.
2 Kwasekusiza kuye abaFarisi bambuza ukuthi: Kuvunyelwe yini ukuthi indoda yale umkayo? bemlinga.
Afarisi ena anabwera kudzamuyesa pomufunsa kuti, “Kodi malamulo amalola kuti mwamuna asiye mkazi wake?”
3 Wasephendula wathi kubo: UMozisi walilayani?
Iye anayankha kuti, “Kodi Mose anakulamulani chiyani?”
4 Basebesithi: UMozisi wavuma ukubhala incwadi yesehlukaniso, lokumala.
Iwo anati, “Mose amaloleza mwamuna kulemba kalata ya chisudzulo ndi kumuchotsa mkazi.”
5 UJesu wasephendula wathi kubo: Ngenxa yobulukhuni benhliziyo yenu walibhalela lumlayo;
Yesu anayankha kuti, “Mose anakulemberani lamulo ili chifukwa chakuwuma kwa mitima yanu.
6 kodwa kusukela ekuqaleni kokudaliweyo, uNkulunkulu wabenza owesilisa lowesifazana.
Koma pachiyambi cha chilengedwe, Mulungu ‘analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.’
7 Ngenxa yalokhu indoda izatshiya uyise lonina, inamathele kumkayo,
‘Pa chifukwa ichi mwamuna adzasiya abambo ake ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake,
8 njalo labo ababili bazakuba nyamanye. Ngakho kabasebabili, kodwa banyamanye.
ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.’ Potero sali awirinso, koma mmodzi.
9 Ngakho lokho uNkulunkulu akuhlanganisileyo, kakungabi lamuntu okwehlukanisayo.
Chifukwa chake chimene Mulungu wachilumikiza pamodzi, munthu wina asachilekanitse.”
10 Endlini abafundi bakhe basebebuya bembuza ngalokhu.
Pamene analinso mʼnyumba, ophunzira anamufunsa Yesu za izi.
11 Wasesithi kubo: Loba ngubani owala umkakhe athathe omunye, uyafeba kuye;
Iye anayankha kuti, “Aliyense amene aleka mkazi wake ndi kukakwatira wina achita chigololo kulakwira mkaziyo.
12 lomfazi uba esala indoda yakhe endele kwenye, uyafeba.
Ndipo akasiya mwamuna wake ndi kukakwatiwa ndi wina, achita chigololo.”
13 Basebeletha abantwana abancane kuye ukuze ababambe; kodwa abafundi bakhe babakhuza ababalethayo.
Anthu anabweretsa ana kwa Yesu kuti awadalitse, koma ophunzira anawadzudzula.
14 Kodwa uJesu ekubona wathukuthela, wathi kubo: Vumelani abantwana abancane beze kimi, lingabenqabeli. Ngoba umbuso kaNkulunkulu ungowabanje.
Pamene Yesu anaona zimenezi anayipidwa. Anati kwa iwo, “Lolani ana abwere kwa Ine, ndipo musawaletse, pakuti Ufumu wa Mulungu uli wa onga awa.
15 Ngiqinisile ngithi kini: Loba ngubani ongemukeli umbuso kaNkulunkulu njengomntwana omncane, kasoze angene kuwo.
Ndikukuwuzani choonadi, aliyense amene sadzalandira Ufumu wa Mulungu ngati kamwana sadzalowamo.”
16 Njalo ebagona, ebeka izandla zakhe phezu kwabo, wababusisa.
Ndipo ananyamula ana mʼmanja ake, ndi kuyika manja ake pa iwo nawadalitsa.
17 Esephumele endleleni, omunye wamgijimela, eguqa phambi kwakhe wambuza wathi: Mfundisi olungileyo, ngingenzani ukuze ngidle ilifa lempilo elaphakade? (aiōnios )
Yesu atanyamuka, munthu wina anamuthamangira nagwa mogwada pamaso pake. Iye anafunsa kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios )
18 UJesu wasesithi kuye: Ungibizelani ngokuthi olungileyo? Kakho olungileyo, ngaphandle koyedwa, uNkulunkulu.
Yesu anamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukunditchula wabwino? Palibe wabwino koma Mulungu yekha.
19 Uyayazi imilayo ethi: Ungafebi, ungabulali, ungebi, ungafakazi amanga, ungadlelezeli, hlonipha uyihlo lonyoko.
Iwe umadziwa malamulo: ‘Usaphe, usachite chigololo, usabe, usapereke umboni wonama, usachite chinyengo, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
20 Wasephendula wathi kuye: Mfundisi, lezizinto zonke ngizigcinile kusukela ebutsheni bami.
Iye anati, “Aphunzitsi zonsezi ndinazisunga kuyambira ndili mnyamata.”
21 Njalo uJesu emkhangela wamthanda, wathi kuye: Kunye okusweleyo; hamba, uthengise konke olakho, uphe abayanga, njalo uzakuba lokuligugu ezulwini; njalo uze, uthathe isiphambano, ungilandele.
Yesu anamuyangʼana ndi kumukonda nati, “Ukusowa chinthu chimodzi. Pita, kagulitse zonse zimene uli nazo ndipo kapereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Ndipo ukabwere ndi kunditsata Ine.”
22 Kodwa edanile ngalelilizwi wasuka wahamba edabukile; ngoba wayelempahla ezinengi.
Pa chifukwa ichi nkhope yake inagwa. Anachoka ali wachisoni, chifukwa anali ndi chuma chambiri.
23 UJesu wasethalaza wathi kubafundi bakhe: Kuzakuba lukhuni kangakanani kwabalenotho ukungena embusweni kaNkulunkulu.
Yesu anayangʼanayangʼana ndipo anati kwa ophunzira ake, “Nʼkovutadi kuti achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!”
24 Abafundi basebemangala ngamazwi akhe. Kodwa uJesu ephendula futhi wathi kubo: Bantwana, kulukhuni kangakanani kwabathembela enothweni ukungena embusweni kaNkulunkulu;
Ophunzira anadabwa ndi mawu ake. Koma Yesu anatinso, “Ananu, nʼkovutadi kulowa mu ufumu wakumwamba!
25 kulula ukuthi ikamela lithutshe entunjeni yenalithi, kulokuthi umuntu onothileyo angene embusweni kaNkulunkulu.
Ndi kwapafupi kwa ngamira kuti idzere pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kuti alowe mu ufumu wa Mulungu.”
26 Basebemangala kakhulukazi, bekhulumisana bathi: Pho kungasindiswa bani?
Ophunzira anadabwa kwambiri, ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
27 UJesu wasebakhangela wathi: Kubantu kakulakwenzeka, kodwa kakunjalo kuNkulunkulu; ngoba zonke izinto ziyenzeka kuNkulunkulu.
Yesu anawayangʼana ndipo anati, “Kwa munthu zimenezi nʼzosatheka, koma osati ndi Mulungu; zinthu zonse zimatheka ndi Mulungu.”
28 UPetro waseqala ukuthi kuye: Khangela, thina sitshiye konke, sakulandela.
Petro anati kwa Iye, “Ife tasiya zonse ndi kukutsatani!”
29 UJesu wasephendula wathi: Ngiqinisile ngithi kini: Kakukho muntu otshiye indlu, kumbe abafowabo, kumbe odadewabo, kumbe uyise, kumbe unina, kumbe umkakhe, kumbe abantwana, kumbe amasimu, ngenxa yami levangeli,
Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti palibe aliyense amene wasiya nyumba kapena abale kapena alongo kapena amayi kapena abambo kapena ana kapena minda chifukwa cha Ine ndi Uthenga Wabwino
30 ongayikwemukela ngokwekhulu khathesi ngalesisikhathi, izindlu labafowabo labodadewabo labonina labantwana lamasimu, kanye lokuzingelwa, lempilo elaphakade esikhathini esizayo. (aiōn , aiōnios )
adzalephera kulandira 100 (nyumba, abale, alongo, amayi, ana ndi minda, pamodzi ndi mazunzo) mʼbado uno ndi moyo wosatha nthawi ya mʼtsogolo. (aiōn , aiōnios )
31 Kodwa abanengi abokuqala bazakuba ngabokucina, labokucina ngabokuqala.
Koma ambiri amene ndi woyambirira adzakhala omalizira, ndipo omalizira adzakhala oyambirira.”
32 Njalo babesendleleni besenyukela eJerusalema; uJesu wayesehamba phambi kwabo, njalo babemangele, belandela babesesaba. Wasethatha futhi abalitshumi lambili, waqala ukubatshela izinto ezazizakwenzakala kuye
Ali pa ulendo wawo wopita ku Yerusalemu, Yesu ali patsogolo, ophunzira ake anadabwa, ndipo amene amamutsatira amachita mantha. Anatenganso ophunzira ake khumi ndi awiri pa mbali ndipo anawawuza zimene zikamuchitikire Iye.
33 ukuthi: Khangelani, senyukela eJerusalema, futhi iNdodana yomuntu izanikelwa kubapristi abakhulu lakubabhali, njalo bazayigwebela ukufa, bayinikele kwabezizwe,
Iye anati, “Ife tikupita ku Yerusalemu ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kwa akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo. Adzamuweruza kuti aphedwe ndipo adzamupereka kwa anthu a mitundu ina,
34 bazayiyangisa, bayitshaye ngesiswepu, bayikhafulele amathe, bayibulale; njalo ngosuku lwesithathu izabuya ivuke ekufeni.
amene adzamuchita chipongwe ndi kumuthira malovu, kumukwapula ndi kumupha. Patatha masiku atatu adzauka.”
35 Kwasekusiza kuye uJakobe loJohane, amadodana kaZebediya, besithi: Mfundisi, sithanda ukuthi usenzele loba yini esizayicela.
Ndipo Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anabwera kwa Iye ndipo anati, “Aphunzitsi, tikufuna kuti mutichitire ife chilichonse chimene tipemphe.”
36 Wasesithi kubo: Lithanda ukuthi ngilenzeleni?
Iye anafunsa kuti, “Kodi mukufuna ndikuchitireni chiyani?”
37 Basebesithi kuye: Siphe ukuthi sihlale omunye ngakwesokunene sakho lomunye ngakwesokhohlo sakho ebukhosini bakho.
Iwo anayankha kuti, “Timafuna kuti mmodzi wa ife adzakhale kumanja ndi wina kumanzere mu ulemerero wanu.”
38 Kodwa uJesu wathi kubo: Kalikwazi elikucelayo. Linganatha yini inkezo engiyinathayo mina, njalo libhabhathizwe ngobhabhathizo engibhabhathizwa ngalo mina?
Yesu anati, “Simukudziwa chimene mukupempha. Kodi mungamwere chikho chimene ndidzamwera kapena kubatizidwa ndi ubatizo umene ndibatizidwe nawo?”
39 Basebesithi kuye: Singakwenza. Kodwa uJesu wathi kubo: Isibili inkezo engiyinathayo mina lizayinatha; lizabhabhathizwa ngobhabhathizo engibhabhathizwa ngalo mina;
Iwo anayankha kuti, “Tikhoza.” Yesu anawawuza kuti, “Mudzamweradi chikho chimene Ine ndidzamwera, ndi kubatizidwa ndi ubatizo umene Ine ndidzabatizidwe nawo,
40 kodwa ukuhlala ngakwesokunene sami langakwesokhohlo sami kayisikho okwami ukukupha, kodwa kungokwalabo abakulungiselweyo.
koma kukhala kumanja kapena kumanzere si Ine wopereka. Malo awa ndi a amene anasankhidwiratu.”
41 Kwathi sebezwile abalitshumi baqala ukuthukuthela ngoJakobe loJohane.
Ophunzira khumiwo otsalawo atamva izi anapsera mtima Yakobo ndi Yohane.
42 Kodwa uJesu wababizela kuye wathi kubo: Liyazi ukuthi labo okuthiwa babusa izizwe bazibusa ngobulukhuni; lezikhulu zazo zisebenzisa amandla phezu kwazo.
Yesu anawayitana pamodzi nati, “Inu mukudziwa kuti iwo amene amadziyesa ngati atsogoleri a anthu amitundu ina amadyera anthu awo masuku pamutu. Akuluakulu awonso amaonetsadi mphamvu zawo pa iwo.
43 Kodwa akuyikuba njalo phakathi kwenu; kodwa loba ngubani othanda ukuba ngomkhulu phakathi kwenu, kabe yisisebenzi senu;
Sizili choncho ndi inu. Mʼmalo mwake, amene akufuna kukhala wamkulu pakati panu ayenera kukhala wotumikira,
44 njalo loba ngubani othanda ukuba ngowokuqala phakathi kwenu, kabe yisisebenzi sabo bonke.
ndipo aliyense amene akufuna kukhala wamkulu akhale kapolo wa onse.
45 Ngoba leNdodana yomuntu kayizanga ukukhonzwa, kodwa ukukhonza, lokunika impilo yayo ibe lihlawulo labanengi.
Pakuti ngakhale Mwana wa Munthu sanabwere kudzatumikiridwa, koma kudzatumikira, ndi kupereka moyo wake kuti ukhale dipo la anthu ambiri.”
46 Basebefika eJeriko; kwathi esephuma eJeriko, labafundi bakhe, lexuku elikhulu, indodana kaTimewu, uBartimewu oyisiphofu wayehlezi endleleni ephanza.
Ndipo anafika ku Yeriko. Pamene Yesu ndi ophunzira ake, pamodzi ndi gulu lalikulu la anthu, ankatuluka mu mzinda, munthu wosaona, Bartumeyu (mwana wa Tumeyu), amakhala mʼmbali mwa msewu ali kupempha.
47 Kwathi esezwile ukuthi nguJesu weNazaretha, waqala ukumemeza lokuthi: Jesu Ndodana kaDavida, akungihawukele!
Pamene anamva kuti anali Yesu wa ku Nazareti, anayamba kufuwula kuti, “Yesu, Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
48 Abanengi basebemkhuza ukuthi athule; kodwa wamemeza kakhulukazi, esithi: Ndodana kaDavida, akungihawukele!
Ambiri anamukalipira ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulitsabe kuti, “Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
49 UJesu esima wasesithi kabizwe; basebesibiza isiphofu, besithi kuso: Mana isibindi; sukuma, uyakubiza.
Yesu anayima nati, “Muyitaneni.” Ndipo anamuyitana kuti, “Kondwera! Imirira! Akukuyitana.”
50 Sasesilahla isembatho saso sasukuma seza kuJesu.
Anaponya mkanjo wake kumbali, analumpha nabwera kwa Yesu.
51 UJesu wasephendula wathi kuso: Ufuna ukuthi ngikwenzeleni? Isiphofu sasesisithi kuye: Raboni, ukuthi ngibuye ngibone.
Yesu anamufunsa kuti, “Ukufuna ndikuchitire chiyani?” Wosaonayo anayankha kuti, “Aphunzitsi, ndikufuna ndione.”
52 UJesu wasesithi kuso: Hamba; ukholo lwakho lukusindisile. Njalo sahle sabuye sabona, salandela uJesu endleleni.
Yesu anati, “Pita, chikhulupiriro chako chakuchiritsa!” Nthawi yomweyo anapenya, nʼkumatsatira Yesu pa ulendowo.