< Abahluleli 6 >

1 Abantwana bakoIsrayeli basebesenza okubi emehlweni eNkosi; iNkosi yasibanikela esandleni sikaMidiyani iminyaka eyisikhombisa.
Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Amidiyani kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
2 Lesandla sikaMidiyani saba lamandla phezu kukaIsrayeli. Ngenxa kaMidiyani abantwana bakoIsrayeli bazenzela imihume esezintabeni, lembalu, lezinqaba.
Amidiyani anapondereza Aisraeli. Tsono chifukwa cha Amidiyaniwa, Aisraeli anakonza malo obisalamo mʼmapiri ndi mʼmapanga. Anamanganso malinga.
3 Kwasekusithi uIsrayeli esehlanyele, enyuka amaMidiyani lamaAmaleki labantwana bempumalanga, benyuka bamelana labo,
Aisraeli amati akadzala mbewu, Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena akummawa amabwera ndi kudzawathira nkhondo.
4 bamisa inkamba maqondana labo, bachitha izithelo zelizwe, uze ufike eGaza, njalo kabatshiyanga okondlayo koIsrayeli loba imvu loba inkabi loba ubabhemi.
Iwo anamanga misasa mʼdzikomo ndi kuwononga zokolola zawo zonse mpaka ku Gaza, ndipo sanawasiyireko chamoyo chilichonse Aisraeliwo, kaya nkhosa kapena ngʼombe ndi bulu yemwe.
5 Ngoba bona benyuka lezifuyo zabo lamathente abo, bafika njengokugcwala kwentethe ngobunengi, okokuthi bona lamakamela abo babengelanani; basebengena elizweni ukulichitha.
Iwo ankabwera ndi zoweta zawo ndi matenti awo omwe. Ankabwera ambiri ngati dzombe, motero kuti kunali kovuta kuwawerenga anthuwo ndi ngamira zawo. Tsono iwo ankabwera ndi kuwononga dziko lonse.
6 UIsrayeli wasesiba ngumyanga kakhulu ngenxa yamaMidiyani, labantwana bakoIsrayeli bakhala eNkosini.
Aisraeli anasauka chifukwa cha Amidiyani ndipo analirira kwa Yehova kuti awathandize.
7 Kwasekusithi lapho abantwana bakoIsrayeli bekhala eNkosini ngenxa yamaMidiyani,
Pamene Aisraeli analirira kwa Yehova chifukwa cha Amidiyaniwo,
8 iNkosi yathuma umprofethi kubantwana bakoIsrayeli, owathi kibo: Itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu wakoIsrayeli: Mina ngalenyusa lisuka eGibhithe ngalikhupha endlini yobugqili,
Iye anawatumizira mneneri amene anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndine amene ndinakutsogolerani kuchokera ku Igupto. Ndinakutulutsani mʼdziko la ukapolo.
9 ngalihluthuna esandleni samaGibhithe, lesandleni sabo bonke abalicindezelayo, ngabaxotsha phambi kwenu, ngalinika ilizwe labo,
Ine ndinakupulumutsani ku ulamuliro wa Igupto komanso mʼmanja mwa amene amakuzunzani. Ndinawathamangitsa adani anu inu mukufika, ndikukupatsani dziko lawo.’
10 ngathi kini: NgiyiNkosi uNkulunkulu wenu; lingesabi onkulunkulu bamaAmori elihlala elizweni lawo. Kodwa kalililalelanga ilizwi lami.
Ndipo ndinakuwuzani kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musapembedze Milungu ya Aamori amene mukukhala mʼdziko lawo.’ Koma inu simunandimvere.”
11 Kwasekufika ingilosi yeNkosi, yahlala ngaphansi kwesihlahla se-okhi esiseOfira, esasingesikaJowashi umAbiyezeri, lendodana yakhe uGidiyoni yayibhula ingqoloyi esikhamelweni sewayini, ukuze iyifihlele amaMidiyani.
Tsiku lina mngelo wa Yehova anabwera ku Ofura ndi kukhala pansi pa tsinde pa mtengo wa thundu umene unali wa Yowasi Mwabiezeri. Tsono Gideoni, mwana wake nʼkuti pa nthawiyo akupuntha tirigu mʼmalo ofinyira mphesa mowabisalira Amidiyani.
12 Ingilosi yeNkosi yasibonakala kuye, yathi kuye: INkosi ilawe, qhawe elilamandla.
Tsono mngelo wa Yehova uja anamuonekera Gideoni nati kwa iye, “Yehova ali nawe, iwe munthu wamphamvu ndi wolimba mtima.”
13 UGidiyoni wasesithi kuyo: Hawu Nkosi yami, uba iNkosi ilathi, kungani konke lokhu kusehlele? Kanti zingaphi zonke izimangaliso zayo abasitshela zona obaba besithi: INkosi kayisenyusanga siphuma eGibhithe yini? Kodwa khathesi iNkosi isidelile, yasinikela esandleni samaMidiyani.
Gideoni anayankha, “Koma mbuye wanga, ngati Yehova ali nafedi, nʼchifukwa chiyani zonsezi zationekera? Nanga ntchito zake zodabwitsa zimene makolo athu anatiwuza pamene anati, ‘Yehova anatitulutsa ku dziko la Igupto,’ zili kuti? Koma tsopano Yehova watitaya ndi kutipereka mʼmanja mwa Amidiyani.”
14 INkosi yasiphendukela kuye yathi: Hamba ngalamandla akho, ukhulule uIsrayeli esandleni samaMidiyani. Kangikuthumanga yini?
Yehova anamuyangʼana namuwuza kuti, “Pita ndi mphamvu zomwe uli nazo, ukapulumutse Aisraeli mʼmanja mwa Amidiyani. Kodi si ndine amene ndakutuma?”
15 Wasesithi kuyo: Hawu Nkosi yami, ngizamkhulula ngani uIsrayeli? Khangela, usendo lwami lungumyanga koManase, njalo ngingomncinyane endlini kababa.
Koma Gideoni anafunsa kuti, “Kodi Ambuye anga ine ndingapulumutse bwanji Israeli? Mbumba yanga ndi yopanda mphamvu mu fuko la Manase, ndiponso ine ndine wamngʼono kwambiri mʼbanja mwa abambo anga.”
16 INkosi yasisithi kuye: Ngoba ngizakuba lawe, uzawatshaya-ke amaMidiyani njengendodanye.
Yehova anamuyankha kuti, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo Amidiyaniwo udzawagonjetsa ngati munthu mmodzi.”
17 Wasesithi kuyo: Uba khathesi ngithole umusa emehlweni akho, ngenzela isibonakaliso sokuthi nguwe okhuluma lami.
Gideoni anati, “Ngati tsopano mwandikomera mtima, ndionetseni chizindikiro kusonyeza kuti ndinudi mukuyankhula ndi ine.
18 Ake ungasuki lapha, ngize ngibuye kuwe, ngikhuphe isipho sami, ngisibeke phambi kwakho. Yasisithi: Mina ngizahlala uze uphenduke.
Chonde musachoke msanga mpaka nditabwerera kwa inu ndi chopereka changa cha chakudya kudzachipereka kwa inu.” Ndipo Yehova anamuwuza kuti, “Ine ndikudikira mpaka utabweranso.”
19 UGidiyoni wasengena, walungisa izinyane lembuzi, lezinkwa ezingelamvubelo nge-efa lempuphu, inyama wayifaka esitsheni, lomhluzi wawufaka embizeni, wakukhuphela kuyo ngaphansi kwesihlahla se-okhi, wakusondeza.
Gideoni analowa mʼnyumba, ndipo anakakonza mwana wambuzi, nakonzanso makeke wopanda yisiti a ufa wa makilogalamu khumi. Nayika nyamayo mʼdengu ndipo msuzi wake anawuthira mu mʼphika. Anabwera nazo ndi kukazipereka kwa mngelo uja pa tsinde pa mtengo wa thundu paja.
20 Ingilosi kaNkulunkulu yasisithi kuye: Thatha inyama lezinkwa ezingelamvubelo, ukubeke phezu kwalelidwala, ubusuthela umhluzi. Wasesenza njalo.
Mngelo wa Mulungu anamuwuza iye kuti, “Tenga nyamayi pamodzi ndi makekewa, uziyike pa mwala uwu ndi kuthirapo msuziwu.” Ndipo Gideoni anatero.
21 Ingilosi yeNkosi yasiselula isihloko somqwayi owawusesandleni sayo, yathinta inyama lezinkwa ezingelamvubelo; kwasekusenyuka umlilo uphuma edwaleni, wadla inyama lezinkwa ezingelamvubelo. Lengilosi yeNkosi yasuka emehlweni akhe.
Mngelo wa Yehova anatenga msonga ya ndodo imene inali mʼmanja mwake nakhudza nayo nyama ndi makeke aja. Nthawi yomweyo moto unabuka pa thanthwepo ndi kupsereza nyama yonse ndi makeke aja. Ndipo mngelo wa Yehova sanaonekenso.
22 UGidiyoni wasebona ukuthi yayiyingilosi yeNkosi. UGidiyoni wathi: Maye, Nkosi Jehova! Ngenxa yokuthi ngibone ingilosi yeNkosi ubuso ngobuso.
Apo Gideoni anazindikira kuti analidi mngelo wa Ambuye, ndipo anati, “Kalanga ine Yehova Wamphamvuzonse! Ine ndaona mngelo wa Yehova ndi maso!”
23 Kodwa iNkosi yathi kuye: Ukuthula kakube kuwe, ungesabi, kawuyikufa.
Koma Yehova anamuwuza kuti, “Mtendere ukhale ndi iwe! Usachite mantha, sufa ayi.”
24 UGidiyoni waseyakhela iNkosi ilathi lapho, walibiza ngokuthi uJehova-shalomi. Kuze kube lamuhla lisesekhona eOfira lamaAbiyezeri.
Choncho Gideoni anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo analitcha kuti, Yehova ndiye mtendere. Kufikira lero lino guwali lilipo ku Ofura wa Mwabiezeri.
25 Kwasekusithi ngalobobusuku iNkosi yathi kuye: Thatha ijongosi lenkunzi engekayihlo, ngitsho ijongosi lesibili elileminyaka eyisikhombisa, udilize ilathi likaBhali elingelikayihlo, lesixuku esiphansi kwalo usigamule;
Usiku womwewo Yehova anati kwa Gideoni, “Tenga ngʼombe ya mphongo ya abambo ako, ngʼombe ina yachiwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ugwetse guwa la Baala limene abambo ako ali nalo, ndi kugwetsanso fano la Asera limene lili pafupi pake.
26 wakhele iNkosi uNkulunkulu wakho ilathi phezu kwengqonga yalinqaba, njengokwejwayelekileyo; ubusuthatha ijongosi lesibili, unikele umnikelo wokutshiswa ngenkuni zesixuku ozasigamula.
Kenaka umangire Yehova Mulungu wako guwa lansembe ndi miyala yoyala bwino pamwamba pa chiwunda chimenecho. Utenge ngʼombe ya mphongo yachiwiri ija ndipo uyipereke ngati nsembe yopsereza pogwiritsa ntchito mitengo ya fano la Asera imene udule ngati nkhunizo.”
27 UGidiyoni wasethatha amadoda alitshumi ezincekwini zakhe, wenza njengokutsho kweNkosi kuye; kodwa kwathi ngenxa yokuthi wayesesaba indlu kayise lamadoda omuzi ukukwenza emini, wakwenza ebusuku.
Choncho Gideoni anatenga antchito ake khumi nachita monga Yehova anamuwuzira. Ndipo popeza ankaopa anthu a pa banja lake ndiponso anthu a mʼmudzimo sanachite zimenezi masana koma usiku.
28 Lapho amadoda omuzi evuka ekuseni kakhulu, khangela, ilathi likaBhali lalidiliziwe, lesixuku esasiphansi kwalo sesiganyuliwe, lejongosi lesibili lanikelwa phezu kwelathi elaselakhiwe.
Anthu a mu mzindamo atadzuka mʼmamawa anangoona guwa la Baala litagwetsedwa ndi fano la Asera limene linali pamwamba pake litadulidwa ndiponso ngʼombe yamphongo yachiwiri ija itaperekedwa ngati nsembe yopsereza pa guwa limene linamangidwa lija.
29 Basebesithi omunye komunye: Ngubani owenze loludaba? Nxa sebedingile bebuza bathi: UGidiyoni indodana kaJowashi wenze loludaba.
Iwo anafunsana wina ndi mnzake, “Wachita zimenezi ndani?” Atafufuza ndi kufunsafunsa, analingalira kuti, “Gideoni mwana wa Yowasi ndiye wachita zimenezi.”
30 Amadoda omuzi asesithi kuJowashi: Khupha indodana yakho ukuze ife, ngoba idilizile ilathi likaBhali, langoba igamule isixuku esasiphansi kwalo.
Ndipo anthuwo anawuza Yowasi kuti, “Tulutsa mwana wako, ayenera kufa chifukwa wagumula guwa lansembe la Baala ndipo wadula fano la Asera lomwe linali pamwamba pake.”
31 Kodwa uJowashi wathi kubo bonke ababemi ngakuye: Lina lizamlwela uBhali yini, kumbe lina limsindise? Omlwelayo uzabulawa kusesekuseni. Uba engunkulunkulu, kazilwele, ngoba ilathi lakhe lidiliziwe.
Koma Yowasi anawuza anthu amene anamuzungulirawo kuti, “Kodi inu mukuti mukhale woyankhulira Baala mlandu? Kodi ndinu amene mukuti mumupulumutse? Amene akufuna kumumenyera nkhondo Baala akhala atafa pofika mmawa! Ngati Baalayo ndi mulungudi, musiyeni adzimenyere yekha nkhondo popeza munthu wina wamugwetsera guwa lansembe lake.”
32 Ngakho ngalolosuku wambiza ngokuthi nguJerubali, esithi: UBhali kalwe laye, ngoba ulidilizile ilathi lakhe.
Choncho tsiku limenelo Gideoni anatchedwa, Yeru-Baala, kutanthauza kuti, “Baala alimbana naye, popeza anagwetsa guwa lake la nsembe.”
33 Lawo wonke amaMidiyani lamaAmaleki labantwana bempumalanga babuthana ndawonye, bachapha, bamisa inkamba esigodini seJizereyeli.
Tsopano Amidiyani, Amaleki ndi anthu ena akummawa anasonkhana ndipo atawoloka Yorodani anakamanga zinthando za nkhondo ku chigwa cha Yezireeli.
34 LoMoya weNkosi wembesa uGidiyoni; wavuthela uphondo, lamaAbiyezeri abizwa emva kwakhe.
Ndipo Mzimu wa Yehova unatsikira pa Gideoni, ndipo anayimba lipenga kuyitana Abiezeri kuti amutsatire iye.
35 Wasethuma izithunywa kuye wonke uManase, labo futhi babizwa emva kwakhe. Wasethuma izithunywa koAsheri lakoZebuluni lakoNafithali; basebesiza ukubahlangabeza.
Iye anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Manase kuti akamenye nkhondo ndipo Amanase anayitanidwanso kuti amutsate. Anatumanso amithenga kwa Aseri, Azebuloni ndi Anafutali, ndipo onsewo anapita kukakumana naye.
36 UGidiyoni wasesithi kuNkulunkulu: Uba uzasindisa uIsrayeli ngesandla sami njengokutsho kwakho,
Gideoni anati kwa Mulungu, “Ngati mudzapulumutsa Israeli ndi dzanja langa monga mwalonjezeramu,
37 khangela, ngizabeka uboya bezimvu obugundiweyo ebaleni lokubhulela; uba amazolo ezakuba phezu koboya obugundiweyo kuphela, lokoma emhlabathini wonke, ngizakwazi-ke ukuthi uzamsindisa uIsrayeli ngesandla sami, njengokutsho kwakho.
onani, ine ndiyala ubweya wankhosa pa malo opunthira tirigu. Ngati mame adzagwera pa ubweya wankhosa pokhapa, pa nthaka ponse pakhala powuma, ndiye ndidziwa kuti mudzapulumutsadi Israeli ndi dzanja langa monga mwanenera.”
38 Kwasekusiba njalo. Lapho evuka ngovivi kusisa, wacindezela uboya obugundiweyo, wakhama amazolo eboyeni obugundiweyo, umganu ogcwele amanzi.
Ndipo zimenezi zinachitikadi. Gideoni atadzuka mʼmamawa ndi kuwufinya ubweya uja, anafinya madzi odzaza mtsuko.
39 UGidiyoni wasesithi kuNkulunkulu: Ulaka lwakho lungangivutheli, ngizakhuluma khathesi kuphela; ake ngihlole khathesi kuphela ngoboya obugundiweyo; ake kube lokoma eboyeni obugundiweyo kuphela, lemhlabathini wonke kakube lamazolo.
Kenaka Gideoni anati kwa Mulungu, “Musandikwiyire. Mundilole ndiyankhule kamodzi kokhaka. Ndiyeseko kamodzi kokha ndi ubweyawu kuti pa ubweya pokhapa pakhale powuma koma pa nthaka ponse pakhale ponyowa ndi mame.”
40 UNkulunkulu wasesenza njalo ngalobobusuku; ngoba kwaba lokoma eboyeni obugundiweyo kuphela, kodwa emhlabathini wonke kwaba lamazolo.
Ndipo Mulungu anachita zomwezo usiku umenewo. Pa ubweya pokha panali powuma, koma pa nthaka ponse panagwa mame.

< Abahluleli 6 >