< UJoshuwa 2 >

1 UJoshuwa indodana kaNuni wasethuma eseShithimi amadoda amabili aba zinhloli ensitha, esithi: Hambani libone ilizwe, leJeriko. Asehamba, ayafikela endlini yomfazi, iwule, obizo lakhe lalinguRahabi, alala khona.
Tsono Yoswa mwana wa Nuni anatuma anthu awiri okazonda dziko mwachinsinsi kuchokera ku Sitimu. Iye anawawuza kuti, “Pitani mukaone dzikolo makamaka mzinda wa Yeriko.” Kotero iwo anapita ndipo anakafika ku nyumba ya mkazi wadama dzina lake Rahabe, ndipo anagona kumeneko.
2 Kwatshelwa inkosi yeJeriko kwathiwa: Khangela, kufike lapha ebusuku amadoda abantwana bakoIsrayeli ukuhlola ilizwe.
Mfumu ya Yeriko inawuzidwa kuti, “Aisraeli ena afika mu mzinda muno usiku uno kudzazonda dziko.”
3 Inkosi yeJeriko yasithumela kuRahabi isithi: Khupha lawo amadoda afikele kuwe, angena endlini yakho, ngoba azehlola ilizwe lonke.
Choncho Mfumu ya Yeriko inatumiza uthenga kwa Rahabe kuti, “Atulutse anthu amene abwera ku nyumba kwakowo chifukwa iwo abwera kuti adzazonde dzikoli.”
4 Kodwa owesifazana wayethethe lawomadoda amabili, wawafihla, wakhuluma kanje: Afikile kimi amadoda, kodwa bengingazi lapha avela khona.
Koma pa nthawiyi nʼkuti mkaziyo atatenga amuna awiriwo ndi kuwabisa. Tsono anayankha kuti, “Inde, anthuwo anafikadi ku nyumba kuno. Koma sindinadziwe kumene anachokera.
5 Kwasekusithi sekuzavalwa isango lapho sekumnyama amadoda aphuma. Kangikwazi lapho amadoda aye khona; axhumeni ngokuphangisa liwalandele, ngoba lizawafica.
Iwo achoka kuno ndi chisisira, chipata cha mzinda chili pafupi kutsekedwa. Ndiye sindidziwa kumene alowera. Koma mukawalondola msanga muwapeza.”
6 Kodwa yena wayewenyusele ephahleni, wawafihla phakathi kwamahlanga efilakisi ayechayelwe yena ephahleni.
Koma nʼkuti atawakweza pa denga azondiwo ndi kuwabisa pansi pa mapesi a thonje amene iye anawayika pa dengapo.
7 Amadoda asewaxhuma ngendlela yeJordani aze afika emazibukweni; bavala amasango emva kokuphuma kwabawaxhumayo bewalandela.
Nthumwi za mfumu zija zitatuluka ndipo chipata chinatsekedwa. Nthumwizo zinapita kukawafunafuna azondi aja mpaka ku dooko la Yorodani.
8 Kwathi wona engakalali, yena wenyukela kuwo ephahleni;
Azondiwo asanagone, Rahabe anakwera pa denga
9 wasesithi emadodeni: Ngiyazi ukuthi iNkosi ilinikile ilizwe, lokuthi ukwesabeka kwenu kuwele phezu kwethu, lokuthi bonke abakhileyo elizweni bayancibilika ngenxa yobukhona benu.
ndipo anawawuza kuti, “Ine ndikudziwa kuti Yehova wakupatsani dziko lino ndipo tili ndi mantha. Anthu onse a mʼdziko lino ali ndi mantha chifukwa cha inu.
10 Ngoba sizwile ukuthi iNkosi yomisa amanzi oLwandle oluBomvu phambi kwenu ekuphumeni kwenu eGibhithe, lalokho elakwenza emakhosini amabili amaAmori ayengaphetsheya kweJordani, uSihoni loOgi elabatshabalalisayo.
Ife tinamva mmene Yehova anawumitsira madzi a Nyanja Yofiira inu mukufika pamene munatuluka mʼdziko la Igupto. Tamvanso zimene munachita kwa Sihoni ndi Ogi, mafumu awiri a Aamori amene ali kummawa kwa Yorodani. Inu munawawononga kotheratu.
11 Sathi sikuzwa lokho inhliziyo yethu yancibilika, kakusekho isibindi emuntwini ngenxa yenu. Ngoba iNkosi uNkulunkulu wenu, nguye uNkulunkulu emazulwini phezulu lemhlabeni phansi.
Titamva zimenezi, ife tinataya mtima ndipo aliyense wa ife ali ndi mantha chifukwa cha inu. Tikudziwa kuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa kumwamba ndi dziko lapansi.
12 Ngakho-ke ake lifunge kimi ngeNkosi, ngoba ngilenzele umusa, lani-ke lizayenzela umusa indlu kababa, linginike isiboniso esiqinileyo,
Choncho mulumbire pamaso pa Yehova ndi kundipatsa chizindikiro choti mudzachitadi zimene mwalonjeza, kuti monga inu ndakuchitirani chifundo, inunso mudzachitira chifundo a pa banja la abambo anga.
13 ukuthi ligcine bephila ubaba lomama, labanewethu labodadewethu, lakho konke abalakho, likhulule impilo yethu ekufeni.
Inu mulonjeze kuti simudzapha abambo anga ndi amayi anga, abale anga ndi alongo anga ndi mabanja awo omwe.”
14 Lamadoda athi kuye: Umphefumulo wethu ufe esikhundleni senu, uba ungavezi obala loludaba lwethu. Njalo kuzakuthi lapho iNkosi isisinikile ilizwe, sizakwenzela umusa leqiniso.
Anthuwo anamuyankha kuti, “Ife ndife okonzeka kufa chifukwa cha inu. Ngati iwe sudzawulula zimene tachitazi, ndiye kuti ife tidzakukomera mtima ndi kusunga pangano lathu ndi iwe, Yehova akadzatipatsa dziko lino.”
15 Wasewehlisa ngentambo ewindini, ngoba indlu yakhe yayisemdulini womuzi, wayehlala phezu komduli.
Popeza nyumba ya Rahabe inali pa linga la mzindawo, azondi aja anatulukira pa zenera. Rahabe anawatsitsa pansi ndi chingwe.
16 Wasesithi kuwo: Yanini entabeni, hlezi abaxhumi bahlangane lani, licatshe khona insuku ezintathu, baze babuye abaxhumi, lemva kwalokho lihambe ngendlela yenu.
Iye anawawuza kuti, “Pitani ku mapiri kuti okuthamangiraniwo asakupezeni. Mukabisale kumeneko masiku atatu mpaka iwo atabwerera, ndipo kenaka muzikapita kwanu.”
17 Amadoda asesithi kuye: Thina sizakhululeka esifungweni sakho lesi osifungise sona.
Anthuwo anati kwa iye, “Lonjezo limene watichititsa ifeli tidzalisungadi
18 Khangela, ekufikeni kwethu elizweni uzabophela lintambo yomnxeba obomvu ewindini osehlise ngalo, njalo uzibuthanisele endlini yakho oyihlo lonyoko labanewenu lendlu yonke kayihlo.
tikadzalowa mʼdzikoli, iwe udzamangirire kansalu kofiira pa zenera limene unatitulutsira, ndi kusonkhanitsa abambo ako, amayi ako, abale ako ndi banja lako lonse mʼnyumba muno.
19 Kuzakuthi-ke, loba ngubani ophumela phandle kweminyango yendlu yakho, igazi lakhe lizakuba phezu kwekhanda lakhe, thina-ke sizakuba singelacala. Njalo loba ngubani ozakuba lawe endlini, igazi lakhe lizakuba sekhanda lethu, uba isandla sisiba phezu kwakhe.
Ngati wina aliyense adzatuluka mʼnyumbamo kuti azikayendayenda mu msewu, magazi ake adzakhala pamutu pake, ife sitidzapalamula kanthu. Koma wina aliyense wokhala mʼnyumba mwakomo akadzaphedwa, mlandu udzakhala wathu.
20 Kodwa uba uluveza obala loludaba lwethu, sizakhululeka esifungweni sakho osifungise sona.
Komanso iwe ukangowulula zimene ife tikuchitazi ndiye kuti ife sitidzasunga zimene talonjezazi.”
21 Wasesithi: Njengamazwi enu, kakube njalo. Wasewayekela ehamba, ahamba, wabophela intambo ebomvu ewindini.
Rahabe anayankha kuti, “Zikhale monga mwaneneramo.” Kenaka iye anawatulutsa ndipo iwowo anapita. Pambuyo pake Rahabe anamangirira kansalu kofiira pa zenera paja.
22 Asehamba afika entabeni, ahlala khona insuku ezintathu, baze babuya abaxhumi, ngoba abaxhumi bawadinga endleleni yonke, kodwa kabawatholanga.
Azondi aja anachoka napita ku mapiri ndipo anakhalako masiku atatu. Apa nʼkuti otumidwa ndi mfumu aja atawafunafuna ponseponse nʼkubwerera osawapeza.
23 Ngakho amadoda womabili aphenduka asesehla entabeni, achapha, afika kuJoshuwa indodana kaNuni, amtshela konke okuwehleleyo.
Pambuyo pake azondi awiri aja anayamba ulendo wobwerera kwawo. Anatsika ku mapiri kuja, nawoloka mtsinje mpaka anakafika kwa Yoswa mwana wa Nuni. Ndipo anamuwuza zonse zimene zinawachitikira.
24 Athi kuJoshuwa: Isibili iNkosi ilinikele esandleni sethu ilizwe lonke, futhi-ke bonke abakhileyo belizwe bancibilikile ngenxa yobukhona bethu.
Iwo anati kwa Yoswa, “Ndithu, Yehova wapereka dziko lonse mʼmanja mwathu. Anthu onse kumeneko akuchita nafe mantha.”

< UJoshuwa 2 >