< U-Isaya 53 >
1 Ngubani okholwe umbiko wethu? Njalo ingalo yeNkosi yembulelwe bani?
Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
2 Ngoba uzakhula phambi kwakhe njengesihlahla esibuthakathaka, lanjengempande emhlabathini owomileyo; kalasimo kumbe ubuhle; lapho simbona, kalakubukeka ukuthi simloyise.
Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
3 Uyeyiswa njalo udelelwa ngabantu; umuntu wezinsizi, njalo ejwayele inhlungu; kwangathi sifihla ubuso kuye; weyiswa, kasimnanzanga.
Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
4 Isibili yena wathwala inhlungu zethu, waphatha insizi zethu; kanti thina sathi ujezisiwe, utshayiwe nguNkulunkulu, njalo uhlutshiwe.
Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
5 Kodwa walinyazwa ngenxa yeziphambeko zethu, wachotshozwa ngenxa yobubi bethu; ukujeziswa kokuthula kwethu kwakuphezu kwakhe, langemivimvinya yakhe thina sisilisiwe.
Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
6 Thina sonke njengezimvu siduhile; saphendukela ngulowo lalowo endleleni yakhe; njalo iNkosi yehlisele phezu kwakhe ububi bethu sonke.
Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
7 Wacindezelwa njalo yena wahlutshwa, kube kanti kawuvulanga umlomo wakhe; walethwa ekuhlatshweni njengewundlu, lanjengemvu ithule phambi kwabagundi bayo, laye kawuvulanga umlomo wakhe.
Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
8 Wasuswa ekucindezelweni lekwahlulelweni; njalo ngubani ongakhuluma ngesizukulwana sakhe? Ngoba waqunywa wasuswa elizweni labaphilayo; ngenxa yesiphambeko sabantu bami watshaywa.
Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
9 Wenza ingcwaba lakhe kanye lababi, njalo kanye lonothileyo ekufeni kwakhe; ngoba engenzanga okubi, njalo kungekho inkohliso emlonyeni wakhe.
Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
10 Kanti kwayithokozisa iNkosi ukumchoboza, yamenza adabuke. Lapho uzakwenza umphefumulo wakhe umnikelo wesono, uzabona inzalo yakhe, elule izinsuku zakhe, lentokoziso yeNkosi izaphumelela esandleni sakhe.
Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
11 Uzabona okuvela ekuhluphekeni komphefumulo wakhe, eneliswe; ngolwazi lwayo, inceku yami elungileyo izalungisisa abanengi, ngoba yona izathwala ububi babo.
Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
12 Ngakho ngizayabela kanye labakhulu, yabelane impango kanye labalamandla; ngoba yathulula umphefumulo wayo ekufeni, yabalwa ndawonye labaphambeki; njalo yona yathwala isono sabanengi, yalabhelela abaphambeki.
Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.