< U-Isaya 50 >
1 Itsho njalo iNkosi: Ingaphi incwadi yesehlukaniso kanyoko engamlahla ngayo? Loba ngubani kubakweledisi bami engilithengise kuye? Khangelani, lathengiswa ngenxa yobubi benu, langenxa yeziphambeko zenu unyoko walahlwa.
Yehova akuti, “Kalata imene ndinasudzulira amayi anu ili kuti? Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole, ndinakugulitsani kwa ati? Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu; amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.
2 Kungani ekufikeni kwami kwakungelamuntu? Ngibiza, kodwa engekho ophendulayo? Isandla sami sifinyeziwe lokufinyezwa yini ukuthi singehlenge? Kumbe kakulamandla kimi okukhulula yini? Khangela ngokukhuza kwami ngomisa ulwandle, ngenza imifula ibe yinkangala; izinhlanzi zayo zibe levumba ngoba kungelamanzi, zife ngenxa yokoma.
Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu? Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha? Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani? Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani? Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu, mitsinje ndinayisandutsa chipululu; nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi; ndipo zinafa ndi ludzu.
3 Ngigqokisa amazulu ngobumnyama, ngenze isaka libe yisembeso sawo.
Ndinaphimba thambo ndi mdima ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”
4 INkosi uJehova inginike ulimi lwabafundileyo, ukuze ngazi ukukhuluma ilizwi ngesikhathi esifaneleyo kokhatheleyo. Iyavuka ukusa ngokusa; ivusa indlebe yami, ukuze ngizwe njengabafundileyo.
Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka. Mmawa mulimonse amandidzutsa, amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.
5 INkosi uJehova ivule indlebe yami, njalo mina kangibanga lenkani, kangibuyelanga emuva.
Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga, ndipo sindinakhale munthu wowukira ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.
6 Nganika umhlana wami kubatshayi, lezihlathi zami kulabo abacutha indevu; kangifihlanga ubuso bami ehlazweni elikhulu lamathe.
Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu; sindinawabisire nkhope yanga anthu ondinyoza ndi ondilavulira.
7 Ngoba iNkosi uJehova izangisiza; ngakho-ke kangiyangiswa; ngakho-ke ngimise ubuso bami njengensengetshe, njalo ngiyazi ukuthi kangiyikuyangeka.
Popeza Ambuye Yehova amandithandiza, sindidzachita manyazi. Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi, chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.
8 Useduze yena ongilungisisayo. Ngubani ongalwisana lami? Kasime ndawonye. Ngubani ummangaleli wami? Kasondele kimi.
Wondikhalira kumbuyo ali pafupi, ndaninso amene adzandiyimba mlandu? Abwere kuti tionane maso ndi maso! Mdani wanga ndi ndani? Abweretu kuti tilimbane!
9 Khangela, iNkosi uJehova izangisiza; ngubani ozangilahla? Khangela, bonke bazaguga njengesembatho; inundu izabadla.
Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza. Ndaninso amene adzanditsutsa? Onse adzatha ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
10 Ngubani phakathi kwenu oyesabayo iNkosi, olalela ilizwi lenceku yayo, ohamba emnyameni, njalo engelakukhanya? Kathembele ebizweni leNkosi, eyame kuNkulunkulu wakhe.
Ndani mwa inu amaopa Yehova ndi kumvera mawu a mtumiki wake? Aliyense woyenda mu mdima, popanda chomuwunikira, iye akhulupirire dzina la Yehova ndi kudalira Mulungu wake.
11 Khangelani, lina lonke eliphemba umlilo, elizigombolozela ngenhlansi: Hambani ekukhanyeni komlilo wenu, lenhlansini elizibasileyo. Lokhu kuzakwenzakala kini kuvela esandleni sami; lizalala phansi ngobuhlungu.
Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu, lowani mʼmoto wanu womwewo. Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa. Ndipo ine Yehova ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.