< UDutheronomi 1 >

1 La ngamazwi uMozisi awakhuluma kuIsrayeli wonke nganeno kweJordani enkangala, egcekeni eliqondene leSufi, phakathi kweParani leTofeli leLabani leHazerothi leDizahabi.
Awa ndi mawu amene Mose anayankhula kwa Aisraeli onse mʼchipululu kummawa kwa Yorodani, ku Araba moyangʼanana ndi Sufi, pakati pa Parani ndi Tofeli, Labani, Heziroti ndi Dizahabu.
2 Kulensuku ezilitshumi lanye kusukela eHorebe ngendlela yentaba yeSeyiri kusiya eKadeshi-Bhaneya.
(Kuyenda kuchokera ku Horebu kukafika ku Kadesi Barinea kudzera njira ya ku Phiri la Seiri ndi ulendo wa masiku khumi ndi limodzi).
3 Kwasekusithi ngomnyaka wamatshumi amane, ngenyanga yetshumi lanye, ngolokuqala lwenyanga, uMozisi wakhuluma kubantwana bakoIsrayeli njengakho konke iNkosi eyamlaya ngakho kubo,
Mʼchaka cha makumi anayi, pa tsiku loyamba la mwezi 11, Mose anafotokozera Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamula zokhudza iwowo.
4 esemtshayile uSihoni inkosi yamaAmori owayehlala eHeshiboni, loOgi inkosi yeBashani owayehlala eAshitarothi eEdreyi.
Apa nʼkuti atagonjetsa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni, ndipo pa Ederi anagonjetsa Ogi mfumu ya ku Basani, amene amalamulira mu Asiteroti.
5 Nganeno kweJordani, elizweni lakoMowabi, uMozisi waqala ukuchasisa lumlayo esithi:
Chakummawa kwa Yorodani mʼchigawo cha Mowabu, Mose anayamba kufotokozera lamulo ili kunena kuti:
6 INkosi uNkulunkulu wethu yakhuluma kithi eHorebe isithi: Selihlale isikhathi eseneleyo kulintaba.
Ku Horebu, Yehova Mulungu wathu anati kwa ife, “Mwakhalitsa pa phiri lino.
7 Phendukani lisuke, liye entabeni yamaAmori, lendaweni ezakhelene lawo, egcekeni, entabeni, lesihotsheni, leningizimu, lekhunjini lolwandle, ilizwe lamaKhanani, leLebhanoni, kuze kube semfuleni omkhulu, umfula iYufrathi.
Sasulani msasa ndipo pitani ku dziko la mapiri la Aamori. Pitani kwa anthu onse oyandikana nawo ku Araba, ku mapiri, mʼmbali mwa mapiri a ku madzulo, ku Negevi ndiponso mʼmbali mwa nyanja, ku dziko la Akanaani ndi ku Lebanoni mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate.
8 Bonani, ngibeke ilizwe phambi kwenu. Ngenani, lidle ilifa lelizwe iNkosi eyalifungela oyihlo, oAbrahama, uIsaka, loJakobe, ukubanika lona lenzalo yabo emva kwabo.
Taonani, Ine ndakupatsani dziko ili. Lowani ndi kulilanda dziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo komanso kwa zidzukulu zawo.”
9 Njalo ngakhuluma kini ngalesosikhathi ngisithi: Kangilakulithwala ngingedwa.
Pa nthawi imeneyi ine ndinati kwa inu, “Inu ndinu katundu olemera kwambiri woti sindingathe kumunyamula ndekha.
10 INkosi uNkulunkulu wenu ilandisile, khangelani-ke, lamuhla linjengenkanyezi zamazulu ngobunengi.
Yehova Mulungu wanu wakuchulukitsani kotero kuti lero lino ndinu ochuluka ngati nyenyezi za kumwamba.
11 INkosi, uNkulunkulu waboyihlo, kayandise kini, njengoba linjalo, ngokuphindwe kankulungwane, ilibusise, njengokukhuluma kwayo kini.
Yehova Mulungu wa makolo anu wachulukitsa chiwerengero chanu ndipo wakudalitsani monga momwe analonjezera!
12 Ngingedwa ngingathwala njani ubunzima benu lomthwalo wenu lenkani yenu?
Koma nanga ndekha ndidzasenza bwanji zovuta ndi zipsinjo zanu komanso milandu yanu?
13 Zithatheleni amadoda ahlakaniphileyo, azwisisayo, laziwayo ezizweni zenu, ngiwabeke-ke abe zinhloko zenu.
Sankhani amuna ena anzeru, ozindikira ndi amene mumawalemekeza kuchokera ku mtundu uliwonse wa mitundu yanu, ndipo ndidzawayika kuti akulamulireni.”
14 Laselingiphendula lisithi: Ilizwi olikhulumileyo lilungile ukulenza.
Inu munandiyankha kuti, “Maganizo amenewa ndi abwino kuwachita.”
15 Ngasengithatha inhloko zezizwe zenu, amadoda ahlakaniphileyo, aziwayo, ngawabeka aba zinhloko phezu kwenu, induna zezinkulungwane, lenduna zamakhulu, lenduna zamatshumi amahlanu, lenduna zamatshumi, leziphathamandla zezizwe zenu.
Choncho ndinatenga anthu otsogolera mafuko anu, anzeru ndi omwe mumawalemekeza, ndipo ndinawayika kuti azikulamulirani mʼmagulu a 1,000, ena 100, ena makumi asanu ndi ena khumi, kuti akhalenso ngati akapitawo a mafuko.
16 Ngasengilaya abahluleli benu ngalesosikhathi ngisithi: Zwanini okuphakathi kwabafowenu, lahlulele ngokulunga phakathi komuntu lomfowabo lowezizweni okuye.
Ndipo pa nthawi imeneyo ndinawawuza olamula anu kuti, “Muzimva milandu ya pakati pa abale anu ndi kuweruza mosakondera, kaya mlanduwo uli pakati pa Aisraeli okhaokha kapena mmodzi wa iwo ndi mlendo.
17 Lingakhangeli ubuso ekwahluleleni, zwanini omncinyane njengomkhulu; lingesabi ubuso bomuntu, ngoba ukwahlulela kungokukaNkulunkulu. Lendaba elukhuni kini lizayiletha kimi, besengiyizwa.
Osamayangʼana nkhope poweruza koma muzimvetsera aangʼono ndi aakulu omwe chimodzimodzi. Musamaope munthu aliyense, pakuti chiweruzo ndi cha Mulungu. Muzindibweretsera mlandu uliwonse wovuta ndipo ndidzaumva.”
18 Langalesosikhathi ngalilaya zonke izinto elifanele ukuzenza.
Ndipo nthawi imeneyo ndinakuwuzani chilichonse chimene munayenera kuchita.
19 Sasesisuka eHorebe, sahamba kuyo yonke leyonkangala enkulu leyesabekayo elayibonayo ngendlela yentaba yamaAmori, njengokusilaya kweNkosi uNkulunkulu wethu, saze safika eKadeshi-Bhaneya.
Tsono monga Yehova Mulungu wathu anatilamulira, tinanyamuka kuchoka ku Horebu ndi kupita cha ku dziko lamapiri la Aamori kudzera ku chipululu chachikulu ndi choopsa chija munachionachi, kotero kuti tinakafika ku Kadesi Barinea.
20 Ngasengisithi kini: Selifikile entabeni yamaAmori iNkosi uNkulunkulu wethu ezasinika yona.
Ndipo ndinati kwa inu, “Mwafika ku dziko la mapiri la Aamori, limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa.
21 Bona, iNkosi uNkulunkulu wakho ilinikile ilizwe phambi kwakho; yenyuka udle ilifa lalo, njengokutsho kweNkosi uNkulunkulu waboyihlo kuwe; ungesabi, ungadideki.
Taonani, Yehova Mulungu wanu wakupatsani dzikoli. Pitani ndi kulitenga monga Yehova, Mulungu wa makolo anu anakuwuzirani. Musaope kapenanso kugwa mphwayi.”
22 Laselisondela kimi lonke lathi: Asithume amadoda phambi kwethu ukuze asihlolele ilizwe, abuyise ilizwi kithi, indlela esizakwenyuka ngayo, lemizi esizangena kuyo.
Tsono nonse munabwera kwa ine ndi kuti, “Tiyeni titumize anthu ayambe apita kuti akazonde dzikolo ndi kutibweretsera mawu pa za njira yomwe tidzere ndi za mizinda imene tikafikireko.”
23 Lendaba yayinhle emehlweni ami; ngakho ngathatha kini amadoda alitshumi lambili, indodanye ngesizwe.
Ndinaona kuti maganizo amenewa anali abwino, choncho ndinasankha anthu khumi ndi awiri, mmodzi ku fuko lililonse.
24 Wona aphenduka, enyukela entabeni aze afika esihotsheni seEshikoli, asihlola.
Iwo ananyamuka napita mʼdziko la mapiri, ndipo anafika ku Chigwa cha Esikolo ndi kukazonda dzikolo.
25 Asethatha okwezithelo zelizwe esandleni sabo, azehlisela kithi; abuyisa ilizwi kithi athi: Ilizwe lihle iNkosi uNkulunkulu wethu esinika lona.
Pobwerera anatitengerako zipatso za mʼdzikomo ndipo anatipatsa mawu akuti, “Dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa ndi labwino.”
26 Kanti kalifunanga ukwenyuka, kodwa lavukela umlomo weNkosi uNkulunkulu wenu,
Koma inu simunafune kupitako ndipo munawukira lamulo la Yehova Mulungu wanu.
27 langunguna emathenteni enu lathi: Ngoba iNkosi yayisizonda, yasikhupha elizweni leGibhithe ukusinikela esandleni samaAmori ukusibhubhisa.
Inu munanyinyirika mʼmatenti anu nʼkumati, “Mulungu amatida nʼchifukwa chake anatitulutsa ku Igupto kuti atipereke mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge.
28 Sizakwenyukela ngaphi? Abafowethu benze inhliziyo yethu iphele amandla besithi: Abantu bakhulu bade kulathi; imizi mikhulu, ibiyelwe ngemithangala efika emazulwini; futhi-ke sibonile khona amadodana amaAnaki.
Tigwire mtengo wanji? Abale athu anatitayitsa mtima. Iwo akuti, ‘Anthuwo ndi amphamvu ndi aatali kuposa ife, mizindayo ndi yayikulu ndipo mipanda yake ndi yayitali yofika kumwamba. Ife tinaonanso Aanaki kumeneko.’”
29 Ngasengisithi kini: Lingatshaywa luvalo, libesabe.
Ndipo ine ndinati kwa inu, “Musachite mantha kapena kuwaopa.
30 INkosi uNkulunkulu wenu ehamba phambi kwenu, yona izalilwela njengakho konke eyalenzela khona eGibhithe phambi kwamehlo enu,
Yehova Mulungu wanu, amene akukutsogolerani, adzakumenyerani nkhondo monga muja anachitira ku Igupto inu mukuona,
31 lenkangala, lapho obone khona ukuthi iNkosi uNkulunkulu wakho yakuthwala njengendoda ithwala indodana yayo, endleleni yonke elahamba ngayo laze lafika kulindawo.
ndi mʼchipululu muja. Kumeneko munaona mmene Yehova Mulungu wanu anakunyamulirani monga abambo anyamulira mwana wawo, njira yonse yomwe munayenda mpaka munafika pamalo ano.”
32 Kodwa ngalelilizwi kalikholwanga iNkosi uNkulunkulu wenu
Ngakhale zinali choncho, simunadalire Yehova Mulungu wanu
33 eyahamba phambi kwenu endleleni, ukulidingela indawo ukuze limise inkamba, ngomlilo ebusuku, ukulitshengisa indlela elizahamba ngayo, langeyezi emini.
amene anakutsogolerani pa ulendo wanu, ndi moto nthawi ya usiku ndi mtambo nthawi ya masana, kukufunirani malo woti mumange msasa ndi kukuonetsani njira yoti muyendemo.
34 Kwathi iNkosi isizwile ilizwi lamazwi enu, yathukuthela yafunga yathi:
Yehova atamva zimene munanena anakwiya nalumbira kuti,
35 Isibili kakho kulamadoda alesisizukulwana esibi ozabona ilizwe elihle engafunga ukulinika oyihlo,
“Palibe ndi mmodzi yemwe mwa mʼbado woyipawu amene adzaona dziko labwino limene ndinalumbira kupatsa makolo anu,
36 ngaphandle kukaKalebi indodana kaJefune; yena uzalibona. Njalo ngizanika kuye ilizwe anyathela kulo, lakubantwana bakhe, ngoba ulandele iNkosi ngokupheleleyo.
kupatula Kalebe mwana wa Yefune. Iye adzaliona, ndipo ndidzamupatsa iye ndi adzukulu ake, dziko limene adzapondamo popeza anatsata Yehova ndi mtima wake wonse.”
37 Lami iNkosi yangithukuthelela ngenxa yenu, isithi: Lawe kawuyikungena khona.
Chifukwa cha inu, Yehova anakwiyiranso ine ndipo anati, “Iwenso sudzalowa mʼdzikomo.
38 UJoshuwa indodana kaNuni oma phambi kwakho, yena uzangena khona; mqinise, ngoba yena uzakwenza uIsrayeli adle ilifa lalo.
Koma Yoswa mwana wa Nuni amene amakuthandiza, adzalowa mʼdzikomo. Umulimbikitse chifukwa adzatsogolera Israeli kukalandira dzikolo.
39 Labantwanyana benu elalisithi bazakuba yimpango, labantwana benu, abangaziyo lamuhla okuhle lokubi, bona bazangena khona; lakubo ngizalinika, bona-ke bazakudla ilifa lalo.
Ndipo angʼonoangʼono amene munati adzagwidwa ukapolo, ana anu amene sanadziwe kusiyanitsa chabwino ndi choyipa, amenewo adzalowa mʼdzikolo. Ndidzalipereka kwa iwo ndipo lidzakhala lawo.
40 Kodwa lina ziphendukeleni, lisuke liye enkangala, indlela yoLwandle oluBomvu.
Koma inu, tembenukani nyamukani kulowera cha ku chipululu kutsatira njira ya ku Nyanja Yofiira.”
41 Laseliphendula lisithi kimi: Sonile eNkosini; thina sizakwenyuka siyekulwa, njengakho konke iNkosi uNkulunkulu wethu eyasilaya khona. Selihlomile, ngulowo lalowo isikhali sakhe sempi, lacabanga ukuthi kulula ukwenyukela entabeni.
Ndipo inuyo munati, “Tachimwa pamaso pa Yehova. Tipita ndi kukachita nkhondo monga Yehova Mulungu wathu watilamulira.” Choncho aliyense wa inu anavala zankhondo, ndi kuganiza kuti nʼkosavuta kupita mʼdziko la mapiri lija.
42 INkosi yasisithi kimi: Tshono kubo: Lingenyuki, lingalwi, ngoba kangikho phakathi kwenu, hlezi litshaywe phambi kwezitha zenu.
Koma Yehova anandiwuza kuti, “Awuze anthuwa kuti, ‘Musapite kukachita nkhondo chifukwa Ine sindidzakhala nanu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu.’”
43 Ngasengikhuluma kini, kodwa kalilalelanga, lavukela umlomo weNkosi, laqholoza lenyukela entabeni.
Choncho ndinakuwuzani koma simunamve. Inu munawukira lamulo la Yehova ndipo mwamwano munayenda kulowa mʼdziko la mapiri.
44 Kwathi amaAmori ayehlala entabeni leyo aphuma ukumelana lani, alixotsha njengokwenziwa zinyosi, alihlakaza eSeyiri, kwaze kwaba seHorma.
Aamori amene ankakhala mʼmapiriwo anatuluka kukakumana nanu ndipo anakuthamangitsani ngati gulu la njuchi ndipo anakukanthani kuchokera ku Seiri, njira yonse mpaka ku Horima.
45 Laselibuya, lakhala inyembezi phambi kweNkosi, kodwa iNkosi kayilizwanga ilizwi lenu, kayibekanga indlebe kini.
Munabwererako mukulira pamaso pa Yehova, koma Iye sanalabadire kulira kwanuko ndipo sanakumvetsereni.
46 Laselihlala eKadeshi insuku ezinengi, njengensuku elahlala ngazo.
Pamenepo munakhala ku Kadesi masiku ambiri kwa nthawi yayitali ndithu.

< UDutheronomi 1 >