< 1 Imilando 24 >

1 Njalo izigaba zamadodana kaAroni. Amadodana kaAroni: ONadabi, loAbihu, uEleyazare, loIthamari.
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 Kodwa oNadabi loAbihu bafa mandulo kuloyise, njalo bengelabantwana; ngakho oEleyazare loIthamari basebenza njengabapristi.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 UDavida wasebehlukanisa, loZadoki emadodaneni kaEleyazare, loAhimeleki emadodaneni kaIthamari, ngokwesikhundla sabo enkonzweni yabo.
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 Kwatholakala emadodaneni kaEleyazare inhloko zamaqhawe amanengi okwedlula emadodaneni kaIthamari mhla bewehlukanisa; emadodaneni kaEleyazare kwakulenhloko ezilitshumi lesithupha zendlu yaboyise, lemadodaneni kaIthamari ngokwendlu yaboyise, eziyisificaminwembili.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 Basebezehlukanisa ngezinkatho, lezi laleziyana, ngoba izinduna zendlu engcwele lezinduna zikaNkulunkulu zazivela emadodaneni kaEleyazare lemadodaneni kaIthamari.
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 UShemaya indodana kaNethaneli umbhali, ovela kumaLevi, wasezibhala phambi kwenkosi leziphathamandla loZadoki umpristi loAhimeleki indodana kaAbhiyatha, lenhloko zaboyise zabapristi lezamaLevi; indlu kayise eyodwa yathathelwa uEleyazare, leyodwa yathathelwa uIthamari.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 Inkatho yokuqala yasiphumela uJehoyaribi, eyesibili uJedaya,
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 eyesithathu uHarimi, eyesine uSeworimi,
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 eyesihlanu uMalikiya, eyesithupha uMijamini,
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 eyesikhombisa uHakhozi, eyesificaminwembili uAbhiya,
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 eyesificamunwemunye uJeshuwa, eyetshumi uShekaniya,
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 eyetshumi lanye uEliyashibi, eyetshumi lambili uJakimi,
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 eyetshumi lantathu uHupha, eyetshumi lane uJeshebeyabi,
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 eyetshumi lanhlanu uBiliga, eyetshumi lesithupha uImeri,
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 eyetshumi lesikhombisa uHeziri, eyetshumi lesificaminwembili uHaphizezi,
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 eyetshumi lesificamunwemunye uPhethahiya, eyamatshumi amabili uJehezekeli,
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 eyamatshumi amabili lanye uJakini, eyamatshumi amabili lambili uGamuli,
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 eyamatshumi amabili lantathu uDelaya, eyamatshumi amabili lane uMahaziya.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 Isikhundla salaba enkonzweni yabo sasiyikungena endlini yeNkosi ngokwesimiso sabo ngesandla sikaAroni uyise, njengalokho iNkosi uNkulunkulu kaIsrayeli yayimlayile.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 Labaseleyo emadodaneni kaLevi: Emadodaneni kaAmramu: NguShubayeli; emadodaneni kaShubayeli: NguJehideya.
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 NgoRehabhiya: Emadodaneni kaRehabhiya, inhloko kwakunguIshiya;
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 kwabakoIzihari, uShelomothi; emadodaneni kaShelomothi, uJahathi.
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 Lamadodana kaHebroni, uJeriya owokuqala, uAmariya owesibili, uJahaziyeli owesithathu, uJekameyamu owesine.
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 Amadodana kaUziyeli, uMika; emadodaneni kaMika, uShamiri.
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 Umfowabo kaMika nguIshiya; emadodaneni kaIshiya, uZekhariya.
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 Amadodana kaMerari: OMahli loMushi; amadodana kaJahaziya: UBheno.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 Amadodana kaMerari: KuJahaziya: OBheno loShohama loZakuri loIbiri.
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 KuMahli: UEleyazare, owayengelamadodana.
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 NgoKishi: Amadodana kaKishi: UJerameli.
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 Lamadodana kaMushi: OMahli loEderi loJerimothi. La ngamadodana amaLevi ngokwendlu yaboyise.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 Lalaba labo benza inkatho yokuphosa njengabafowabo, amadodana kaAroni, phambi kukaDavida inkosi loZadoki loAhimeleki lenhloko zaboyise babapristi labamaLevi, inhloko yaboyise njengomfowabo omnciyane.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 1 Imilando 24 >