< Otra Mozus 8 >

1 Tad Tas Kungs sacīja uz Mozu: ej pie Faraona un saki tam: tā saka Tas Kungs: atlaid Manus ļaudis, ka tie Man kalpo;
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze.
2 Un ja tu liegsies, tos atlaist, redzi, tad Es visas tavas robežas sitīšu ar vardēm,
Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule.
3 Ka upe kustin kustēs ar vardēm, un tās celsies un nāks tavā namā un tavā guļamā kambarī un uz tavu gultu un tavu kalpu namos un pār taviem ļaudīm un tavos cepļos un tavās abrās.
Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo.
4 Un vardes nāks uz tevi un uz taviem ļaudīm un uz taviem kalpiem.
Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”
5 Tad Tas Kungs sacīja uz Mozu: saki Āronam: izstiep savu roku ar savu zizli pār strautiem, pār upēm un pār ezeriem, un liec vardēm nākt pār Ēģiptes zemi.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’”
6 Un Ārons izstiepa savu roku pār Ēģiptes ūdeņiem, tad nāca vardes un apklāja Ēģiptes zemi
Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto.
7 Un tie burvji darīja arīdzan tā ar savu buršanu un lika vardēm nākt pār Ēģiptes zemi.
Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.
8 Tad Faraons aicināja Mozu un Āronu un sacīja: lūdziet To Kungu, ka Viņš tās vardes atņemtu no manis un no maniem ļaudīm; tad es tos ļaudis atlaidīšu, upurēt Tam Kungam.
Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”
9 Bet Mozus sacīja uz Faraonu: saki man jel, kad man būs lūgt tevis dēļ un tavu kalpu un tavu ļaužu labad, lai tās vardes tiek izdeldētas, ka vairs nav pie tevis nedz tavā namā, bet paliek upē vien?
Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”
10 Un viņš sacīja: rītu. Un tas sacīja: lai ir pēc tava vārda; lai tu atzīsti, ka neviens nav kā Tas Kungs, mūsu Dievs.
Farao anati, “Mawa.” Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu.
11 Tām vardēm būs atstāties no tevis un no tava nama un no taviem kalpiem un no taviem ļaudīm; upē vien tām būs palikt.
Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”
12 Tad Mozus un Ārons aizgāja no Faraona, un Mozus sauca uz To Kungu to varžu dēļ, kā viņš Faraonam bija apsolījis.
Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao.
13 Un Tas Kungs darīja pēc Mozus vārda, un tās vardes nomira namos, sētās un uz laukiem.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa
14 Un tie tās meta kopās, un zeme smirdēja.
Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha.
15 Kad nu Faraons redzēja, ka bija dabūjis atvieglināšanu, tad viņš apcietināja savu sirdi un tiem neklausīja, kā Tas Kungs bija sacījis.
Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.
16 Tad Tas Kungs sacīja uz Mozu: saki Āronam: izstiep savu zizli un sit zemes pīšļus, lai top par utīm pa visu Ēģiptes zemi, un tie tā darīja.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.”
17 Jo Ārons izstiepa savu roku ar savu zizli un sita zemes pīšļus, un utis radās pie cilvēkiem un pie lopiem; - visi zemes pīšļi palika par utīm pa visu Ēģiptes zemi.
Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe.
18 Tad tie burvji darbojās arī tā ar savu buršanu, likt utīm nākt; bet tie nevarēja. Tā bija utis pie cilvēkiem un pie lopiem.
Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.
19 Tad tie burvji sacīja uz Faraonu: šis ir Dieva pirksts. Tomēr Faraona sirds apcietinājās, un viņš tiem neklausīja, tā kā Tas Kungs bija sacījis.
Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.
20 Tad Tas Kungs sacīja uz Mozu: celies rīt agri un stājies Faraona priekšā: redzi, viņš izies pie ūdens, - un runā uz to: tā saka Tas Kungs: atlaid Manus ļaudis, lai tie Man kalpo.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze.
21 Bet ja tu Manus ļaudis neatlaidīsi, tad Es sūtīšu visādus kukaiņus pār tevi un pār taviem kalpiem un pār taviem ļaudīm un tavos namos, un visādiem kukaiņiem būs piepildīt ēģiptiešu namus un to zemi, kur tie ir.
Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’”
22 Un tanī dienā Es izšķiršu Gošenes zemi, kur Mani ļaudis dzīvo, ka tur nebūs kukaiņiem būt, lai tu atzīsti, ka Es Tas Kungs esmu pa visu zemi.
“Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino.
23 Un Es darīšu starpību starp Maniem ļaudīm un taviem ļaudīm; rīt šai zīmei būs notikt.
Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”
24 Un Tas Kungs darīja tā, un kukaiņi nāca bariem Faraona namā un viņa kalpu namos un pa visu Ēģiptes zemi, un zeme tapa maitāta no kukaiņiem.
Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.
25 Tad Faraons aicināja Mozu un Āronu un sacīja: ejat un upurējat savam Dievam šinī zemē.
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”
26 Bet Mozus sacīja: tā nevar darīt; jo, kas ēģiptiešiem negantība, to mēs upurētu Tam Kungam, savam Dievam. Redzi, ja tad mēs, kas ēģiptiešiem negantība, upurētu viņu priekšā, vai tie mūs ar akmeņiem nenomētātu?
Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife.
27 Mēs iesim kādu treju dienu gājumu tuksnesī un upurēsim Tam Kungam, savam Dievam, kā Viņš mums ir sacījis.
Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”
28 Tad Faraons sacīja: es jūs atlaidīšu, upurēt Tam Kungam, savam Dievam; tikai neaizejiet visai tālu, - lūdziet par mani.
Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”
29 Tad Mozus sacīja: redzi, es aizeju no tevis un lūgšu To Kungu, ka šiem kukaiņiem rītu būs atstāties no Faraona un no viņa kalpiem un no viņa ļaudīm; tikai Faraonam nebūs vairs mani pievilt, neatlaižot tos ļaudis, upurēt Tam Kungam.
Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”
30 Tad Mozus aizgāja no Faraona un lūdza To Kungu.
Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova.
31 Un Tas Kungs darīja pēc Mozus vārda, un tie kukaiņi atstājās no Faraona, no viņa kalpiem un no viņa tautas, ka tur neviens nepalika.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala.
32 Tomēr Faraons arī šo reiz apcietināja savu sirdi un neatlaida tos ļaudis.
Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.

< Otra Mozus 8 >