< Salamans Mācītājs 10 >

1 Nosprāgušas mušas dara smirdam un rūgstam aptiekāra zāles; tāpat no lielāka svara, nekā gudrība un gods, ir maķenīt ģeķības (tāpat arī mazliet ģeķības pārsver cienījama vīra gudrību un godu).
Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira, choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.
2 Gudra vīra sirds ir pa viņa labo roku, bet ģeķa sirds ir pa viņa kreiso roku.
Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino, koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.
3 Un arī kad ģeķis pa ceļu staigā, tad viņam prāta trūkst, un viņš saka uz ikkatru, ka esot ģeķis.
Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu, zochita zake ndi zopanda nzeru ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.
4 Ja valdnieka dusmība pret tevi ceļas, tad neatstājies no savas vietas, jo lēnprātība klusina lielus grēkus.
Ngati wolamulira akukwiyira, usachoke pa ntchito yako; kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.
5 Vēl ir ļaunums, ko pasaulē esmu redzējis, proti misēklis, kas ceļas no valdnieka.
Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano, kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:
6 Dažs ģeķis top celts lielā godā, un bagātie sēž zemajā vietā.
Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba, pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.
7 Es esmu redzējis kalpus uz zirgiem, un lielus kungus kājām tāpat kā kalpus.
Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.
8 Kas bedri rok, tas kritīs iekšā; un kas sētu ārda, tam čūska iedzels.
Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha; amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.
9 Kas akmeņus veļ, tas no tiem dabūs sāpes; kas malku skalda, tas ievainosies.
Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo; amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.
10 Kad dzelzs ir nodilusi un viņas asmens netop tecināts(asināts), tad vairāk spēka jāpieliek; bet gudrība veicina darbu.
Ngati nkhwangwa ili yobuntha yosanoledwa, pamafunika mphamvu zambiri potema, koma luso limabweretsa chipambano.
11 Kad čūska iedzēlusi, pirms apvārdota, tad vārdotājam peļņas nav.
Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka ngati njokayo yakuluma kale.
12 Vārdi no gudra vīra mutes ir jauki; bet ģeķa lūpas pašu aprij.
Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa, koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.
13 Viņa mutes vārdu iesākums ir ģeķība, un viņa valodas gals ir neprātība un posts.
Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa; potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala
14 Ģeķis gan daudz runā, bet cilvēks nezin, kas notiks, un kas būs pēc viņa; kas viņam to teiks?
ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu. Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?
15 Ģeķa pūliņš to nogurdina, jo tas nezina ceļu uz pilsētu.
Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa; ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.
16 Ak vai, tev, zeme, kam ķēniņš ir bērns, un kam lielkungi rīta laikā plītē.
Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana, ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.
17 Labi tev, zeme, kam ķēniņš ir cienījams, un kam lielkungi īstā laikā ēd, stiprināties un ne plītēt.
Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake, kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.
18 Caur kūtrību sijas gāžas, un aiz slinkām rokām namam pil cauri.
Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka; ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.
19 Dzīres top taisītas par prieku, un vīns ielīksmo tos, kas dzīvo, un nauda visu to gādā.
Phwando ndi lokondweretsa anthu, ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo, koma ndalama ndi yankho la chilichonse.
20 Nelādi ķēniņu savā sirdī, un nelādi bagātu savā guļamā kambarī, jo putni apakš debess aiznes to skaņu un ar spārniem skriedami izpauž to valodu.
Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako, kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako, pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako nʼkukafotokoza zomwe wanena.

< Salamans Mācītājs 10 >