< Amosa 5 >

1 Klausiet šo vārdu, ar ko es par jums sāku raudu dziesmu, Israēla nams!
Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
2 Israēla meita ir kritusi, viņa vairs necelsies, viņa ir atstāta zemē, neviena nav, kas to uzceļ.
“Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
3 Jo tā saka Tas Kungs Dievs: tai pilsētai, kur iziet tūkstoši, atliksies simts, un kur iziet simts, atliksies desmit Israēla namā.
Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
4 Jo tā saka Tas Kungs uz Israēla namu: meklējiet Mani un dzīvojiet!
Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
5 Bet nemeklējiet Bēteli un nenāciet uz Gilgalu un nenoejat uz Bēršebu, jo Gilgala taps aizvesta un Bētele paliks par neko.
musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
6 Meklējiet To Kungu un dzīvojiet, - lai Viņš neizšaujas Jāzepa namā kā uguns, kas to norij, un neviens to nevar dzēst Bētelē, -
Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
7 Jūs, kas tiesu pārvēršat par vērmelēm un stumjat taisnību pie zemes:
Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
8 Kas radījis Sietiņu un Orijonu un nāves ēnu pārvērš par rīta gaismu un dienu aptumšo, ka nakts metās, kas jūras ūdeni sauc un to izgāž pa zemes virsu, - Kungs ir Viņa vārds,
(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
9 Tam prāts ir, to spēcīgo postīt, ka posts nāk pār stipro pili.
Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
10 Tie ienīst to, kas vārtos pārmāca, un kas patiesību runā, to tie tur par negantu.
inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
11 Tādēļ ka jūs apbēdinājāt nabagu un ņemat labības dāvanu no viņa, tad jūs gan esiet uztaisījuši namus no cirstiem akmeņiem, bet jūs tanīs nedzīvosiet, jūs esat stādījuši diženus vīna dārzus, bet viņu vīnu jūs nedzersiet.
Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
12 Jo es zinu, ka jūsu pārkāpumu daudz un jūsu grēku varen daudz. Tie nospaida taisno un ņem dāvanas, un nomāc nabagus vārtos.
Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
13 Tādēļ prātīgais šinīs laikos cieš klusu, jo tie ir nikni laiki.
Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
14 Meklējiet labu un ne ļaunu, lai jūs dzīvojat, un tā Tas Kungs, tas Dievs Cebaot, būs ar jums, kā jūs sakāt.
Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
15 Ienīstiet ļaunu un mīļojiet labu un spriežat vārtos tiesu, vai varbūt Tas Kungs, tas Dievs Cebaot, neapžēlosies par Jāzepa atlikušiem.
Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
16 Tādēļ tā saka Tas Kungs, tas Dievs Cebaot, Tas Kungs: visās ielās vaimanas un visās gatvēs saka: vai, vai! Arāju sauc pie asarām, un pie vaimanām vaidētājus.
Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
17 Un visos vīna dārzos būs vaimanas, jo Es iešu caur jūsu vidu, saka Tas Kungs.
Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
18 Ak vai, tiem, kas ilgojās pēc Tā Kunga dienas! Par ko tad jums būs Tā Kunga diena? Tā būs tumsa un ne gaisma.
Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
19 Tā kā kad vīrs bēgtu no lauvas un to sastaptu lācis! Un nāktu namā un atslietos ar roku pie sienas, un čūska viņam iedzeltu!
Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
20 Vai tad Tā Kunga diena nebūs tumsa un ne gaisma, un nakts, kam nav spožuma?
Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
21 Es ienīstu un atmetu jūsu svētkus un negribu ost jūsu sapulces.
“Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
22 Jo kad jūs Man dedzināmos upurus upurējat līdz ar saviem ēdamiem upuriem, tad Man pie viņiem nav labs prāts, un pateicības upuri no jūsu barotiem lopiem Es negribu ieredzēt.
Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
23 Atstājies jel no Manis ar savu dziesmu bļaušanu, un tavu kokļu skaņu Es negribu dzirdēt.
Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
24 Bet lai plūst tiesa kā ūdens un taisnība kā stipra upe.
Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
25 Vai četrdesmit gadus tuksnesī jūs Man esat nesuši upurus un ēdamus upurus, Israēla nams?
“Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
26 Bet jūs nesāt sava(Sikuta) ķēniņa būdu un sava Ķijuna bildi, sava dieva zvaigzni, ko jūs sev pašiem bijāt taisījuši.
Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
27 Tādēļ Es jūs aizvedīšu tālu viņpus Damaskus, saka Tas Kungs, kam vārds ir Dievs Cebaot.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.

< Amosa 5 >