< Psalmorum 22 >

1 in finem pro adsumptione matutina psalmus David Deus Deus meus respice me quare me dereliquisti longe a salute mea verba delictorum meorum
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
2 Deus meus clamabo per diem et non exaudies et nocte et non ad insipientiam mihi
Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
3 tu autem in sancto habitas Laus Israhel
Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
4 in te speraverunt patres nostri speraverunt et liberasti eos
Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
5 ad te clamaverunt et salvi facti sunt in te speraverunt et non sunt confusi
Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
6 ego autem sum vermis et non homo obprobrium hominum et abiectio plebis
Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
7 omnes videntes me deriserunt me locuti sunt labiis moverunt caput
Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
8 speravit in Domino eripiat eum salvum faciat eum quoniam vult eum
“Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
9 quoniam tu es qui extraxisti me de ventre spes mea ab uberibus matris meae
Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
10 in te proiectus sum ex utero de ventre matris meae Deus meus es tu
Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
11 ne discesseris a me quoniam tribulatio proxima est quoniam non est qui adiuvet
Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
12 circumdederunt me vituli multi tauri pingues obsederunt me
Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
13 aperuerunt super me os suum sicut leo rapiens et rugiens
Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
14 sicut aqua effusus sum et dispersa sunt universa ossa mea factum est cor meum tamquam cera liquescens in medio ventris mei
Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
15 aruit tamquam testa virtus mea et lingua mea adhesit faucibus meis et in limum mortis deduxisti me
Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
16 quoniam circumdederunt me canes multi concilium malignantium obsedit me foderunt manus meas et pedes meos
Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
17 dinumeraverunt omnia ossa mea ipsi vero consideraverunt et inspexerunt me
Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
18 diviserunt sibi vestimenta mea et super vestem meam miserunt sortem
Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
19 tu autem Domine ne elongaveris auxilium tuum ad defensionem meam conspice
Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
20 erue a framea animam meam et de manu canis unicam meam
Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
21 salva me ex ore leonis et a cornibus unicornium humilitatem meam
Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
22 narrabo nomen tuum fratribus meis in media ecclesia laudabo te
Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
23 qui timetis Dominum laudate eum universum semen Iacob magnificate eum
Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
24 timeat eum omne semen Israhel quoniam non sprevit neque dispexit deprecationem pauperis nec avertit faciem suam a me et cum clamarem ad eum exaudivit me
Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
25 apud te laus mea in ecclesia magna vota mea reddam in conspectu timentium eum
Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
26 edent pauperes et saturabuntur et laudabunt Dominum qui requirunt eum vivent corda eorum in saeculum saeculi
Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
27 reminiscentur et convertentur ad Dominum universi fines terrae et adorabunt in conspectu eius universae familiae gentium
Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
28 quoniam Dei est regnum et ipse dominabitur gentium
pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
29 manducaverunt et adoraverunt omnes pingues terrae in conspectu eius cadent omnes qui descendunt in terram
Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
30 et anima mea illi vivet et semen meum serviet ipsi
Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
31 adnuntiabitur Domino generatio ventura et adnuntiabunt iustitiam eius populo qui nascetur quem fecit Dominus
Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.

< Psalmorum 22 >