< Psalmorum 91 >

1 Laus cantici David. [Qui habitat in adjutorio Altissimi, in protectione Dei cæli commorabitur.
Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
2 Dicet Domino: Susceptor meus es tu, et refugium meum; Deus meus, sperabo in eum.
Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa, Mulungu wanga amene ndimadalira.”
3 Quoniam ipse liberavit me de laqueo venantium, et a verbo aspero.
Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje ndi ku mliri woopsa;
4 Scapulis suis obumbrabit tibi, et sub pennis ejus sperabis.
Adzakuphimba ndi nthenga zake, ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo; kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
5 Scuto circumdabit te veritas ejus: non timebis a timore nocturno;
Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku, kapena muvi wowuluka masana,
6 a sagitta volante in die, a negotio perambulante in tenebris, ab incursu, et dæmonio meridiano.
kapena mliri umene umayenda mu mdima, kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
7 Cadent a latere tuo mille, et decem millia a dextris tuis; ad te autem non appropinquabit.
Anthu 1,000 atha kufa pambali pako, anthu 10,000 kudzanja lako lamanja, koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
8 Verumtamen oculis tuis considerabis, et retributionem peccatorum videbis.
Udzapenya ndi maso ako ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.
9 Quoniam tu es, Domine, spes mea; Altissimum posuisti refugium tuum.
Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo; wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
10 Non accedet ad te malum, et flagellum non appropinquabit tabernaculo tuo.
Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
11 Quoniam angelis suis mandavit de te, ut custodiant te in omnibus viis tuis.
Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
12 In manibus portabunt te, ne forte offendas ad lapidem pedem tuum.
ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
13 Super aspidem et basiliscum ambulabis, et conculcabis leonem et draconem.
Udzapondaponda mkango ndi njoka, udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.
14 Quoniam in me speravit, liberabo eum; protegam eum, quoniam cognovit nomen meum.
“Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa; ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
15 Clamabit ad me, et ego exaudiam eum; cum ipso sum in tribulatione: eripiam eum, et glorificabo eum.
Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha; ndidzakhala naye pa mavuto, ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
16 Longitudine dierum replebo eum, et ostendam illi salutare meum.]
Ndidzamupatsa moyo wautali ndi kumupulumutsa.”

< Psalmorum 91 >