< 시편 135 >

1 할렐루야 여호와의 이름을 찬송하라! 여호와의 종들아 찬송하라!
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 여호와의 집 우리 하나님의 전정에 섰는 너희여,
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 여호와를 찬송하라! 여호와는 선하시며 그 이름이 아름다우니 그 이름을 찬양하라!
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 여호와께서 자기를 위하여 야곱 곧 이스라엘을 자기의 특별한 소유로 택하셨음이로다
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 내가 알거니와 여호와께서는 광대하시며 우리 모든 신보다 높으시도다
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 여호와께서 무릇 기뻐하시는 일을 천지와 바다와 모든 깊은 데서 행하셨도다
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 안개를 땅 끝에서 일으키시며 비를 위하여 번개를 만드시며 바람을 그 곳간에서 내시는도다
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 저가 애굽의 처음 난 자를 사람부터 짐승까지 치셨도다
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 애굽이여, 여호와께서 너의 중에 징조와 기사를 보내사 바로와 그 모든 신복에게 임하게 하셨도다
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 저가 많은 나라를 치시고 강한 왕들을 죽이셨나니
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 곧 아모리인의 왕 시혼과 바산 왕 옥과 가나안의 모든 국왕이로다
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 저희의 땅을 기업으로 주시되 자기 백성 이스라엘에게 기업으로 주셨도다
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 여호와여, 주의 이름이 영원하시니이다 여호와여, 주의 기념이 대대에 이르리이다
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 여호와께서 자기 백성을 판단하시며 그 종들을 긍휼히 여기시리로다
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 열방의 우상은 은, 금이요 사람의 수공물이라
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 입이 있어도 말하지 못하며 눈이 있어도 보지 못하며
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 귀가 있어도 듣지 못하며 그 입에는 아무 기식도 없나니
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 그것을 만든자와 그것을 의지하는 자가 다 그것과 같으리라
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 이스라엘 족속아 여호와를 송축하라! 아론의 족속아 여호와를 송축하라!
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 레위 족속아 여호와를 송축하라! 여호와를 경외하는 너희들아 여호와를 송축하라!
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 예루살렘에 거하신 여호와는 시온에서 찬송을 받으실지어다! 할렐루야
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< 시편 135 >