< 1 Yohana 1 >
1 Chilya chinu chaliga chiliwo okusoka bhusimuka-chilya chinu chonguywe, chilya chinu chalolele kwa meso geswe, chilya chinu chabhwene, na chinu amabhoko geswe gachigwatile-okulubhana no musango gwo bhuanga.
Tikukulalikirani za Mawu a moyo amene analipo kuyambira pachiyambi, amene tinawamva, amene tinawaona ndi maso athu, amene tinawapenyetsetsa, ndipo tinawakhudza ndi manja athu.
2 No bhuanga bhulya bhwakolelwe kwo kumenyekana abhwelu, na nichibhulola, no kubhubhambalila, no kubhalasisha obhuanga bhwa kajanende, bhunu bhwaliga ku Lata na nibhukolwa kumenyekana kweswe. (aiōnios )
Moyowo unaoneka, tinawuona ndipo tikuchitira umboni. Tikukulalikirani za moyo wosatha umene unali ndi Atate ndipo unaonekera kwa ife. (aiōnios )
3 Chilya chinu chalolele no kuchungwa echichikumusha kwemwe one, koleleki ati mutule okubhanyasha amwi neswe, no bhulangi bhweswe amwi na Lata no mwana waye Yesu Kristo.
Tikukulalikirani chimene tinachiona ndi kumva, kuti inuyo muyanjane nafe. Kuyanjana kwathu, tikuyanjana ndi Atate ndiponso ndi Mwana wawo, Yesu Khristu.
4 Na echibhandikila emisango jinu emwe koleleki ati obhulosi bhweswe bhukumile.
Tikukulemberani zimenezi kuti chimwemwe chathu chikhale chathunthu.
5 Gunu Nigwo omusango gunu chonguywe okusoka kwaye no kubhalasisha: Nyamuanga ni bhwelu na munda yaye chitalimo chisute na katyali.
Uthenga umene tinamva kwa Iye ndipo tikuwulalikira kwa inu ndi uwu: Mulungu ndiye kuwunika ndipo mwa Iye mulibe mdima konse.
6 Alabha chikaika ati chili no bhusangi nage kenu nichilibhatila mu chisute, chaliga na chitakukola je chimali.
Tikanena kuti timayanjana naye, koma nʼkumayendabe mu mdima, tikunama ndipo sitikuchita choonadi.
7 Mbe nawe chikalibhatila mu bhwelu lwa kutyo ali mu bhwelu, echisangila eswe abhene kwa bhene, na insagama ya Yesu Kristo, eyo mwana waye eichesha okusoka mu bhibhibhi bhyona.
Koma tikamayenda mʼkuwunika, monga Iye ali mʼkuwunika, pamenepo timayanjana wina ndi mnzake, ndipo magazi a Yesu, Mwana wake, amatitsuka ndi kutichotsera tchimo lililonse.
8 Alabha chikaika ati chitana bhibhibhi, echijiga-jiga weswe abhene, ne chimali chitachilimo eswe.
Tikanena kuti tilibe tchimo, tikudzinyenga tokha ndipo mwa ife mulibe choonadi.
9 Mbe nawe chikata ebhibhibhi bhyeswe, mwenene ni mwiikanyibhwa na mulengelesi okuchiswalilila ebhibhibhi bhyeswe no kuchesha na mabhibhi gona.
Koma tikavomereza machimo athu, Iye ndi wokhulupirika ndi wolungama ndipo adzatikhululukira machimo athu, nadzatiyeretsa ndi kutichotsera chosalungama chilichonse.
10 Chikaika ati chichali kukola bhibhibhi, echimukola mwenene kubha mulimi, no musango gwaye gutachilimo kweswe.
Ife tikanena kuti sitinachimwe, tikumutenga Mulungu kukhala wonama, ndipo Mawu ake sali mwa ife.