< Dagiti Salmo 62 >

1 Anusak nga urayen ti Dios, aggapu kenkuana ti pannakaisalakanko.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
2 Isuna laeng ti batok ken pannakaisalakanko; isuna ti nangato a torrek; saanakto a magaraw a pulos.
Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
3 Kasano kabayag ti panangdarupyo iti maysa a tao, tapno maitumbayo isuna a kasla nakairig a diding wenno marmarba nga alad?
Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
4 Agdamagda kenkuana tapno laeng ibabada isuna manipud iti mararaem a saadna; pagay-ayatda iti agsao kadagiti inuulbod; bendisionanda isuna babaen kadagiti ngiwatda, ngem kadagiti pusoda, ilunlunodda isuna. (Selah)
Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
5 Anusak nga urayen ti Dios; ta isu ti paggapuan ti namnamak.
Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
6 Isuna laeng ti batok ken pannakaisalakanko; isuna ti nangato a torek; saanakto a magaraw.
Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
7 Adda iti Dios ti pannakaisalakan ken dayawko; ti Dios iti bato ti pigsak ken ti kamangko.
Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
8 Agtalekkayo kenkuana iti amin a tiempo, dakayo a tattao; ibagayo kenkuana ti amin a parikutyo; ti Dios ket pagkamangantayo. (Selah)
Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
9 Pudno nga awan pategna dagiti nababa a tao, ken nauulbod dagiti nangato a tattao; nalag-an ti timbangda kadagiti timbangan; pagtitiponen a timbangen ket nalaglag-anda.
Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
10 Saankayo nga agtalek iti panangparigat wenno panagtakaw; ken saankayo a mangnamnama iti awan serserbina a kinabaknang, ta saanda nga agbunga; saankayo nga agtalek kadagitoy.
Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
11 Saan lang a naminsan a nangngegko a sinao ti Dios daytoy: adda kenkuana ti pannakabalin.
Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
12 Kasta met a napudnoka, O Apo, iti tulagmo, ta subsubadam ti tunggal tao segun iti inaramidna.
komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.

< Dagiti Salmo 62 >