< Numero 14 >
1 Iti dayta a rabii, nagsangit iti napigsa dagiti amin a tattao.
Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri.
2 Inuyaw dagiti amin a tattao ti Israel da Moises ken Aaron. Kinuna dagiti tattao kadakuada, “Nataykami la koman idiay daga iti Egipto, wenno iti daytoy a let-ang!
Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno!
3 Apay nga impannakami ni Yahweh iti daytoy a daga a matay babaen iti kampilan? Agbalin a biktima dagiti assawa ken dagiti annakmi. Saan kadi a nasaysayaat nga agsublikami idiay Egipto?”
Nʼchifukwa chiyani Yehova akutilowetsa mʼdziko limenelo? Kodi kuti tikaphedwe ndi lupanga? Kuti akazi ndi ana athu akatengedwe ngati katundu wolanda ku nkhondo? Kodi sikungakhale bwino kuti tibwerere ku Igupto?”
4 Kinunada iti tunggal maysa, “Mangpilitayo iti sabali a pangulo, ket agsublitayo idiay Egipto.”
Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”
5 Ket nagpakleb da Moises ken Aaron iti sangoanan dagiti amin a gimong dagiti tattao ti Israel.
Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo.
6 Ni Josue nga anak a lalaki ni Nun ken ni Caleb nga anak a lalaki ni Jefone, a dadduma kadagiti naibaon a mangsukimat iti daga, ket rinay-abda dagiti badoda.
Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune, omwe anali amodzi mwa amene anakazonda nawo dziko, anangʼamba zovala zawo
7 Nagsaoda kadagiti amin a tattao ti Israel. Kinunada, “Ti daga a napananmi ken sinukimatmi ket nasayaat unay.
ndipo anati kwa gulu lonse la Aisraeli, “Dziko limene tinakayendamo ndi kuliona ndi labwino kwambiri zedi.
8 No maay-ayo ni Yahweh kadatayo, ipannatayo ngarud iti daytoy a daga ket itedna daytoy kadatayo. Ti daga nga agay-ayus iti gatas ken diro.
Ngati Yehova akukondwera nafe, adzatitsogolera kulowa mʼdziko limenelo. Dziko loyenda mkaka ndi uchi adzalipereka kwa ife,
9 Ngem saankayo nga agsukir kenni Yahweh, ken saankayo nga agbuteng kadagiti tattao iti daga. Ibusentayo ida a kas kalaka ti pannangan iti taraon. Maikkatto kadakuada ti salaknibda, gapu ta adda kadatayo ni Yahweh. Saankayo nga agbuteng kadakuada.”
koma musawukire Yehova. Komanso musaope anthu a mʼdzikomo, pakuti tidzawagonjetsa. Chitetezo chawachokera, koma ife Yehova ali nafe. Musawaope.”
10 Ngem binutbuteng ida dagiti amin a tattao a batoenda ida agingga a matayda. Ket nagparang ti dayag ni Yahweh idiay tabernakulo kadagiti amin a tattao ti Israel.
Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano.
11 Kinuna ni Yahweh kenni Moises, “Kasano pay kabayag ti panangumsi dagitoy a tattao kaniak? Kasano pay kabayag ti saanda a panagtalek kaniak, iti laksid dagiti amin nga inaramidko kadakuada a pagilasinan iti pannakabalinko?
Yehova anawuza Mose kuti, “Anthu awa adzandinyoza mpaka liti? Sadzandikhulupirira mpaka liti, ngakhale ndachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi pakati pawo?
12 Darupek ida babaen kadagiti didigra, ikkatek dagiti tawidda, ken manipud iti pulim mangaramidak iti maysa a nasion a dakdakkel ken nabilbileg ngem isuda.”
Ndidzawakantha ndi mliri ndi kuwawononga. Koma ndidzakusandutsa iwe mtundu waukulu ndi wamphamvu kuposa iwo.”
13 Kinuna ni Moises kenni Yahweh, “No aramidem daytoy, ket mangeg dagiti Egipcio ti maipanggep iti daytoy, gapu ta insalakanmo dagitoy a tattao manipud kadakuada babaen iti pannakabalinmo.
Mose anati kwa Yehova, “Aigupto adzamva zimenezi! Mwa mphamvu yanu munawatulutsa anthu amenewa pakati pawo.
14 Ibagadanto kadagiti agnanaed iti daytoy a daga. Nangngegda a sika, O Yahweh ket adda kadagitoy a tattao, gapu ta nakitadaka iti rupan-rupa. Agtalinaed ti ulepmo iti ngatoen dagiti tattaomi. Umun-unaka ngem isuda babaen iti adigi nga ulep iti aldaw ken iti adigi nga apuy iti rabii.
Ndipo iwowo adzawuza anthu okhala mʼdziko lino zimenezi. Anthuwa amva kale kuti Inu Yehova mumakhala pakati pa anthu amenewa ndi kuti Inuyo Yehova mwawaonekera maso ndi maso. Mtambo wanu umakhala pamwamba pawo ndiponso mumayenda nawo mu mtambo woyima, masana ndi moto woyima, usiku.
15 Ita no patayem dagitoy a tattao a kas maysa a tao, ket agsao ken ibaga dagiti nasion a nakangngeg iti kinalatakmo a,
Tsono mukawapha anthu onsewa nthawi imodzi, mayiko amene anamva za Inu adzati,
16 'Gapu ta saan a maipan ni Yahweh dagitoy a tattao iti daga nga inkarina nga itedna kadakuada, pinatayna ida idiay let-ang.'
‘Yehova walephera kuwalowetsa anthuwo mʼdziko lomwe anawalonjeza molumbira, ndipo wawapha mʼchipululu.’
17 Ita, agpakpakaasiak kenka, usarem ti naindaklan a pannakabalinmo. Ta kinunam,
“Chonde Ambuye wonetsani mphamvu yanu monga munalonjezera kuti,
18 “Saan a nalaka nga agunget ni Yahweh ken aglaplapusanan ti kinapudnona iti tulagna. Pakpakawanenna ti pagkurkurangan ken pagbasbasolan. Ikkatenna dagiti nagbasol inton iyegna kadagiti kaputotanda ti dusa ti basol dagiti kapuonanda, kadagiti maikatlo ken maika-uppat a henerasion.'
‘Yehova sakwiya msanga, ndipo ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika, wokhululukira tchimo ndi kuwukira. Koma Iye sadzaleka kulanga ochimwa. Iyeyo amalanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo kufikira mʼbado wachitatu ndi wachinayi.’
19 Agpakaasiak kenka a pakawanem ti basol dagitoy a tattao gapu iti naindaklan a kinapudnom iti tulagmo, kas iti kanayon a panangpakawanmo kadagitoy a tattao manipud idi addada pay laeng idiay Egipto agingga ita.”
Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, akhululukireni anthuwa tchimo lawo monga mwakhala mukuwakhululukira kuchokera pa nthawi imene anachoka ku Igupto mpaka tsopano.”
20 Kinuna ni Yahweh, “Pinakawanko ida kas iti dinawatmo,
Yehova anayankha kuti, “Ndawakhululukira monga wapemphera.
21 ngem iti kinapudnona, iti panagbibiagko, ken kas mapunno iti dayagko ti entero a daga,
Komabe, ndikunenetsa kuti pali Ine, ndiponso pamene dziko lapansi ladzaza ndi ulemerero wa Yehova,
22 amin dagiti tattao a nakakita ti dayagko ken dagiti pagilasinan iti pannakabalin nga inaramidko idiay Egipto ken idiay let-ang—sinuotdak latta dagitoy iti naminsangapulo ken saanda a dimngeg iti timekko.
palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anaona ulemerero wanga ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinazichita ku Igupto ndi mʼchipululu muno, koma osandimvera ndi kundiyesa kokwanira kakhumi,
23 Isu nga ibagak a sigurado a saandanto a makita ti daga nga inkarik kadagiti kapuonanda. Awan ti uray maysa kadakuada a nangumsi kaniak ti makakita iti daytoy,
palibe ndi mmodzi yemwe wa anthu amenewa amene adzaone dziko limene ndinalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo. Aliyense amene anandinyoza sadzaliona dzikolo.
24 malaksid kenni Caleb nga adipenko, gapu ta adda sabali nga espirituna. Naan-anay a sinurotnak; ipankonto isuna iti daga a napanna sinukimat. Tagikuaento daytoy dagiti kaputotanna.
Koma mtumiki wanga Kalebe, pakuti ali ndi mtima wosiyana ndi ena ndiponso amanditsatira ndi mtima wonse, ndidzamulowetsa mʼdziko limene anapitamolo ndipo zidzukulu zake zidzalandira dzikolo ngati cholowa chawo.
25 (Ita, agnanaed dagiti Amalekita ken Canaaneo idiay tanap.) Agsublikayo inton bigat ket mapankayo idiay let-ang babaen iti dalan nga agturong iti baybay dagiti Runo.”
Ndipo popeza kuti Aamaleki ndi Akanaani akukhala ku chigwa, mawa mubwerere ndipo mupite ku chipululu podzera ku Nyanja Yofiira.”
26 Nagsao ni Yahweh kada Moises ken Aaron. Kinunana,
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
27 “Kasano pay kabayag ti panangib-ibturko kadagitoy a nadangkes a tattao a manguy-uyaw kaniak? Nangngegko dagiti panagrekreklamo dagiti tattao ti Israel kaniak.
“Kodi anthu oyipawa adzangʼungʼudza ndi kutsutsana nane mpaka liti? Ndamva madandawulo a Aisraeli ongʼungʼudzawa.
28 Ibagam kadakuada, kinuna ni Yahweh, ‘Iti panagbibiagko,' 'kas insaoyo iti panagdengngegko, Aramidek daytoy kadakayo:
Tsono awuze kuti, ‘Ndikulumbira pali Ine,’ akutero Yehova, ‘Ndidzakuchitirani zinthu zonse zimene ndamva inu mukunena:
29 Mataykayonto iti daytoy a let-ang, aminkayo a nagreklamo maibusor kaniak, dakayo a nabilang iti sensus, ti sibubukel a bilang dagiti amin a tattao manipud iti agtawen iti duapulo ken agpangato.
Mitembo yanu idzakhala ili ngundangunda mʼchipululu muno; mtembo wa munthu aliyense pakati panu amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, amene anawerengedwa pa chiwerengero chija ndipo anangʼungʼudza motsutsana nane.
30 Awan duadua a saankayo a makastrek iti daga nga inkarik a pagnaedanyo, malaksid kenni Caleb nga anak a lalaki ni Jefone ken ni Josue nga anak a lalaki ni Nun.
Palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene adzalowe mʼdziko lomwe ndinalumbira mokweza manja kuti likhale lanu, kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
31 Ngem ipankonto iti dayta a daga dagiti annakyo a kinunayo nga agbalin a biktima. Mapadasandanto ti daga a linaksidyo!
Koma ana anu amene mukunena kuti adzatengedwa ngati katundu wolanda ku nkhondo, Ine ndidzawalowetsa kuti akasangalale mʼdziko limene munalikana.
32 No maipapan kadakayo, mataykayonto iti daytoy a let-ang.
Koma inu mitembo yanu idzakhala ngundangunda mʼchipululu muno.
33 Agalla-allanto dagiti annakyo iti let-ang iti uppat a pulo a tawen. Rumbeng a lak-amenda dagiti supapak dagiti panagsukiryo agingga a patayen ti let-ang dagiti bagbagiyo.
Ana anu adzakhala abusa mʼchipululu muno zaka makumi anayi, kuvutika chifukwa cha kusakhulupirika kwanu, mpaka munthu womaliza mwa inu atafa mʼchipululu muno.
34 Kas iti bilang dagiti aldaw idi sinukimatyo ti daga iti uppat a pulo nga aldaw, kasta met ti masapul a pananglak-amyo kadagiti supapak dagiti basolyo iti uppat a pulo a tawen—maysa a tawen para iti maysa nga aldaw, ken masapul a maammoanyo ti pagbanagan ti agbalin a kabusorko.
Mudzavutika chifukwa cha machimo anu kwa zaka makumi anayi Chaka chimodzi chikuyimira tsiku limodzi la masiku makumi anayi amene munakazonda dziko lija ndipo mudzadziwa kuyipa kwake kwa kukangana ndi Ine.’
35 Siak, ni Yahweh, ti nagsao. Awan duadua nga aramidek daytoy kadagiti amin a nadangkes a tattao a nagtitipon a sangsangkamaysa a maibusor kaniak. Maibusdanto iti daytoy a let-ang. Ditoydanto a matay.'”
Ine Yehova, ndanena, ndidzachitadi zimenezi kwa anthu onse oyipawa, amene agwirizana kunditsutsa. Adzathera mʼchipululu momwe muno, adzafera muno basi.”
Ndipo anthu amene Mose anawatuma kukazonda dziko aja anachoka pamaso pake nachititsa gulu lonse la anthu kuwukira Moseyo chifukwa chofalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo.
37 Isu a natay iti sangoanan ni Yahweh dagiti amin a lallaki nga imbaon ni Moises a mangkita iti daga babaen ti didigra. Dagitoy dagiti lallaki a nagsubli ken nangipadamag iti saan a nasayaat maipanggep iti daga. Daytoy ti gapuna a nagreklamo amin a tattao maibusor kenni Moises.
Anthu amene ankafalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo anakanthidwa ndi mliri ndipo anafa pamaso pa Yehova.
38 Kadagiti lallaki a napan nangkita iti daga, ni laeng Josue nga anak a lalaki ni Nun ken ni Caleb nga anak a lalaki ni Jefone ti nagtalinaed a sibibiag.
Mwa anthu amene anakaona dzikolo, Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune ndi okhawo amene anapulumuka.
39 Idi impadamag ni Moises dagitoy a sasao kadagiti amin a tattao ti Israel, nagladingitda iti kasta unay.
Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri.
40 Nasapada a bimmangon iti bigbigat ket napanda iti tuktok ti bantay ket kinunada, “Kitaenyo, addatayo ditoy, ket mapantayo iti lugar nga inkari ni Yahweh, ta nagbasoltayo.”
Mmamawa tsiku linalo anapita mbali ya ku dziko la mapiri. Iwo anati, “Tachimwa, tipita ku dziko limene Yehova anatilonjeza.”
41 Ngem kinuna ni Moises, “Apay a salsalangusingenyon ita dagiti bilin ni Yahweh? Saankayo nga agballigi.
Koma Mose anati, “Chifukwa chiyani simukumvera lamulo la Yehova? Zimenezi sizitheka!
42 Saankayo a mapan, gapu ta awan kadakayo ni Yahweh a manglapped iti pannakaparmekyo kadagiti kabusoryo.
Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu
43 Adda sadiay dagiti Amalekita ken Cananeo, ket mataykayonto babaen kadagiti kampilan gapu ta timmalikodkayo manipud iti panangsursurotyo kenni Yahweh. Isu nga awanto isuna kadakayo.”
chifukwa kumeneko mukakumana ndi Aamaleki ndi Akanaani. Popeza mwaleka kutsata Yehova, Iyeyo sadzakhala nanu ndipo mudzaphedwa ndi lupanga.”
44 Ngem pinilitda latta iti sumang-at iti katurturodan a pagilian; nupay kasta, saan a pimmanaw ni Moises wenno ti lakasa ti tulag ni Yahweh iti kampo.
Komabe mwa maganizo awo anapita molunjika dziko la mapiri ngakhale kuti Mose sanachoke ndi Bokosi la Chipangano la Yehova pa msasa.
45 Ket simmalog dagiti Amalekita, kasta met dagiti Cananeo nga agnanaed kadagitoy a turturod. Rinautda dagiti Israelita ket pinarmekda ida agingga idiay Horma.
Koma Aamaleki ndi Akanaani amene ankakhala ku dziko lamapirilo anatsika ndi kumenyana nawo ndipo anawakantha mʼnjira yonse mpaka ku Horima.