< 4 Mózes 7 >

1 És lőn, hogy a mely napon elvégezé Mózes a sátor felállítását, és felkené azt, és megszentelé azt, minden edényével egybe, és az oltárt és annak minden edényét; és felkené és megszentelé azokat:
Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
2 Akkor előjövének az Izráel fejedelmei, az ő atyjok házának fejei; ezek a törzsek fejedelmei, és ezek a megszámláltattak felügyelői:
Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
3 És vivék az ő áldozatukat az Úr elé: hat borított szekeret, és tizenkét ökröt; egy-egy szekeret két-két fejedelemért, és mindenikért egy-egy ökröt; és odavivék azokat a sátor elébe.
Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
4 És szóla az Úr Mózesnek, mondván:
Yehova anawuza Mose kuti,
5 Vedd el ő tőlök, és legyenek azok felhasználva a gyülekezet sátorának szolgálatában; és add azokat a lévitáknak, mindeniknek az ő szolgálata szerint.
“Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
6 Elvevé azért Mózes a szekereket és ökröket, és adá azokat a lévitáknak.
Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
7 Két szekeret és négy ökröt ada a Gerson fiainak, az ő szolgálatuk szerint.
Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
8 Négy szekeret pedig és nyolcz ökröt ada a Mérári fiainak, az ő szolgálatuk szerint, Ithamárnak, Áron pap fiának keze alá.
ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
9 A Kéhát fiainak pedig semmit nem ada; mert a szentség szolgálata illette vala őket, a melyet vállon hordoznak vala.
Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
10 Vivének pedig a fejedelmek az oltár felszentelésére valókat azon napon, a melyen az felkenetett, és vivék a fejedelmek az ő áldozatukat az oltár elébe.
Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
11 És monda az Úr Mózesnek: Egyik napon egyik fejedelem, másik napon másik fejedelem vigye az ő áldozatát az oltár felszentelésére.
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
12 És vivé első napon az ő áldozatát Naasson, az Amminádáb fia, Júda nemzetségéből.
Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
13 Vala pedig az ő áldozata, egy ezüst tál, száz és harmincz siklus súlyú, egy ezüst medencze hetven siklus súlyú, a szent siklus szerint, és mind a kettő telve vala olajjal elegyített lisztlánggal, ételáldozatul.
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
14 Egy arany csésze, tíz siklus súlyú, füstölő szerekkel telve.
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
15 Egy fiatal tulok, egy kos, egy esztendős bárány egészen égőáldozatul.
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
16 Egy kecskebak bűnért való áldozatul.
mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
17 Hálaadó áldozatul pedig két ökör, öt kos, öt kecskebak, öt bárány, esztendősök. Ez Naassonnak, Amminádáb fiának áldozata.
ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
18 Másodnapon vivé Néthanéel, Suárnak fia, Izsakhár nemzetségének fejedelme.
Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
19 Vive az ő áldozatául egy ezüst tálat, száz és harmincz siklus súlyút, egy ezüst medenczét, hetven siklus súlyút, a szent siklus szerint, mind a kettő telve vala olajjal elegyített lisztlánggal, ételáldozatul.
Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
20 Egy arany csészét, tíz siklus súlyút, füstölő szerekkel telve.
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
21 Egy fiatal tulkot, egy kost, egy esztendős bárányt egészen égőáldozatul.
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
22 Egy kecskebakot bűnért való áldozatul.
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
23 Hálaadó áldozatul pedig két ökröt, öt kost, öt bakot, öt bárányt, esztendősöket. Ez Néthanéelnek a Suár fiának áldozata.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
24 Harmadik napon a Zebulon fiainak fejedelme: Eliáb, Hélon fia.
Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
25 Az ő áldozata volt egy ezüst tál, száz harmincz siklus súlyú, egy ezüst medencze, hetven siklus súlyú, a szent siklus szerint, mind a kettő telve vala olajjal elegyített lisztlánggal, ételáldozatul.
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
26 Egy arany csésze, tíz siklus súlyú füstölő szerekkel telve.
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
27 Egy fiatal tulok, egy kos, egy esztendős bárány, egészen égőáldozatul.
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
28 Egy kecskebak, bűnért való áldozatul.
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
29 Hálaadó áldozatul pedig két ökör, öt kos, öt bak, öt bárány, esztendősök. Ez Eliábnak, Hélon fiának áldozata.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
30 Negyedik napon a Rúben fiainak fejedelme: Elisúr, Sedeúrnak fia.
Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
31 Az ő áldozata volt egy ezüst tál, száz harmincz siklus súlyú, egy ezüst medencze, hetven siklus súlyú, a szent siklus szerint, mind a kettő telve vala olajjal elegyített lisztlánggal, ételáldozatul.
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
32 Egy arany csésze, tíz siklus súlyú, füstölő szerekkel telve.
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
33 Egy fiatal tulok, egy kos, egy esztendős bárány, egészen égőáldozatul.
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
34 Egy kecskebak bűnért való áldozatul.
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
35 Hálaadó áldozatul pedig két ökör, öt kos, öt bak, öt bárány, esztendősök. Ez Elisúrnak, Sedeúr fiának áldozata.
ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
36 Ötödnapon a Simeon fiainak fejedelme: Selúmiel, Surisaddai fia.
Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
37 Az ő áldozata volt egy ezüst tál, száz harmincz siklus súlyú, egy ezüst medencze, hetven siklus súlyú, a szent siklus szerint, mind a kettő telve vala olajjal elegyített lisztlánggal, ételáldozatul.
Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
38 Egy arany csésze, tíz siklus súlyú, füstölő szerekkel telve.
mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
39 Egy fiatal tulok, egy kos, egy esztendős bárány, egészen égőáldozatul.
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
40 Egy kecskebak, bűnért való áldozatul.
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
41 Hálaadó áldozatul pedig két ökör, öt kos, öt bak, öt bárány, esztendősök. Ez Selúmielnek, Surisaddai fiának áldozata.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
42 Hatodnapon a Gád fiainak fejedelme: Éliásáf, a Dehuél fia.
Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
43 Az ő áldozata volt egy ezüst tál, száz harmincz siklus súlyú, egy ezüst medencze, hetven siklus súlyú, a szent siklus szerint, mind a kettő telve vala olajjal elegyített lisztlánggal, ételáldozatul.
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
44 Egy arany csésze, tíz siklus súlyú, füstölő szerekkel telve.
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
45 Egy fiatal tulok, egy kos, egy esztendős bárány, egészen égőáldozatul.
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
46 Egy kecskebak bűnért való áldozatul.
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
47 Hálaadó áldozatul pedig két ökör, öt kos, öt bak, öt bárány, esztendősök. Ez Eliásáfnak, Dehuél fiának áldozata.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
48 Hetednapon az Efraim fiainak fejedelme: Elisáma, az Ammihúd fia.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
49 Az ő áldozata volt egy ezüst tál, száz harmincz siklus súlyú, egy ezüst medencze, hetven siklus súlyú, a szent siklus szerint, mind a kettő telve vala olajjal elegyített lisztlánggal, ételáldozatul.
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
50 Egy arany csésze, tíz siklus súlyú, füstölő szerekkel telve.
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
51 Egy fiatal tulok, egy kos, egy esztendős bárány, egészen égőáldozatul.
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
52 Egy kecskebak bűnért való áldozatul.
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
53 Hálaadó áldozatul pedig két ökör, öt kos, öt bak, öt bárány, esztendősök. Ez Elisámának, Ammihúd fiának áldozata.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
54 Nyolczadnapon a Manasse fiainak fejedelme: Gamliél, Pédasúr fia.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
55 Az ő áldozata volt egy ezüst tál, száz harmincz siklus súlyú, egy ezüst medencze, hetven siklus súlyú, a szent siklus szerint, mind a kettő telve vala olajjal elegyített lisztlánggal, ételáldozatul.
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
56 Egy arany csésze, tíz siklus súlyú, füstölő szerekkel telve.
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
57 Egy fiatal tulok, egy kos, egy esztendős bárány egészen égőáldozatul.
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
58 Egy kecskebak bűnért való áldozatul.
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
59 Hálaadó áldozatul pedig két ökör, öt kos, öt bak, öt bárány, esztendősök. Ez Gámliélnek, a Pédasúr fiának áldozata.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
60 Kilenczednapon a Benjámin fiainak fejedelme: Abidán, a Gideóni fia.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
61 Az ő áldozata volt egy ezüst tál, száz harmincz siklus súlyú, egy ezüst medencze hetven siklus súlyú, a szent siklus szerint, mind a kettő telve vala olajjal elegyített lisztlánggal, ételáldozatul.
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
62 Egy arany csésze, tíz siklus súlyú, füstölő szerekkel telve.
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
63 Egy fiatal tulok, egy kos, egy esztendős bárány egészen égőáldozatul.
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
64 Egy kecskebak bűnért való áldozatul.
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
65 Hálaadó áldozatul pedig két ökör, öt kos, öt bak, öt bárány, esztendősök. Ez Abidánnak, Gideóni fiának áldozata.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
66 Tizedik napon a Dán fiainak fejedelme: Ahiézer, az Ammisaddai fia.
Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
67 Az ő áldozata volt egy ezüst tál, száz harmincz siklus súlyú, egy ezüst medencze hetven siklus súlyú, a szent siklus szerint, mind a kettő telve vala olajjal elegyített lisztlánggal, ételáldozatul.
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
68 Egy arany csésze, tíz siklus súlyú, füstölő szerekkel telve.
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
69 Egy fiatal tulok, egy kos, egy esztendős bárány egészen égőáldozatul.
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
70 Egy kecskebak bűnért való áldozatul.
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
71 Hálaadó áldozatul pedig két ökör, öt kos, öt bak, öt bárány, esztendősök. Ez Ahiézernek, az Ammisaddai fiának áldozata.
ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
72 Tizenegyedik napon az Áser fiainak fejedelme: Págiel, Okrán fia.
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
73 Az ő áldozata volt egy ezüst tál, száz harmincz siklus súlyú, egy ezüst medencze, hetven siklus súlyú, a szent siklus szerint, mind a kettő telve vala olajjal elegyített lisztlánggal, ételáldozatul.
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
74 Egy arany csésze, tíz siklus súlyú, füstölő szerekkel telve.
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
75 Egy fiatal tulok, egy kos, egy esztendős bárány egészen égőáldozatul.
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
76 Egy kecskebak bűnért való áldozatul.
mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
77 Hálaadó áldozatul pedig két ökör, öt kos, öt bak, öt bárány, esztendősök. Ez Págielnek, Okrán fiának áldozata.
ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
78 Tizenkettedik napon a Nafthali fiainak fejedelme: Ahira, Enán fia.
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
79 Az ő áldozata volt egy ezüst tál, száz harmincz siklus súlyú, egy ezüst medencze, hetven siklus súlyú, a szent siklus szerint, mind a kettő telve vala olajjal elegyített lisztlánggal, ételáldozatul.
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
80 Egy arany csésze, tíz siklus súlyú, füstölő szerekkel telve.
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
81 Egy fiatal tulok, egy kos, egy esztendős bárány egészen égőáldozatul.
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
82 Egy kecskebak bűnért való áldozatul.
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
83 Hálaadó áldozatul pedig két ökör, öt kos, öt bak, öt bárány, esztendősök. Ez Ahirának, az Enán fiának áldozata.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
84 Ez volt az áldozat az oltár felszentelésére, a napon, a melyen felkenetett, az Izráelnek fejedelmeitől. Tizenkét ezüst tál, tizenkét ezüst medencze, tizenkét arany csésze.
Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
85 Száz és harmincz siklus súlyú vala egy ezüst tál, egy ezüst medencze pedig hetven siklus súlyú; az edények minden ezüstje: kétezer négyszáz siklus, a szent siklus szerint;
Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
86 Tizenkét arany csésze, füstölő szerekkel, tíz-tíz siklus súlyú vala egy-egy csésze, a szent siklus szerint: A csészéknek minden aranya: száz húsz siklus.
Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
87 Az egészen égőáldozatra való minden barom: tizenkét tulok, tizenkét kos, esztendős bárány tizenkettő, a hozzájok való ételáldozatokkal, és tizenkét kecskebak bűnért való áldozatul.
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
88 A hálaadó áldozatra való minden barom pedig: huszonnégy tulok, hatvan kos, hatvan bak, esztendős bárány hatvan. Ez volt az oltár felszentelésére való áldozat, minekutána felkenetett volt.
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
89 Mikor pedig bemegy vala Mózes a gyülekezet sátorába, hogy szóljon ő vele, hallja vala annak szavát, a ki szól vala vele a fedél felől, amely van a bizonyság ládáján, a két Kérub közűl; és szól vala vele.
Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.

< 4 Mózes 7 >