< Ezera 6 >
1 A LAILA kauoha ae la o Dariu ke alii, imihia ma ka hale o na palapala, kahi i waiho ai na waiwai ilaila ma Babulona.
Atalandira mawuwo mfumu Dariyo anapereka lamulo ndipo kafukufuku anachitikadi ku Babuloni mʼnyumba yosungira chuma ndi mabuku ambiri yakale.
2 A loaa iho la, ma Akemeta, ma ka halealii, o ko Media, he palapala, a peneia ka olelo i kakauia'i maloko.
Ndipo ku Ekibatana, likulu la dera la Mediya, kunapezeka mpukutu mmene munalembedwa kuti, Chikumbutso:
3 I ka makahiki mua o Kuro ke alii, kauoha ae la o ua Kuro la ke alii no ka hale o ke Akua ma Ierusalema, E hauaia ka hale, kahi i kaumaha aku ai i na mohai, a e hoonohopaaia ke kumu; he kanaono hailima ke kiekie, a he kanaono hailima ka laula;
Mʼchaka choyamba cha ufumu wa Koresi, mfumuyo inapereka lamulo lokhudza Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Analamula kuti Nyumba ya Mulungu imangidwenso kukhala malo woperekerako nsembe. Maziko ake amangidwe kolimba pa malo pomwe paja pali maziko ake akale ndipo mulitali mwake mukhale mamita 27, mulifupi mwake mukhale mamita 27.
4 Pakolu na papapohaku kalai, a e pakahi hoi ka papa laau hou; a e haawiia ka waiwai mai ka hale o ke alii mai:
Mumange mizere itatu ya miyala yayikulu ndi mzere umodzi wa matabwa, ndalama zake zolipirira ntchitoyo zichokere mʼthumba la ufumu.
5 A o na kiaha gula hoi a me ke kala o ka hale o ke Akua, na mea a Nebukaneza i lawe ae mai ka luakini mai ma Ierusalema, a hali mai i Babulona, e hoihoiia'ku, a e haliia aku i ka luakini ma Ierusalema, o kela keia ma kona wahi iho, a e waiho ma ka hale o ke Akua.
Ndipo ziwiya zagolide ndi zasiliva za ku Nyumba ya Mulungu zimene Nebukadinezara anatenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu kupita nazo ku Babuloni, zonsezi zibwezedwe ndipo zipite ku Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu. Chilichonse chikabwezedwe pamalo pake mʼNyumbayo.
6 Ano hoi, e Tatenai, ke kiaaina ma kela aoao o ka muliwai, a me Setare bozenai, a me ko laua poe hoalawehana, ka poe Aparesaka, ma kela aoao o ka muliwai, e hookaawaleia oukou mai ia wahi aku.
Tsopano Tatenai, bwanamkubwa wa dera la Patsidya pa Yufurate ndiponso Setari-Bozenai pamodzi ndi anzanu muchokeko kumeneko.
7 E waiho malie oukou i ka hana o keia hale o ke Akua; a o ke alii kiaaina o na Iudaio, a me ka poe kahiko o na Iudaio, e hana lakou i keia hale o ke Akua ma kona wahi.
Ntchito yomanga Nyumba ya Mulunguyi muyileke. Mulekeni bwanamkubwa wa Ayuda ndiponso akuluakulu a Ayuda kuti amangenso Nyumba ya Mulunguyo pamalo pake.
8 Eia hoi ka'u o kauoha aku nei i ka mea a oukou e hana aku ai i na lunakahiko o keia poe Iudaio, no ka hana ana i keia hale o ke Akua: noloko mai o ka waiwai o ke alii, oia ka hookupu ma kela aoao o ka muliwai, e haawi koke ia'ku ka waiwai no keia poe kanaka, i keakea ole ia'i lakou.
Kuwonjezera pamenepo, ndikukhazikitsa lamulo lonena za mmene mudzachitire ndi akuluakulu a Ayuda powathandiza kumanganso Nyumba ya Mulunguyo: Anthuwa muwalipire msanga kuchokera mʼthumba la ufumu, kuchotsa pa msonkho wa dera la Patsidya pa Yufurate.
9 A o na mea e pono ai lakou, o na keikibipikane, a o na hipakane, a me na keikihipa, no na mohaikuni na ke Akua o ka lani, o ka palaoa, ka paakai, o ka waina, a me ka aila, e like me ke kauoha a na kahuna ma Ierusalema, e haawiia'ku ia na lakou i kela la keia la, aole ka ole:
Ndipo zonse zofunikira monga, ana angʼombe, nkhosa zazimuna, ana ankhosa aamuna zoperekera nsembe yopsereza kwa Mulungu wakumwamba, ndi tirigu, mchere, vinyo ndi mafuta monga mmene ansembe a ku Yerusalemu angafunire, muziwapatsa zimenezo tsiku ndi tsiku ndipo musamalephere kutero.
10 I kaumaha aku ai lakou i na mea ala i ke Akua o ka lani, a i pule aku hoi no ke ola o ke alii, a no kana mau keiki.
Zikatero ndiye kuti azipereka nsembe za fungo lokomera Mulungu wakumwamba ndi kupempherera moyo wa mfumu ndi ana ake.
11 A ke kauoha aku nei no hoi au, o kela kanaka keia kanaka e hoololi i keia olelo, e laweia ka laau mai kona hale mai, a kukuluia, e kaaweia oia maluna o ia mea, a e hooliloia kona hale i puu lepo no keia mea.
Ndikulamulanso kuti ngati wina asintha zimene ndalamulazi, mtanda umodzi wa nyumba yake udzasololedwa ndi kumunkhomera pamenepo ndipo nyumba yake adzayisandutse dzala.
12 A o ke Akua, nana i waiho kona inoa malaila, e luku aku ia i na'lii a pau, a me na kanaka, ke o aku ko lakou lima e hoololi, a e wawahi i keia hale o ke Akua ma Ierusalema. Owau, o Dariu ka i kauoha aku; e hana koke ia hoi oia.
Mulungu amene anasankha kuti anthu azimupembedza pa malo amenewa, achotse mfumu iliyonse kapena munthu aliyense amene adzasinthe zimenezi kapena kuwononga Nyumba ya Mulungu ya ku Yerusalemuko. Ine Dariyo ndikuyika lamuloli, aliyense alitsate mosamala kwambiri.
13 Alaila o Tatenai, ke kiaaina ma keia aoao o ka muliwai, e Setare-bozenai, a me ko laua hoalawehana, e like me ka mea a ke alii i hoouna mai ai, pela lakou i hana koke aku ai.
Tsono potsata zomwe analamula mfumu Dariyo, Tatenai bwanamkubwa wa dera la Patsidya pa Yufurate, Setari-Bozenai ndi anzawo anatsatira mosamala kwambiri zimene mfumu Dariyo analamula.
14 A hana aku la na luna kahiko o na Iudaio, a ua pomaikai lakou ma ka wanana a Hagai ke kaula, a me Zakaria ke keiki a Ido. A hana lakou, a hoopaa hoi, e like me ke kauoha a ke Akua o ka Iseraela, a like hoi me ke kauoha a Kuro, a me Dariu, a me Aretasaseta, ke alii o Peresia.
Ndipo akuluakulu a Ayuda anapitiriza ntchito yomanga ija molimbikitsidwa ndi aneneri Hagai ndi Zekariya mwana wa Ido. Anamaliza ntchito yomanga Nyumbayo, monga momwe Mulungu wa Israeli analamulira ndiponso potsata lamulo la Koresi, Dariyo ndi Aritasasita, mafumu a ku Perisiya.
15 A ua hoopaaia keia hale i ke kolu o ka la o ka malama Adara, oia ke oao o ka makahiki a Dariu ke alii i noho alii ai.
Anatsiriza kumanga Nyumbayo pa tsiku lachitatu la mwezi wa Adara mʼchaka chachisanu ndi chimodzi cha ulamuliro wa mfumu Dariyo.
16 A o na mamo a Iseraela, na kahuna, a me na Levi, a me na mea i koe o ka poe i pio, hoolaa aku la lakou i keia hale o ke Akua me ka olioli.
Choncho Aisraeli, ansembe, Alevi ndi anthu ena onse amene anali atabwerako ku ukapolo, anachita chikondwerero chopereka Nyumba ya Mulungu mwachimwemwe.
17 A kaumaha aku la no ka hoolaa ana i keia hale o ke Akua, i hookahi haneri bipikane, i elua haneri hipakane, a i eha haneri keikihipa; a i umikumamalua na kaokane i mohaihala no ka Iseraela a pau, e like me na ohana o ka Iseraela.
Poporeka Nyumba ya Mulunguyi, anthu anapereka nsembe za ngʼombe zazimuna 100, nkhosa zazimuna 200, ana ankhosa aamuna 400. Anaperekanso mbuzi zazimuna 12 ngati nsembe yopepesera machimo a anthu onse, potsata chiwerengero cha mafuko a Israeli.
18 A hoonoho iho la lakou i na kahuna ma ko lakou mau papa, a me na Levi ma ko lakou mau papa, no ka oihana o ke Akua ma Ierusalema; e like me ko kauoha ma ka buke a Mose.
Ndipo anakhazikitsa ansembe ndi Alevi pa ntchito zawo zotumikira Mulungu mu Yerusalemu monga zinalembedwera mʼbuku la Mose.
19 A malama aku la ka poe i pio i ka moliaola, i ka la umikumamaha o ka malama mua.
Pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba, obwera ku ukapolo aja anachita chikondwerero cha Paska.
20 No ka mea, ua huikala pu ia na kahuna, a me na Levi, a ua maemae lakou a pau, a kalua aku la lakou i ka moliaola, no ka poe i pio a pau, a no ko lakou poe hoahanau na kahuna, a no lakou iho.
Ansembe ndi Alevi anali atadziyeretsa ndipo onsewo anali oyeretsedwa. Alevi anapha mwana wankhosa wa Paska kuphera onse amene anatuluka ku ukapolo, ansembe anzawo ndi iwo eni.
21 A ai iho la na mamo a Iseraela, ka poe i hoi mai, mai ke pio ana mai, a me ka poe a pau i hookaawale ia lakou iho mai ka mea haumia o na lahuikanaka o ka aina, e imi ia Iehova ke Akua o ka Iseraela;
Nkhosa ya Paskayo anayidya ndi Aisraeli onse amene anatuluka ku ukapolo, wina aliyense amene anaphatikana nawo atadziyeretsa ku zonyansa za mitundu ina ya anthu akunja a mʼdzikomo kuti apembedze Yehova Mulungu wa Israeli.
22 A malama lakou i ka ahaaina berena hu ole i na la ehiku me ka olioli: no ka mea, o Iehova ka i hoohauoli mai ia lakou, a hoohuli mai i ka naau o ke alii o Asuria ia lakou, e hooikaika i ko lakou lima i ka hana ana i ka hale o ke Akua, ke Akua o ka Iseraela.
Choncho pa masiku asanu ndi awiri anasangalala pa chikondwerero cha buledi wopanda yisiti, chifukwa Yehova anawadzaza ndi chimwemwe. Iye anatembenuza mtima wa mfumu ya ku Asiriya motero kuti iyo inakomera mtima Aisraeli ndi kuwathandiza ntchito yomanga Nyumba ya Mulungu, Mulungu wa Israeli.