< 2 Samuel 8 >
1 Und es geschah danach, daß David die Philister schlug und sie niederbeugte, und David nahm Metheg-Ammah aus der Hand der Philister.
Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.
2 Und er schlug Moab und maß sie mit der Schnur, so daß er sie zur Erde ließ niederliegen und zwei Schnüre maß, um zu töten, und eine volle Schnur am Leben zu lassen. Und es ward Moab dem David zu Knechten, daß sie ihm Geschenke zutrugen.
Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.
3 Und David schlug Hadadeser, Rechobs Sohn, König von Zobah, da er hinzog, seine Hand zurückzuwenden am Flusse.
Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
4 Und David nahm von ihm tausendsiebenhundert Reiter und zwanzigtausend Mann zu Fuß, und David lähmte alle Streitwagen und ließ hundert Streitwagen von ihnen übrig.
Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
5 Und Aram Damaskus kam, dem Hadadeser, König von Zobah, beizustehen; und David schlug dem Aram zweiund- zwanzigtausend Mann.
Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
6 Und David legte Besatzungen Aram Damaskus, und Aram ward David zu Knechten und trugen Geschenke zu, und Jehovah half dem David überall, wohin er ging.
Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
7 Und David nahm die goldenen Schilde, welche die Knechte Hadadesers hatten, und brachte sie nach Jerusalem,
Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
8 Und von Betach und von Berothai, Städten Hadadesers, nahm König David sehr viel Erz.
Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.
9 Und Thoi, König von Chamath, hörte, daß David die ganze Streitmacht Hadadesers geschlagen;
Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri,
10 Und Thoi sandte seinen Sohn Joram zu König David, um sein Wohlsein zu erfragen, und ihn zu segnen dafür, daß er wider Hadadeser gestritten und ihn geschlagen hätte, denn Thoi war ein Mann des Streites wider Hadadeser; und in seiner Hand waren Gefäße von Silber und Gefäße von Gold und Gefäße von Erz.
anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.
11 Auch sie heiligte König David dem Jehovah mit dem Silber und dem Gold, das er von allen Völkerschaften, die er unterworfen, geheiligt hatte.
Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa:
12 Von Syrien und von Moab und von den Söhnen Ammons und von den Philistern und von Amalek und von der Beute Hadadesers, Rechobs Sohne, König von Zobah.
Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.
13 Und David machte sich einen Namen, als er zurückkam, nachdem er von dem Aram im Salztal achtzehntausend geschlagen.
Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
14 Und er legte Besatzungen in Edom, in ganz Edom legte er Besatzungen, und ganz Edom wurde dem David zum Knechte, und Jehovah half dem David in allem, wo er hinging.
Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
15 Und David regierte über ganz Israel, und David tat Recht und Gerechtigkeit all seinem Volke.
Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
16 Und Joab, Zerujahs Sohn, war über das Heer, und Joschaphat, der Sohn Achiluds, war Kanzler.
Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika.
17 Und Zadok, der Sohn Achitubs, und Achimelech, der Sohn Abjathars, waren Priester, und Serajah war Schreiber.
Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi;
18 Und da waren Benajahu, der Sohn Jehojadas, und die Krethi und Plethi, und die Söhne Davids waren Priester.
Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.