< Psalm 76 >

1 Dem Musikmeister, mit Saitenspiel; ein Psalm von Asaph, ein Lied. Allbekannt ist Gott in Juda,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
2 in Salem erstand seine Hütte und seine Wohnstatt in Zion.
Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
3 Allda hat er zerbrochen des Bogens Blitze, Schild und Schwert und jegliche Kriegswehr. (SELA)
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
4 Ruhmvoll bist du, herrlich von den ewigen Bergen her.
Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
5 Ausgeplündert wurden die tapferen Streiter, sanken hin in ihren Todesschlaf, und all den Helden versagte der Arm:
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
6 vor deinem Drohruf, du Gott Jakobs, sanken in Betäubung so Wagen wie Rosse.
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
7 Ja du bist furchtbar, und wer kann bestehn vor dir, sobald dein Zorn entbrannt ist?
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
8 Vom Himmel her kündigtest du das Gericht an: da erschrak die Erde und wurde still,
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
9 als Gott sich erhob zum Gerichtsvollzug, um allen Bedrückten auf Erden zu helfen. (SELA)
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
10 Denn der Menschen Grimm wird dir zum Lobpreis, wenn zuletzt du dich gürtest mit Zornesflammen.
Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
11 Bringt Gelübde dar und erfüllt sie dem HERRN, eurem Gott: alle, die ihn rings umgeben, müssen Geschenke dem Schrecklichen bringen,
Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
12 ihm, der den Hochmut der Fürsten dämpft und furchtbar ist den Königen der Erde.
Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.

< Psalm 76 >