< Psalm 120 >
1 Ein Wallfahrtslied. Ich rief zum HERRN in meiner Not:
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
2 O HERR, errette mich von der Lügenlippe, von der trügerischen Zunge!
Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
3 Was wird Er dir jetzt und in Zukunft bescheren, du trügerische Zunge?
Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
4 Geschärfte Kriegerpfeile samt Kohlen vom Ginsterstrauch!
Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
5 Wehe mir, daß ich als Fremdling in Mesech weile, daß ich wohne bei den Zelten von Kedar!
Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
6 Lange genug schon weile ich hier bei Leuten, die den Frieden hassen.
Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
7 Ich bin ganz friedlich gestimmt, doch was ich auch rede: sie gehen auf Krieg aus.
Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.