< Psalm 103 >
1 Von David. Lobe den HERRN, meine Seele,
Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
2 Lobe den HERRN, meine Seele, und vergiß nicht, was er dir Gutes getan!
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
3 Der dir alle deine Schuld vergibt und alle deine Gebrechen heilt;
Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
4 der dein Leben erlöst vom Verderben, der dich krönt mit Gnade und Erbarmen;
amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
5 der dein Alter mit guten Gaben sättigt, daß, dem Adler gleich, sich erneut deine Jugend.
amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
6 Gerechtigkeit übt der HERR, schafft allen Unterdrückten ihr Recht;
Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
7 er hat Mose seine Wege kundgetan, den Kindern Israel seine Großtaten.
Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
8 Barmherzig und gnädig ist der HERR, voller Langmut und reich an Güte;
Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
9 er wird nicht ewig hadern und den Zorn nicht immerdar festhalten;
Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
10 er handelt nicht mit uns nach unsern Sünden und vergilt uns nicht nach unsern Missetaten;
satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
11 nein, so hoch der Himmel über der Erde ist, so groß ist seine Gnade über denen, die ihn fürchten;
Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
12 so fern der Sonnenaufgang ist vom Niedergang, läßt er unsre Verschuldungen fern von uns sein;
monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
13 wie ein Vater sich über die Kinder erbarmt, so erbarmt der HERR sich derer, die ihn fürchten.
Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
14 Denn er weiß, welch ein Gebilde wir sind, er denkt daran, daß wir Staub sind.
pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
15 Der Mensch – dem Grase gleicht seine Lebenszeit, wie die Blume des Feldes, so blüht er:
Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
16 wenn ein Windstoß über sie hinfährt, ist sie dahin, und ihr Standort weiß nichts mehr von ihr.
koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
17 Doch die Gnade des HERRN erweist sich von Ewigkeit zu Ewigkeit an denen, die ihn fürchten, und seine Gerechtigkeit besteht für Kindeskinder
Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
18 bei denen, die seinen Bund bewahren und seiner Gebote gedenken, um sie auszuführen.
iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
19 Der HERR hat seinen Thron im Himmel festgestellt, und seine Königsmacht umschließt das All.
Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
20 Lobet den HERRN, ihr seine Engel, ihr starken Helden, die ihr sein Wort vollführt, gehorsam der Stimme seines Gebots!
Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
21 Lobet den HERRN, alle seine Heerscharen, ihr seine Diener, Vollstrecker seines Willens!
Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
22 Lobet den HERRN, alle seine Werke an allen Orten seiner Herrschaft! Lobe den HERRN, meine Seele!
Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.