< 1 Mose 5 >

1 Dies ist die Geschlechtstafel Adams: Am Tage, als Gott den Adam schuf, gestaltete er ihn nach Gottes Ebenbild;
Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
2 als Mann und Weib schuf er sie und segnete sie und gab ihnen den Namen »Mensch« damals, als sie geschaffen wurden.
Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
3 Adam aber war 130 Jahre alt, als ihm ein Sohn geboren wurde, der ihm als sein Abbild glich und den er Seth nannte.
Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
4 Nach der Geburt Seths lebte Adam noch 800 Jahre und hatte Söhne und Töchter.
Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
5 Demnach betrug die ganze Lebenszeit Adams 930 Jahre; dann starb er. –
Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
6 Als Seth 105 Jahre alt war, wurde ihm Enos geboren.
Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
7 Nach der Geburt des Enos lebte Seth noch 807 Jahre und hatte Söhne und Töchter.
Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
8 Demnach betrug die ganze Lebenszeit Seths 912 Jahre; dann starb er. –
Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
9 Als Enos 90 Jahre alt war, wurde ihm Kenan geboren.
Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
10 Nach der Geburt Kenans lebte Enos noch 815 Jahre und hatte Söhne und Töchter.
Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
11 Demnach betrug die ganze Lebenszeit des Enos 905 Jahre; dann starb er. –
Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
12 Als Kenan 70 Jahre alt war, wurde ihm Mahalalel geboren.
Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
13 Nach der Geburt Mahalalels lebte Kenan noch 840 Jahre und hatte Söhne und Töchter.
Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
14 Demnach betrug die ganze Lebenszeit Kenans 910 Jahre; dann starb er. –
Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
15 Als Mahalalel 65 Jahre alt war, wurde ihm Jered geboren.
Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
16 Nach der Geburt Jereds lebte Mahalalel noch 830 Jahre und hatte Söhne und Töchter.
Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
17 Demnach betrug die ganze Lebenszeit Mahalalels 895 Jahre; dann starb er. –
Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
18 Als Jered 162 Jahre alt war, wurde ihm Henoch geboren.
Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
19 Nach der Geburt Henochs lebte Jered noch 800 Jahre und hatte Söhne und Töchter.
Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
20 Demnach betrug die ganze Lebenszeit Jereds 962 Jahre; dann starb er. –
Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
21 Als Henoch 65 Jahre alt war, wurde ihm Methusalah geboren.
Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
22 Henoch wandelte mit Gott; er lebte nach der Geburt Methusalahs noch 300 Jahre und hatte Söhne und Töchter.
Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
23 Demnach betrug die ganze Lebenszeit Henochs 365 Jahre.
Zaka zonse za Enoki zinali 365.
24 Henoch wandelte mit Gott und war plötzlich nicht mehr da, denn Gott hatte ihn hinweggenommen. –
Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
25 Als Methusalah 187 Jahre alt war, wurde ihm Lamech geboren.
Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
26 Nach der Geburt Lamechs lebte Methusalah noch 782 Jahre und hatte Söhne und Töchter.
Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
27 Demnach betrug die ganze Lebenszeit Methusalahs 969 Jahre; dann starb er. –
Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
28 Als Lamech 182 Jahre alt war, wurde ihm ein Sohn geboren,
Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
29 den er Noah nannte; »denn«, sagte er, »dieser wird uns Trost verschaffen bei unserer Arbeit und bei der Mühsal, die unsere Hände durch den Acker haben, den der HERR verflucht hat«.
Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
30 Nach der Geburt Noahs lebte Lamech noch 595 Jahre und hatte Söhne und Töchter.
Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
31 Demnach betrug die ganze Lebenszeit Lamechs 777 Jahre; dann starb er. –
Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
32 Als Noah 500 Jahre alt war, wurden ihm seine Söhne Sem, Ham und Japheth geboren.
Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.

< 1 Mose 5 >