< Psalm 97 >
1 Der HERR ist König; des freue sich das Erdreich und seien fröhlich die Inseln, soviel ihrer sind.
Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
2 Wolken und Dunkel ist um ihn her; Gerechtigkeit und Gericht ist seines Stuhles Festung.
Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 Feuer geht vor ihm her und zündet an umher seine Feinde.
Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 Seine Blitze leuchten auf den Erdboden; das Erdreich siehet's und erschrickt.
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 Die Berge zerschmelzen wie Wachs vor dem HERRN, vor dem Herrscher des ganzen Erdbodens.
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 Die Himmel verkündigen seine Gerechtigkeit, und alle Völker sehen seine Ehre.
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 Schämen müssen sich alle, die den Bildern dienen und sich der Götzen rühmen. Betet ihn an, alle Götter!
Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
8 Zion hört es und ist froh; und die Töchter Juda's sind fröhlich, HERR, über dein Regiment.
Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 Denn du, HERR, bist der Höchste in allen Landen; du bist hoch erhöht über alle Götter.
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 Die ihr den HERRN liebet, hasset das Arge! Der HERR bewahret die Seelen seiner Heiligen; von der Gottlosen Hand wird er sie erretten.
Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 Dem Gerechten muß das Licht immer wieder aufgehen und Freude den frommen Herzen.
Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 Ihr Gerechten freuet euch des HERRN und danket ihm und preiset seine Heiligkeit!
Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.