< Psaumes 122 >
1 Cantique graduel. De David. Je me réjouis, quand on me dit: Allons à la maison de l'Éternel!
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
2 Nos pieds s'arrêtent dans tes Portes, Jérusalem!
Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
3 Jérusalem, bâtie comme une ville où les édifices se lient l'un à l'autre,
Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
4 rendez-vous des tribus, des tribus de l'Éternel, selon l'ordre donné à Israël, qui vient pour y louer le nom de l'Etemel!
Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
5 Car des trônes y sont placés pour le siège de la justice, les trônes de la maison de David.
Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
6 Faites des vœux pour la prospérité de Jérusalem! Heureux soient ceux qui t'aiment!
Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
7 Que la paix soit dans tes murs, et la sécurité dans tes palais!
Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
8 En faveur de mes frères et de mes amis, je veux implorer le salut pour toi;
Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
9 en faveur de la maison de l'Éternel, notre Dieu, je demanderai pour toi le bonheur.
Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.