< Lévitique 21 >

1 Et l'Éternel parla à Moïse: Parle aux Prêtres, fils d'Aaron, et leur dis: Nul ne se mettra pour un mort en état d'impureté dans son peuple,
Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi ansembe, ana a Aaroni, ndipo uwawuze kuti, ‘Wansembe asadzidetse pokhudza munthu wakufa pakati pa abale ake.
2 excepté pour les plus proches parents du même sang que lui, pour sa mère ou son père, ou son fils ou sa fille, ou son frère,
Koma akhoza kukhudza thupi lakufa la amayi ake, abambo ake, mwana wake wamwamuna, mwana wake wamkazi, mchimwene wake,
3 ou pour sa sœur vierge qui est avec lui, et n'a pas encore un mari: pour celle-ci il pourra se mettre en état d'impureté.
kapena mlongo wake wosakwatiwa amene amadalira iye chifukwa sanakwatiwe. Iye akhoza kudzidetsa pokhudza thupi lakufa la mchemwali wake wosakwatiwa yekha.
4 Comme mari il ne doit pas se mettre en état d'impureté dans son peuple pour se profaner.
Koma wansembe asadzidetse chifukwa cha anthu amene ali nawo pa ubale obwera chifukwa cha ukwati.
5 Ils ne se raseront point la tête, ne se couperont point les coins de la barbe et ne se feront sur le corps point d'incisions.
“‘Ansembe asamete tsitsi kumutu kwawo kapena mʼmphepete mwa ndevu zawo, kapenanso kudzichekacheka pa thupi lawo.
6 Ils seront saints en vue de leur Dieu, et ne profaneront pas le nom de leur Dieu, car ils offrent les sacrifices ignés de l'Éternel, l'aliment de leur Dieu; qu'ils soient donc en état de sainteté.
Ayenera kukhala oyera pamaso pa Mulungu wawo ndipo asachititse manyazi dzina la Mulungu wawo. Popeza amapereka nsembe zotentha pa moto kwa Yehova, chakudya cha Mulungu wawo, iwo azikhala woyera.
7 Ils n'épouseront ni une prostituée, ni une femme déshonorée, ils n'épouseront pas non plus une femme répudiée par son mari, car ils sont consacrés à leur Dieu.
“‘Asakwatire akazi amene adzidetsa ndi chiwerewere kapena akazi amene amuna awo awasudzula, chifukwa ansembe ndi oyera pamaso pa Mulungu wawo.
8 Maintiens-les donc dans l'état de sainteté, car ils présentent le pain de leur Dieu; qu'ils soient sacrés pour toi, car je suis Saint, moi l'Éternel qui veux vous rendre saints.
Iwo akhale oyera chifukwa amapereka nsembe kwa Mulungu wanu. Muziwaona kuti ndi oyera, popeza Ine Yehova amene ndimawayeretsa ndine woyera, nawonso akhale oyera.
9 Et la fille d'un personnage sacerdotal qui se met à être impudique, profane son père; elle sera brûlée au feu.
“‘Ngati mwana wamkazi wa wansembe adziyipitsa pochita zachiwerewere, ndiye kuti iye akuchititsa manyazi abambo ake; mwanayo atenthedwe pa moto.
10 Et le Prêtre qui a la prééminence sur ses frères, qui a reçu sur sa tête l'effusion de l'huile d'onction, qui à son installation a été revêtu du costume, ne doit ni laisser sa tête échevelée ni déchirer ses vêtements,
“‘Munthu amene ali mkulu wa ansembe pakati pa abale ake, amene anamudzoza pomutsanulira mafuta pamutu pake, ndiponso amene anapatulidwa pomuveka zovala zaunsembe, asalekerere tsitsi lake kapena kungʼamba zovala zake kusonyeza kuti ali pa chisoni.
11 et il ne s'approchera d'aucun mort; même pour un père ou une mère il ne se mettra pas en état d'impureté.
Asalowe mʼnyumba mmene muli munthu wakufa ngakhale womwalirayo ndi amayi ake kapena abambo ake.
12 Et il ne sortira pas du Sanctuaire, afin de ne pas profaner le Sanctuaire de son Dieu, car il porte la consécration de l'huile d'onction de son Dieu. Je suis l'Éternel.
Asadzidetse potulukira kunja kwa malo opatulika popeza mafuta womupatula kukhala wansembe ali pamutu pake. Ine ndine Yehova.
13 Il prendra une femme qui ait sa virginité,
“‘Iye akwatire namwali wosadziwa mwamuna.
14 et il n'épousera ni une veuve, ni une femme répudiée ou déshonorée ou impudique: mais il choisira une vierge dans son peuple.
Asakwatire mkazi wamasiye, mkazi wosudzulidwa, kapena mkazi wachiwerewere, koma akwatire namwali wosadziwa mwamuna pakati pa anthu a mtundu wake,
15 Et il ne profanera point sa race au milieu de son peuple; car je suis l'Éternel qui le consacre.
kuti mtundu wake usakhale wodetsedwa pakati pa abale popeza ndine Yehova, amene ndimamuyeretsa.’”
16 Et l'Éternel parla à Moïse et dit: Parle à Aaron en ces termes:
Yehova anawuza Mose kuti,
17 Aucun de tes descendants dans tes générations, qui aura un défaut corporel, ne s'approchera pour présenter le pain de son Dieu;
“Muwuze Aaroni kuti, ‘Munthu aliyense mwa zidzukulu zake ku mibado yawo yonse ikubwera akakhala ndi chilema asabwere kudzapereka nsembe kwa Mulungu wake.
18 l'accès est interdit à tout homme affligé d'un défaut corporel, qui sera ou aveugle ou boiteux ou camus ou disproportionné,
Munthu aliyense wachilema motere: munthu wakhungu kapena wolumala miyendo, munthu wolumala nkhope kapena waziwalo zambiri,
19 ou qui aura une fracture à un pied ou à une main,
munthu wa phazi lolumala kapena dzanja lolumala,
20 ou qui sera bossu ou grêle, ou qui aura une tache blanche à l'œil, ou la gale ou la teigne, ou les testicules écrasés.
kapena munthu wokhota msana kapena wamfupi kwambiri, kapena wolumala maso, munthu wa nthenda yonyerenyetsa, kapena wamphere, kapenanso wophwanyika mavalo, sayenera kusendera pafupi.
21 Aucun des descendants du Prêtre Aaron, qui aura un défaut corporel, ne sera admis à offrir les sacrifices ignés à l'Éternel; il a un défaut, il ne saurait avoir accès pour présenter le pain de son Dieu.
Mdzukulu aliyense wa Aaroni wansembe, amene ali ndi chilema asadzayandikire kukapereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Popeza kuti ali ndi chilema, asayandikire kudzapereka nsembe ya chakudya kwa Mulungu wake.
22 Il pourra manger l'aliment de son Dieu, des choses sacro-saintes et des choses saintes.
Koma iye angathe kudya chakudya chopatulika kwambiri chija, ngakhalenso chakudya chotsala pa nsembe zopatulika.
23 Seulement il ne s'approchera ni du rideau, ni de l'Autel, parce qu'il a un défaut, afin qu'il ne profane pas mes Sanctuaires, car je suis l'Éternel qui les consacre.
Koma chifukwa cha kulumala kwake, sayenera kuyandikira katani kapena kufika pa guwa kuti angadetse malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.’”
24 Et Moïse parla à Aaron et à ses fils et à tous les enfants d'Israël.
Choncho Mose anawuza Aaroni ndi ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse zimenezi.

< Lévitique 21 >