< Lévitique 19 >
1 Et l'Éternel parla à Moïse en ces termes:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Parle à toute l'Assemblée des enfants d'Israël et dis-leur: Soyez saints, car je suis Saint, moi, l'Éternel, votre Dieu.
“Uza gulu lonse la Aisraeli kuti, ‘Khalani oyera mtima chifukwa Ine, Yehova Mulungu wanu, ndine Woyera.
3 Que chacun de vous respecte son père et sa mère et observez mes sabbats. Je suis l'Éternel, votre Dieu.
“‘Aliyense mwa inu azilemekeza abambo ake ndi amayi ake. Ndipo muzisunga masabata anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
4 Ne vous adressez point aux idoles et ne vous faites point de dieux de fonte. Je suis l'Éternel, votre Dieu.
“‘Musatembenukire ku mafano kapena kudzipangira nokha milungu ya zitsulo zosungunula. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
5 Et quand vous sacrifierez une victime pacifique à l'Éternel, vous l'offrirez de manière à être agréés.
“‘Pamene mukupereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, muyipereke mwanjira yoti ilandiridwe.
6 Et elle se mangera le jour du sacrifice et le lendemain, et ce qui sera resté jusqu'au troisième jour sera brûlé au feu.
Nsembe izidyedwa tsiku lomwe mwayiperekalo kapena mmawa mwake. Chilichonse chotsala mpaka tsiku lachitatu chiyenera kutenthedwa.
7 Et si on en mange le troisième jour, elle sera un objet de dégoût, et n'agréera point.
Ngati mudya choperekacho tsiku lachitatu, ndiye kuti mwachita chonyansa ndipo chakudyacho sichidzalandiridwa.
8 Et qui en mangera sera sous le poids de sa faute; car il aura profané ce qui est consacré à l'Éternel; et cette personne sera éliminée du sein de son peuple.
Munthu aliyense amene adya chakudyacho adzasenza machimo ake chifukwa wayipitsa chinthu chimene ndi choyera kwa Yehova. Munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.
9 Et quand vous récolterez les moissons de votre pays, tu ne moissonneras pas entièrement les angles de ton champ et ne ramasseras pas la glanure après ta moisson.
“‘Pamene mukolola zinthu mʼmunda mwanu musakolole mpaka mʼmphepete mwa munda, ndipo musatole khunkha lake.
10 Et tu ne grappilleras pas ta vigne et ne recueilleras pas les grains tombés de tes ceps; tu les abandonneras au pauvre et à l'étranger. Je suis l'Éternel, votre Dieu.
Musakolole mphesa zonse mʼmunda wanu wa mpesa kapena kutola mphesa zakugwa mʼmundamo. Zimenezi muzisiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wako.
11 Ne dérobez point, et n'employez ni mensonge ni fraude les uns envers les autres.
“‘Musabe. “‘Musamanamizane. “‘Musachitirane zinthu mwachinyengo.
12 Et ne faites point de faux serment en mon nom, car ce serait profaner le nom de ton Dieu. Je suis l'Éternel.
“‘Musalumbire mʼdzina langa monyenga popeza kutero ndi kuyipitsa dzina la Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
13 N'exerce sur ton prochain ni oppression ni rapine. Que le salaire du mercenaire ne séjourne pas chez toi jusqu'au matin.
“‘Musapsinje mnzanu kapena kumulanda zinthu zake. “‘Musasunge malipiro a munthu wantchito usiku wonse mpaka mmawa.
14 Ne maudis point le sourd, et ne place point d'achoppement devant l'aveugle, et aie la crainte de ton Dieu. Je suis l'Éternel.
“‘Musatemberere wosamva kapena kuyikira munthu wosaona chinthu choti apunthwe nacho patsogolo pake, koma muziopa Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
15 Ne prévariquez point en jugeant, et n'ayez ni partialité pour les petits, ni considération pour les grands: juge ton prochain selon la justice.
“‘Musamaweruze mopanda chilungamo. Musachite tsankho pakati pa osauka ndi olemera, koma muweruze mlandu wa mnzanu mwachilungamo.
16 Ne va point calomniant parmi tes concitoyens, et ne t'offre pas comme témoin contre la vie de ton prochain. Je suis l'Éternel.
“‘Musamapite uku ndi uku kunena bodza pakati pa anthu anu. “‘Musachite kanthu kalikonse kamene kangadzetse imfa kwa mnzanu. Ine ndine Yehova.
17 Ne hais point ton frère dans ton cœur, exprime tes griefs à ton prochain afin que, à cause de lui, tu ne te charges pas d'un péché.
“‘Musamude mʼbale wanu mu mtima mwanu. Koma mudzudzuleni mnzanu moona mtima kuti musakhale wolakwa.
18 Ne sois ni vindicatif ni rancunier envers les enfants de ton peuple, et aime ton prochain comme toi-même. Je suis l'Éternel.
“‘Musamubwezere mnzanu choyipa kapena kumusungira kanthu kunkhosi, koma konda mnansi wako monga iwe mwini. Ine ndine Yehova.
19 Observez mes statuts. Vous n'accouplerez point des bestiaux de deux espèces. Tu n'ensemenceras point ton champ de semences de deux espèces, et tu ne porteras point d'habits tissus de fils de deux espèces.
“‘Muzisunga malangizo anga. “‘Tsono musamalole kuti ngʼombe zanu zikwerane ndi chiweto cha mtundu wina. “‘Ndiponso musamadzale mbewu za mitundu iwiri mʼmunda umodzi. “‘Musavale chovala chopangidwa ndi nsalu za mitundu iwiri.
20 Si un homme a commerce avec une femme et que ce soit une fille fiancée à un autre, mais qui n'a pas été rachetée ni affranchie, il y aura châtiment; mais ils ne seront pas mis à mort, parce qu'elle n'est pas affranchie.
“‘Ngati munthu agonana ndi kapolo wamkazi amene wafunsidwa mbeta ndi munthu wina, koma sanawomboledwe kapenanso kulandira ufulu wake, alangidwe. Koma onsewa asaphedwe, chifukwa mkaziyo anali asanalandire ufulu wake.
21 Il amènera sa victime pour délit à l'Éternel à l'entrée de la Tente du Rendez-vous, un bélier comme victime pour délit.
Koma mwamunayo abwere ndi nsembe yopepesera kupalamula kwa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano. Nsembe yake ikhale nkhosa yayimuna
22 Et le Prêtre fera pour lui la propitiation avec le bélier, victime pour délit, devant l'Éternel, à cause du péché qu'il a commis, afin qu'il obtienne son pardon pour le péché qu'il a commis.
ndipo wansembe achite nayo mwambo wopepesera chifukwa cha kupalamula kumene anachita pamaso pa Yehova. Akatero tchimo lake lidzakhululukidwa.
23 Et quand vous serez entrés au pays et y aurez planté toute sorte d'arbres fruitiers, vous jetterez leur prépuce, leurs [premiers] fruits; pendant trois ans vous les tiendrez pour incirconcis, et vous ne vous en nourrirez pas;
“‘Mukadzalowa mʼdzikomo ndi kudzala mtengo wa mtundu uliwonse wa zipatso, zipatso zakezo mudzaziyese ngati zodetsedwa. Ndiye kuti kwa zaka zitatu zidzakhale zoletsedwa kwa inu. Musadzazidye nthawi imeneyi.
24 et la quatrième année tous leurs fruits seront saints et serviront aux fêtes de l'Éternel;
Chaka chachinayi, zipatso zake zonse zidzakhala zopatulika, ndipo zidzakhala chopereka cha matamando kwa Yehova.
25 mais la cinquième année vous en mangerez les fruits — pour en augmenter la récolte à votre profit. Je suis l'Éternel, votre Dieu.
Koma chaka chachisanu, mudzatha kudya zipatso zake kuti mitengoyo idzakubalireni zochuluka. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
26 Ne mangez rien avec du sang. Ne pratiquez point de charmes et ne tirez point d'augures.
“‘Musadye nyama ya magazi. “‘Musamawombeze kapena kuchita zamatsenga.
27 Ne tondez point en rond l'extrémité de votre chevelure, et ne rase point les coins de ta barbe.
“‘Musamamete mduliro kapena kumeta mʼmphepete mwa ndevu zanu.
28 Ne vous faites point d'incision sur le corps à propos d'un mort et ne vous marquez d'aucune inscription au poinçon. Je suis l'Éternel.
“‘Musadzichekecheke pathupi panu chifukwa cha munthu wakufa kapena kudzitema mphini pa thupi lanu. Ine ndine Yehova.
29 Ne profane point ta fille en la prostituant, afin que le pays ne se prostitue pas et ne se remplisse pas de crime.
“‘Musamuyipitse mwana wanu wamkazi pomusandutsa mkazi wachiwerewere. Mukatero dziko lidzasanduka la anthu achiwerewere ndi lodzaza ndi zoyipa.
30 Observez mes Sabbats et révérez mon Sanctuaire. Je suis l'Éternel.
“‘Muzisunga Masabata anga ndipo muzilemekeza malo anga opatulika. Ine ndine Yehova.
31 Ne vous adressez ni aux évocateurs, ni aux devins; ne les consultez pas afin de ne pas vous souiller avec eux. Je suis l'Éternel, votre Dieu.
“‘Musamapite kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kapena kwa owombeza. Musamawafunefune kuti angakuyipitseni. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
32 Lève-toi devant les cheveux blancs, et honore la personne du vieillard, et aie la crainte de ton Dieu. Je suis l'Éternel.
“‘Muzikhala mwa ulemu pamaso pa munthu wachikulire, ndipo muzichitira ulemu munthu wokalamba. Kumeneko ndiye kuopa Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
33 Si un étranger séjourne chez vous dans votre pays, ne l'opprimez pas;
“‘Pamene mlendo akhala nanu mʼdziko mwanu, musamuzunze.
34 traitez comme un indigène l'étranger qui séjourne chez vous, et aime-le comme toi-même, car vous fûtes étrangers dans le pays d'Egypte. Je suis l'Éternel, votre Dieu.
Mlendo amene akhala nanu akhale ngati mmodzi mwa mbadwa zanu. Mumukonde monga momwe mumadzikondera inu nomwe. Paja inu munali alendo mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
35 Ne commettez d'iniquité ni en jugeant, ni en prenant une dimension, ni en pesant, ni en mesurant;
“‘Musamachite za chinyengo poweruza mlandu, kapena poyeza utali, kulemera ngakhalenso kuchuluka kwa zinthu.
36 ayez une balance juste, et des poids justes, et un épha juste et un hin juste. Je suis l'Éternel, votre Dieu, qui vous ai tirés du pays d'Egypte.
Miyeso ya sikelo, miyeso yoyezera kulemera kwa zinthu, miyeso yotchedwa efa ndi miyeso yotchedwa hini zikhale zolungama. Ine ndine Yehova, Mulungu wanu amene ndinakutulutsani ku dziko la Igupto.
37 Observez ainsi tous mes statuts et toutes mes lois et pratiquez-les. Je suis l'Éternel.
“‘Choncho muzisunga malangizo ndi malamulo angawa ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.’”