< Jérémie 32 >

1 La parole qui fut adressée à Jérémie par l'Éternel, la dixième année de Sédécias, roi de Juda: c'était la dix-huitième année de Nébucadnézar.
Yehova anayankhula ndi Yeremiya mʼchaka chakhumi cha Zedekiya mfumu ya Yuda, chimene chinalinso chaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara.
2 Or l'armée du roi de Babel assiégeait alors Jérusalem, et Jérémie, le prophète, était enfermé dans le vestibule de la prison qui était dans la maison du roi de Juda,
Pa nthawi imeneyi nʼkuti ankhondo a mfumu ya ku Babuloni atazinga Yerusalemu, ndipo mneneri Yeremiya ndiye anamutsekera mʼbwalo la alonda mʼnyumba yaufumu ya ku Yuda.
3 où l'avait enfermé Sédécias, roi de Juda, en disant: Pourquoi prophétises-tu disant: « Ainsi parle l'Éternel: Voici, je vais livrer cette ville aux mains du roi de Babel, pour qu'il s'en empare,
Tsono Zedekiya mfumu ya Yuda nʼkuti itamutsekera mʼmenemo, ndipo inati, “Nʼchifukwa chiyani ukulosera motero? Iwe ukunena kuti, ‘Yehova akuti: Ndidzapereka mzinda uno kwa mfumu ya ku Babuloni, ndipo idzawulanda.
4 et Sédécias, roi de Juda, n'échappera pas aux mains des Chaldéens, mais il sera livré aux mains du roi de Babel, et il lui parlera bouche à bouche, et ses yeux rencontreront ses yeux;
Zedekiya mfumu ya Yuda sidzapulumuka mʼmanja mwa Ababuloni, koma idzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni. Adzayankhula naye ndi kuonana naye maso ndi maso.
5 et il conduira Sédécias à Babel, où il demeurera jusqu'à ce que je le visite, dit l'Éternel. Si vous vous battez contre les Chaldéens, vous n'aurez point de succès »?
Zedekiya adzatengedwa kupita naye ku Babuloni, kumene adzakhale mpaka nditamukhawulitsa, akutero Yehova. Ngakhale iye adzamenyane ndi Babuloni, koma sadzapambana.’”
6 Alors Jérémie dit: La parole de l'Éternel m'a été adressée en ces mots:
Yeremiya anati, “Yehova wandiwuza kuti:
7 Voici, Hanaméel, fils de Sallum ton oncle, s'approchera de toi pour te dire: Achète mon champ qui est à Anathoth, car tu as le droit de retrait pour le rachat.
Taonani, Hanameli mwana wa Salumu, amalume ako akubwera ndipo adzakuwuza kuti, ‘Gula munda wanga wa ku Anatoti, chifukwa iwe ndiwe mʼbale wanga ndipo ndiwe woyenera kuwuwombola.’”
8 Et Hanaméel, fils de mon oncle, s'approcha de moi selon la parole de l'Éternel, dans le vestibule de la prison, et me dit: Achète mon champ qui est à Anathoth, dans le pays de Benjamin, car tu as le droit de succession et de retrait; achète-le! Et je reconnus que c'était là la parole de l'Éternel.
Ndipo monga momwe Yehova ananenera, Hanameli, msuweni wanga anabweradi ku bwalo la alonda ndipo anati, “Gula munda wanga wa ku Anatoti mʼdziko la Benjamini. Popeza ndiwe woyenera kuwugula ndi kukhala wako, gula munda umenewu kuti ukhale wako.” “Ine ndinadziwa kuti amenewa anali mawu a Yehova aja;
9 Et j'achetai le champ de Hanaméel, fils de mon oncle, à Anathoth, et je lui pesai le prix, sept sicles [d'or], et dix sicles d'argent.
choncho ndinagula munda wa ku Anatoti kwa Hanameli msuweni wanga, ndipo ndinamupatsa masekeli asiliva 17.
10 Et je consignai cela dans une lettre que je scellai; et je pris des témoins, et je pesai l'argent à la balance.
Ndinasayina panganolo ndikulimata pamaso pa mboni, kenaka ndinayeza ndalama zasilivazo pa sikelo.”
11 Puis je pris la lettre d'achat, celle qui était scellée selon l'ordonnance et les statuts, et celle qui était ouverte;
Pambuyo pake ndinatenga makalata anga a pangano, imodzi yomatidwa mʼmene munali malamulo onse a panganolo ndi ina yosamatidwa.
12 et je remis la lettre d'achat à Baruch, fils de Nérija, fils de Mahaséïa, en présence de Hanaméel, mon parent, et en présence des témoins signataires de la lettre d'achat, et en présence de tous les Juifs assis dans le vestibule de la prison;
Ndinapereka makalatawo kwa Baruki mwana wa Neriya, mdzukulu wa Maseya pamaso pa Hanameli msuweni wanga, pamaso pa mboni zimene zinasayina panganoli ndiponso pamaso pa Ayuda onse okhala mʼbwalo la alonda.
13 et en leur présence je donnai cet ordre à Baruch:
“Ndinamulangiza Baruki pamaso pa onsewo kuti,
14 Ainsi parle l'Éternel des armées, Dieu d'Israël: Prends ces lettres, cette lettre d'achat scellée, et cette lettre ouverte, et mets-les dans un vase de terre, afin qu'elles se conservent longtemps.
‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Tenga makalata awa a umboni wapangano, iyi yokhala ndi chizindikiro ndi yopanda chizindikiro, uwasunge mʼmbiya kuti akhale nthawi yayitali.
15 Car ainsi parle l'Éternel des armées, Dieu d'Israël: Il sera encore acheté des maisons, et des champs, et des vignes dans ce pays-ci.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Anthu adzagulanso nyumba, minda ndi mitengo yamphesa mʼdziko lino.’”
16 Et je priai l'Éternel, après avoir remis la lettre d'achat à Baruch, fils de Nérija, disant:
Nditamupatsa makalata a panganowa Baruki mwana wa Neriya, ndinapemphera kwa Yehova:
17 Ah! Seigneur Éternel, voici, tu as formé les Cieux et la terre par ta grande force et ton bras étendu: rien n'est trop difficile pour toi.
“Aa, inu Ambuye Yehova, munalenga dziko lakumwamba ndi dziko lapansi. Munazilenga ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo palibe chokulakani.
18 Tu fais grâce à mille [générations] et tu fais retomber la peine du péché des pères dans le sein de leurs enfants après eux. Dieu grand et puissant, dont le nom est l'Éternel des armées,
Mumaonetsa chikondi chanu kwa anthu osawerengeka koma mumalanga ana chifukwa cha machimo a makolo awo. Inu ndinu Mulungu Wamkulu ndi Wamphamvu. Dzina lanu ndinu Yehova Wamphamvuzonse.
19 toi qui es grand en conseil et puissant en action, toi dont les yeux sont ouverts sur toutes les voies des enfants des hommes, pour rendre à chacun selon ses voies et selon le fruit de ses œuvres,
Zolinga zanu ndi zazikulu ndipo zochita zanu ndi zamphamvu. Maso anu amaona zonse zimene anthu amachita. Mumapereka mphotho kwa munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndi ntchito zake.
20 toi qui fis des signes et des miracles au pays d'Egypte jusqu'à ce jour, et pour Israël, et pour d'autres hommes, et qui t'es fait un nom tel qu'[il est] aujourd'hui;
Inu munachita zizindikiro zozizwitsa ku Igupto, ndipo mwakhala mukuzichita mpaka lero, pakati pa Aisraeli ndiponso pakati pa anthu onse. Choncho mwadzitchukitsa mpaka lero lino.
21 et qui tiras du pays d'Egypte ton peuple d'Israël, avec des signes et des miracles, et d'une main forte et d'un bras étendu, et avec une grande terreur,
Munatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu pochita zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene zinaopseza adani anu.
22 et qui leur donnas ce pays que tu avais juré à leurs pères de leur donner, pays découlant de lait et de miel;
Munawapatsa dziko lino limene munalonjeza mwalumbiro kulipereka kwa makolo awo, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
23 et ils sont venus et en ont pris possession; mais ils n'ont point obéi à ta voix, ni suivi ta loi, ne pratiquant point tout ce que tu leur avais commandé de faire; et tu as fait fondre sur eux toutes ces calamités!
Iwo analowa nʼkulitenga kukhala lawo, koma sanamvere Inu kapena kutsatira lamulo lanu; ndipo sanachite zomwe munawalamula. Choncho inu mwawagwetsera masautso onsewa.”
24 Voici, les terrasses atteignent déjà cette ville, en sorte qu'elle sera prise, puis livrée aux mains des Chaldéens qui lui sont hostiles, par l'épée et la famine et la peste; et ce que tu as dit arrive, et voici, tu en es témoin.
“Onani momwe adani azingira ndi mitumbira yankhondo mzindawu kuti awulande ndipo akuwuthira nkhondo. Chifukwa cha lupanga, njala ndi mliri. Mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni anthu atafowoka ndi nkhondo, njala ndi mliri. Zimene munkanena zija zachitikadi monga mukuzionera tsopano.
25 Et néanmoins tu m'as dit, Seigneur, Éternel: « Achète-toi un champ pour de l'argent, et prends des témoins; » et cette ville est livrée aux mains des Chaldéens!
Ngakhale mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni, komabe Inu Ambuye Yehova, munandiwuza kuti, ‘Gula munda ndi siliva ndipo upereke ndalamazo pali mboni.’”
26 Et la parole de l'Éternel fut adressée à Jérémie en ces mots:
Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti,
27 Voici, moi l'Éternel, je suis le Dieu de toute chair; y a-t-il rien de trop difficile pour moi?
“Taonani, Ine ndine Yehova, Mulungu wa anthu onse. Kodi chilipo chinthu choti Ine nʼkundikanika?
28 Aussi, ainsi parle l'Éternel: Voici, je livre cette ville aux mains des Chaldéens, et aux mains de Nébucadnézar, roi de Babel, pour qu'il s'en empare.
Nʼchifukwa chake ine Yehova ndikuti: Ndidzawupereka mzinda uno kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulanda.
29 Et les Chaldéens qui font la guerre à cette ville, vont arriver, et mettre le feu à cette ville, et la brûler, ainsi que les maisons sur les toits desquelles ils ont encensé Baal, et offert des libations à d'autres dieux, afin de me provoquer.
Ndipo Ababuloni amene akuwuthira nkhondo mzinda uno adzalowa ndi kuwutentha; adzatentha ndi kugwetsa nyumba zimene pa denga pake anthu ankandipsetsa mtima pofukiza lubani kwa Baala ndi popereka chopereka cha chakumwa kwa milungu ina.
30 Car les enfants d'Israël et les enfants de Juda n'ont fait que ce qui est mal à mes yeux dès leur jeunesse; car les enfants d'Israël n'ont fait que me provoquer par l'œuvre de leurs mains, dit l'Éternel,
“Aisraeli ndi Ayuda akhala akuchita zoyipa zokhazokha pamaso panga kuyambira ubwana wawo. Kunena zoona Aisraeli akumandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa, akutero Yehova.
31 car dans la colère et le courroux que cette ville me donne depuis le jour où elle fut bâtie, jusques aujourd'hui, j'ai résolu de l'ôter de ma vue,
Kuyambira tsiku limene mzindawu unamangidwa mpaka lero, wakhala ukuwutsa mkwiyo wanga ndi ukali wanga. Nʼchifukwa chake ndiyenera kuwuchotsa pamaso panga.
32 à cause de tout le mal qu'ont fait les enfants d'Israël et les enfants de Juda pour me provoquer, eux, leurs rois, leurs princes, leurs sacrificateurs et leurs prophètes, et les hommes de Juda et les habitants de Jérusalem.
Aisraeli ndi Ayuda, anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, mafumu awo, nduna zawo, ansembe ndi aneneri awo anandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa.
33 Et ils m'ont présenté le dos et non point le visage; dès le matin je les ai instruits et instruits; mais ils ne furent point dociles à recevoir la remontrance;
Anandifulatira ndipo ngakhale ndinakhala ndikuwaphunzitsa kawirikawiri, sanamve kapena kuphunzirapo kanthu.
34 et ils ont placé leurs abominations dans la maison appelée de mon nom pour la souiller,
Iwo anayika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi dzina langa ndipo anayipitsa.
35 et ils ont élevé des tertres à Baal dans la vallée des fils de Hinnom, pour offrir leurs fils et leurs filles à Moloch; ce que je n'avais point ordonné et qui ne m'était point venu dans la pensée, qu'on fît de telles horreurs pour porter Juda à pécher.
Anamanga malo opembedzerapo Baala mʼChigwa cha Hinomu kuti aziperekapo ana awo aamuna ndi aakazi ngati nsembe kwa Moleki. Ine sindinawalamulire kutero, ndipo sindinaganizepo nʼkomwe kuti iwo angachite chinthu chonyansa chotero, ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda.
36 Et maintenant, ainsi prononce cependant l'Éternel, Dieu d'Israël, sur cette ville dont vous dites: Elle sera livrée aux mains du roi de Babel par l'épée et la famine et la peste:
“Anthu ponena za mzindawu akuti udzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni mwa nkhondo, njala ndi mliri, koma Yehova Mulungu wa Israeli akuti,
37 Voici, je les recueillerai de tous les pays où je les aurai dispersés dans ma colère, et dans ma fureur, et dans mon grand courroux, et je les ferai revenir en ce lieu et habiter en sécurité,
Ine ndidzawasonkhanitsadi anthuwa kuchokera ku mayiko onse kumene ndinawapirikitsira ndili wokwiya ndi waukali kwambiri. Ndidzabwera nawo ku malo ano ndipo ndidzawalola kukhala mwamtendere.
38 et ils seront mon peuple, et je serai leur Dieu;
Iwo adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
39 et je leur donnerai un seul cœur et une seule voie pour me craindre toujours, afin d'être heureux, eux et leurs enfants après eux.
Ndidzawapatsa mtima umodzi ndi khalidwe limodzi kotero kuti azidzandiopa nthawi zonse ndipo iwo pamodzi ndi zidzukulu zawo zinthu zidzawayendera bwino.
40 Et je leur donne cette alliance éternelle, que je ne cesserai de leur faire du bien, et je mettrai ma crainte dans leurs cœurs, afin qu'ils ne s'éloignent pas de moi.
Ndidzachita nawo pangano losatha: sindidzaleka kuwachitira zabwino, ndipo ndidzawapatsa mtima woti azidzandiopa, kuti asadzandisiyenso.
41 Et ma joie à leur égard sera de leur faire du bien, et je les planterai dans ce pays, véritablement, de tout mon cœur et de toute mon âme.
Ndidzakondwera powachitira zabwino, ndipo ndidzawakhazikitsa ndithu mʼdziko lino ndi mtima wanga wonse ndi moyo wanga wonse.
42 Car ainsi parle l'Éternel: De même que j'ai fait venir sur ce peuple tous ces grands maux, de même je ferai venir sur eux tous les biens que je leur ai promis;
“Yehova akuti: Monga momwe ndinagwetsera masautso aakulu onsewa pa anthuwa, momwemonso ndidzawapatsa zinthu zonse zabwino zimene ndinawalonjeza.
43 et des champs seront achetés dans ce pays duquel vous dites: « C'est un désert sans hommes ni bestiaux, il est livré aux mains des Chaldéens; »
Adzagulanso minda mʼdziko muno, limene inu mukuti, ‘Ndi dziko losiyidwa, lopanda anthu kapena nyama, pakuti linaperekedwa kwa Ababuloni.’
44 on achètera des champs pour de l'argent, les lettres en seront écrites et scellées, munies du témoignage des témoins, dans le pays de Benjamin, et dans les alentours de Jérusalem, et dans les villes de Juda, et dans les villes de la montagne, et dans les villes du bas-pays, et dans les villes du Midi; car je ramènerai leurs captifs, dit l'Éternel.
Adzagula minda ndi ndalama zasiliva, ndipo achita pangano, ndi kumata pamaso pa mboni. Izi zidzachitika mʼdziko la Benjamini, ku malo ozungulira Yerusalemu, mʼmizinda ya Yuda, mʼmizinda ya ku mapiri, mʼmizinda ya kuchigwa ndi yakummwera ku Negevi. Zoona, ndidzabwezera ufulu wawo, akutero Yehova.”

< Jérémie 32 >