< Proverbes 4 >
1 Écoutez, mes fils, l’instruction d’un père, Et soyez attentifs, pour connaître la sagesse;
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Car je vous donne de bons conseils: Ne rejetez pas mon enseignement.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 J’étais un fils pour mon père, Un fils tendre et unique auprès de ma mère.
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 Il m’instruisait alors, et il me disait: Que ton cœur retienne mes paroles; Observe mes préceptes, et tu vivras.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Acquiers la sagesse, acquiers l’intelligence; N’oublie pas les paroles de ma bouche, et ne t’en détourne pas.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Ne l’abandonne pas, et elle te gardera; Aime-la, et elle te protégera.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Voici le commencement de la sagesse: Acquiers la sagesse, Et avec tout ce que tu possèdes acquiers l’intelligence.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Exalte-la, et elle t’élèvera; Elle fera ta gloire, si tu l’embrasses;
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Elle mettra sur ta tête une couronne de grâce, Elle t’ornera d’un magnifique diadème.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Écoute, mon fils, et reçois mes paroles; Et les années de ta vie se multiplieront.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Je te montre la voie de la sagesse, Je te conduis dans les sentiers de la droiture.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Si tu marches, ton pas ne sera point gêné; Et si tu cours, tu ne chancelleras point.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Retiens l’instruction, ne t’en dessaisis pas; Garde-la, car elle est ta vie.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 N’entre pas dans le sentier des méchants, Et ne marche pas dans la voie des hommes mauvais.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Évite-la, n’y passe point; Détourne-t’en, et passe outre.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Car ils ne dormiraient pas s’ils n’avaient fait le mal, Le sommeil leur serait ravi s’ils n’avaient fait tomber personne;
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Car c’est le pain de la méchanceté qu’ils mangent, C’est le vin de la violence qu’ils boivent.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Le sentier des justes est comme la lumière resplendissante, Dont l’éclat va croissant jusqu’au milieu du jour.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 La voie des méchants est comme les ténèbres; Ils n’aperçoivent pas ce qui les fera tomber.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Mon fils, sois attentif à mes paroles, Prête l’oreille à mes discours.
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 Qu’ils ne s’éloignent pas de tes yeux; Garde-les dans le fond de ton cœur;
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Car c’est la vie pour ceux qui les trouvent, C’est la santé pour tout leur corps.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Garde ton cœur plus que toute autre chose, Car de lui viennent les sources de la vie.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Écarte de ta bouche la fausseté, Éloigne de tes lèvres les détours.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Que tes yeux regardent en face, Et que tes paupières se dirigent devant toi.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Considère le chemin par où tu passes, Et que toutes tes voies soient bien réglées;
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 N’incline ni à droite ni à gauche, Et détourne ton pied du mal.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.